< 2 Mafumu 16 >
1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
I Pekas, Remaljas Søns, syttende Regeringsår blev Akaz, Jotams Søn, Konge over Juda.
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
Akaz var tyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede seksten År i Jerusalem. Han gjorde ikke, hvad der var ret i HERREN hans Guds Øjne, som hans Fader David,
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
men vandrede i Israels Kongers Spor. Ja, han lod endog sin Søn gå igennem Ilden efter de Folks vederstyggelige Skik, som HERREN havde drevet bort foran Israeliterne.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Han ofrede og tændte Offerild på Offerhøjene og de høje Steder og under alle grønne Træer.
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
På den Tid drog Kong Aezin af Aram og Remaljas Søn, Kong Peka af Israel, op for at angribe Jerusalem; og de indesluttede Akaz, men var ikke stærke nok til at angribe.
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
Ved den Lejlighed tog Edoms Konge; Elat tilbage til Edom; og efter at han havde jaget Judæerne ud af Elat, kom Edomiterne og bosatte sig der, og de bor der den Dag i Dag.
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
Men Akaz sendte Sendebud til Assyrerkongen Tiglat-Pileser og lod sige: "Jeg er din Træl og din Søn! Kom op og frels mig fra Arams og Israels Konger, som angriber mig!"
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
Tillige tog Akaz det Sølv og Guld, der fandtes i HERRENs Hus og Skat Kammeret i Kongens Palads, og sendte det som Gave til Assyrerkongen.
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
Assyrerkongen opfyldte hans Ønske og drog op mod Damaskus og indtog det; Indbyggerne førte han bort til Kir, og Rezin lod han dræbe.
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
Da Kong Akaz var draget op til Damaskus for at mødes med Assyrerkongen Tiglat-Pileser, så han Alteret i Damaskus, og Kong Akaz sendte Alterets Mål og en Tegning af det i alle Enkeltheder til Præsten Urija.
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
Og Præsten Urija byggede Alteret; i nøje Overensstemmelse med den Vejledning, Kong Akaz havde sendt fra Damaskus, udførte Præsten Urija det, før Kong Akaz kom hjem fra Damaskus.
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
Da Kongen kom hjem fra Damaskus og så Alteret, trådte han hen og steg op derpå;
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
og han ofrede sit Brændoffer og Afgrødeoffer, udgød sit Drikoffer og sprængte Blodet af sine Takofre på Alteret.
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
Men Kobberalteret, der stod for HERRENs Åsyn, fjernede han fra dets Plads foran Templet mellem Alteret og HERRENS Hus og flyttede det hen til Nordsiden af Alteret.
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
Derpå bød Kong Akaz Præsten Urija: "På det store Alter skal du ofre Morgenbrændofrene og Aftenafgrødeofrene, Kongens Brændofre og Afgrødeofre og Brændofrene fra alt Landets Folk såvel som deres Afgrødeofre og Drikofre og sprænge alt Blodet fra Brændofrene og Slagtofrene derpå. Hvad der skal gøres ved Kobberalteret, vil jeg tænke over."
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
Og Præsten Urija gjorde ganske som Kong Akaz bød.
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
Fremdeles lod Kong Aka Mellemstykkerne bryde af Stellene og Bækkenerne tage ned af dem; ligeledes lod han Havet løfte ned fra Kobberokserne, som har det, og opstille på Stenfliser;
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
den overdækkede Sabbatsgang, man havde bygget i Templet, og den kongelige Indgang udenfor lod han fjerne fra HERRENs Hus for Assyrerkongens Skyld.
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Hvad der ellers er at fortælle om Akaz, alt, hvad han udførte. står jo optegnet i Judas Kongers Krønike.
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Så lagde Akaz sig til Hvile hos sine Fædre og blev jordet hos sine Fædre i Davidsbyen; og hans Søn Ezekias blev Konge i hans Sted.