< 2 Mafumu 12 >

1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
İsrail Kralı Yehu'nun krallığının yedinci yılında Yoaş Yahuda Kralı oldu. Yedi yaşında kral oldu ve Yeruşalim'de kırk yıl krallık yaptı. Annesi Beer-Şevalı Sivya'ydı.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
Yoaş Kâhin Yehoyada yaşadığı sürece RAB'bin gözünde doğru olanı yaptı. Çünkü Kâhin Yehoyada ona yol gösteriyordu.
3 Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
Ancak alışılagelen tapınma yerleri henüz kaldırılmamıştı ve halk oralarda hâlâ kurban kesip buhur yakıyordu.
4 Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
Yoaş kâhinlere şöyle dedi: “RAB'bin Tapınağı için yapılan bağışları: Nüfus sayımından elde edilen geliri, kişi başına düşen vergiyi ve halkın gönüllü olarak RAB'bin Tapınağı'na sunduğu paraları toplayın.
5 Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
Her kâhin bunları hazine görevlilerinden alsın. Tapınağın neresinde yıkık bir yer varsa, onarılsın.”
6 Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
Yoaş'ın krallığının yirmi üçüncü yılında kâhinler tapınağı hâlâ onarmamışlardı.
7 Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
Bunun üzerine Kral Yoaş, Kâhin Yehoyada ile öbür kâhinleri çağırıp, “Neden RAB'bin Tapınağı'nı onarmıyorsunuz?” diye sordu, “Hazine görevlilerinden artık para almayın. Aldığınız paraları da RAB'bin Tapınağı'nın onarımına devredin.”
8 Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
Böylece kâhinler halktan para toplamamayı ve tapınağın onarım işlerine karışmamayı kabul ettiler.
9 Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
Kâhin Yehoyada bir sandık aldı. Kapağına bir delik açıp sunağın yanına, RAB'bin Tapınağı'na girenlerin sağına yerleştirdi. Kapıda görevli kâhinler RAB'bin Tapınağı'na getirilen bütün paraları sandığa atıyorlardı.
10 Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
Sandıkta çok para biriktiğini görünce kralın yazmanıyla başkâhin RAB'bin Tapınağı'na getirilen paraları sayıp torbalara koyarlardı.
11 Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
Sayılan paralar RAB'bin Tapınağı'ndaki işlerin başında bulunan adamlara verilirdi. Onlar da paraları RAB'bin Tapınağı'nda çalışan marangozlara, yapıcılara,
12 amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
duvarcılara, taşçılara öder, tapınağı onarmak için kereste ve yontma taş alımında kullanır ve onarım için gereken öbür malzemelere harcarlardı.
13 Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
RAB'bin Tapınağı'nda toplanan paralar, tapınak için gümüş tas, fitil maşaları, çanak, borazan, altın ya da gümüş eşya yapımında kullanılmadı.
14 Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
Bu para yalnız işçilere ödendi ve tapınağın onarımına harcandı.
15 Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
Tapınakta çalışanlara para ödemekle görevli kişiler öyle dürüst insanlardı ki, onlara hesap bile sorulmazdı.
16 Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
Suç ve günah sunusu olarak verilen paralarsa RAB'bin Tapınağı'na getirilmezdi; bunlar kâhinlere aitti.
17 Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
O sırada Aram Kralı Hazael, Gat Kenti'ne saldırıp kenti ele geçirdi. Sonra Yeruşalim'e saldırmaya karar verdi.
18 Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
Yahuda Kralı Yoaş, ataları olan öbür Yahuda krallarından Yehoşafat'ın, Yehoram'ın, Ahazya'nın ve kendisinin RAB'be adamış olduğu bütün kutsal armağanları, RAB'bin Tapınağı'nda ve sarayın hazinelerinde bulunan bütün altınları Aram Kralı Hazael'e gönderdi. Bunun üzerine Hazael Yeruşalim'e saldırmaktan vazgeçti.
19 Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Yoaş'ın krallığı dönemindeki öteki olaylar ve bütün yaptıkları Yahuda krallarının tarihinde yazılıdır.
20 Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
Kral Yoaş'ın görevlileri düzen kurup onu Silla'ya inen yolda, Beytmillo'da öldürdüler.
21 Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Yoaş'ı öldürenler, görevlilerinden Şimat oğlu Yozakar'la Şomer oğlu Yehozavat'tı. Yoaş Davut Kenti'nde atalarının yanına gömüldü. Yerine oğlu Amatsya kral oldu.

< 2 Mafumu 12 >