< 2 Mafumu 16 >

1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
Idet syttende Pekas, Remalias Søns, Aar blev Akas, en Søn af Judas Konge Jotham, Konge.
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
Akas var tyve Aar gammel, der han blev Konge, og regerede i seksten Aar i Jerusalem, og han gjorde ikke det, som var ret for Herrens, hans Guds, Øjne, som David, hans Fader,
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
men han vandrede i Israels Kongers Vej; tilmed lod han sin Søn gaa igennem Ilden efter de Hedningers Vederstyggeligheder, hvilke Herren havde fordrevet for Israels Børns Ansigt.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Han ofrede ogsaa og gjorde Røgelse paa de høje Steder og paa Højene og under alle grønne Træer.
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
Da drog Rezin, Kongen af Syrien, og Peka, Remalias Søn, Kongen i Israel, op imod Jerusalem til Krig og belejrede Akas, men de kunde ikke komme til at stride.
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
Paa den samme Tid bragte Rezin, Kongen af Syrien, Elath igen til Syrien og fordrev Jøderne af Elath, og Syrerne kom til Elath og boede der indtil denne Dag.
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
Saa sendte Akas Bud til Thiglath-Pileser, Kongen af Assyrien, og lod sige: Jeg er din Tjener og din Søn, kom op og frels mig af Syriens Konges Haand, og af Israels Konges Haand, hvilke have oprejst sig imod mig.
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
Og Akas tog det Sølv og det Guld, som fandtes i Herrens Hus og i Kongens Hus's Skatkammer og sendte Kongen af Assyrien det til Skænk.
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
Og Kongen af Assyrien adlød ham, og Kongen af Assyrien drog op til Damaskus og indtog den og førte dem bort til Kir, og han dræbte Rezin.
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
Da drog Kong Akas hen til Damaskus at møde Thiglath-Pileser, Kongen af Assyrien, og han saa det Alter, som var i Damaskus; da sendte Kong Akas en Afbildning af Alteret og en Lignelse af det, efter alt dets Arbejde, til Præsten Uria.
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
Og Præsten Uria byggede et Alter; efter alt som Kong Akas sendte fra Damaskus, saa gjorde Præsten Uria, indtil Kong Akas kom fra Damaskus.
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
Og der Kongen kom fra Damaskus, da saa Kongen Alteret, og Kongen nærmede sig Alteret og ofrede paa det.
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
Og han gjorde Røgofre af sit Brændoffer og sit Madoffer og udøste sit Drikoffer, og han stænkede Takofrenes Blod, som han havde, paa Alteret.
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
Men Kobberalteret, som stod for Herrens Ansigt, flyttede han længere bort fra Huset, at det ikke skulde staa imellem Alteret og imellem Herrens Hus; og han satte det op ved Siden af Alteret imod Norden.
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
Og Kong Akas bød Præsten Uria og sagde: Gør Røgoffer paa det store Alter af Brændofferet om Morgenen og Madofferet om Aftenen og af Kongens Brændoffer og hans Madoffer og af alt Folkets Brændoffer i Landet og deres Madoffer og deres Drikofre, og alt Brændofferets Blod og alt Slagtofferets Blod skal du stænke derpaa; men Kobberalteret skal være mig til at adspørge ved.
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
Og Præsten Uria gjorde efter alt det, som Kong Akas befalede.
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
Og Kong Akas afbrød Fyldingerne af Stolene og borttog Kedelen af dem, og Havet tog han ned af de Kobberøksne, som vare derunder, og han satte det paa et Stengulv,
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
og den bedækkede Sabbatsgang, som de havde hygget ved Huset, og den ydre Opgang for Kongen vendte han indad imod Herrens Hus, for Kongen af Assyriens Skyld.
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Men det øvrige af Akas's Handeler, og hvad han gjorde, ere de Ting ikke skrevne i Judas Kongers Krønikers Bog?
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Og Akas laa med sine Fædre og blev begraven hos sine Fædre i Davids Stad, og Ezekias, hans Søn, blev Konge i hans Sted.

< 2 Mafumu 16 >