< 2 Mafumu 14 >

1 Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
Amasías, hijo de Joás, llegó a ser rey de Judá en el segundo año del reinado de Joás, hijo de Joacaz, rey de Israel.
2 Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
Tenía veinticinco años cuando llegó a ser rey, y reinó en Jerusalén durante veintinueve años. Su madre se llamaba Joadán de Jerusalén.
3 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
Hizo lo que era correcto a los ojos del Señor, pero no de la misma manera que su antepasado David. Hizo todo como lo había hecho su padre Joás.
4 Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
Pero los altares paganos no fueron destruidos. El pueblo seguía sacrificando y presentando holocaustos en esos lugares.
5 Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
Una vez que estuvo seguro en el trono, ejecutó a los funcionarios que habían asesinado a su padre el rey.
6 Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
Pero no ejecutó a los hijos de los asesinos, siguiendo el mandato del Señor en la ley de Moisés: “Los padres no deben morir por los pecados de sus hijos, ni los hijos deben morir por los pecados de sus padres. Cada uno debe morir por su propio pecado”.
7 Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
Amasías mató a diez mil edomitas en el Valle de la Sal. Atacó y capturó Sela y la rebautizó como Joktheel, que es como se llama hasta hoy.
8 Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
Amasías envió mensajeros al rey de Israel, Joás, hijo de Joacaz, hijo de Jehú, diciéndole: “Luchemos, cara a cara!”
9 Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
Joás, rey de Israel, respondió a Amasías, rey de Judá: “En el Líbano, un cardo envió un mensaje a un cedro, diciendo: ‘Dale tu hija como esposa a mi hijo’. Pero pasó un animal salvaje del Líbano y pisoteó el cardo.
10 Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
Puede que hayas derrotado a Edom. Ahora te has vuelto arrogante. Quédate en casa y disfruta de tu victoria. ¿Por qué provocar problemas que te harán caer a ti, y a Judá contigo?”
11 Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
Pero Amasías se negó a escuchar, así que Joás, rey de Israel, vino a atacarlo. Él y Amasías, rey de Judá, se encontraron cara a cara en Bet Semes, en Judá.
12 Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
El ejército de Judá fue derrotado por Israel y huyó a su casa.
13 Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
Joás, rey de Israel, capturó a Amasías, rey de Judá, hijo de Joás, hijo de Ocozías, en Bet Semes. Entonces Joás atacó Jerusalén y derribó la muralla de la ciudad desde la puerta de Efraín hasta la puerta de la Esquina, de unos cuatrocientos codos de longitud.
14 Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
Se llevó todo el oro y la plata, y todos los objetos que se encontraban en el Templo del Señor y en los tesoros del palacio real, y también algunos rehenes. Luego regresó a Samaria.
15 Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
El resto de lo que sucedió en el reinado de Joás, todo lo que hizo y sus grandes logros y su guerra con Amasías, rey de Judá, están registrados en el Libro de las Crónicas de los Reyes de Israel.
16 Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
Joás murió y fue enterrado en Samaria con los reyes de Israel. Su hijo Jeroboam le sucedió como rey.
17 Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
Amasías, hijo de Joás, rey de Judá, vivió quince años más después de la muerte de Joás, hijo de Joacaz, rey de Israel.
18 Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
El resto de los acontecimientos que ocurrieron en el reinado de Amasías están registrados en el Libro de las Crónicas de los Reyes de Judá.
19 Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
Una conspiración contra Amasías tuvo lugar en Jerusalén, y él huyó a Laquis. Pero se enviaron hombres tras él y lo asesinaron allí.
20 Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
Lo trajeron de vuelta a caballo y lo enterraron en Jerusalén con sus antepasados en la Ciudad de David.
21 Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
Entonces todo el pueblo de Judá nombró rey al hijo de Amasías, Azarías, para que reemplazara a su padre. Azarías tenía dieciséis años.
22 Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
Azarías reconquistó Elat para Judá y la reconstruyó después de la muerte de su padre.
23 Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
Jeroboam, hijo de Joás, llegó a ser rey de Israel en el año quince del reinado de Amasías, hijo de Joás, rey de Judá. Reinó en Samaria durante cuarenta y un años.
24 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
Hizo lo malo a los ojos del Señor y no puso fin a todos los pecados que Jeroboam, hijo de Nabat, había hecho cometer a Israel.
25 Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
Restituyó la frontera de Israel a donde estaba, desde Lebó-Jamat hasta el Mar de la Arabá, como el Señor, el Dios de Israel, había dicho por medio de su siervo Jonás, hijo de Amitai, el profeta, que venía de Gat-Jefer.
26 Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
El Señor había visto lo mucho que estaban sufriendo los israelitas, tanto los esclavos como los libres. Nadie estaba allí para ayudar a Israel.
27 Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
Sin embargo, como el Señor había dicho que no eliminaría a Israel, lo salvó por medio de Jeroboam, hijo de Joás.
28 Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
El resto de lo que sucedió en el reinado de Jeroboam, todo lo que hizo, sus grandes logros y las batallas que libró, y cómo recuperó para Israel tanto Damasco como Jamat, están registrados en el Libro de las Crónicas de los Reyes de Israel.
29 Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Jeroboam murió y fue enterrado con los reyes de Israel. Su hijo Zacarías le sucedió como rey.

< 2 Mafumu 14 >