< 2 Mafumu 12 >
1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
Jehoash começou a reinar no sétimo ano de Jehu, e ele reinou quarenta anos em Jerusalém. O nome de sua mãe era Zíbia de Berseba.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
Jehoash fez o que estava certo aos olhos de Iavé todos os seus dias em que Jehoiada, o sacerdote, o instruiu.
3 Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
However, os lugares altos não lhe foram tirados. O povo ainda sacrificava e queimava incenso nos lugares altos.
4 Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
Jehoash disse aos sacerdotes: “Todo o dinheiro das coisas sagradas que é trazido à casa de Iavé, em dinheiro corrente, o dinheiro do povo para quem cada homem é avaliado, e todo o dinheiro que entra no coração de qualquer homem para trazer à casa de Iavé,
5 Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
deixe os sacerdotes levá-lo a eles, cada homem de seu doador; e eles repararão os danos à casa, onde quer que se encontre algum dano”.
6 Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
Mas foi assim, que no vigésimo terceiro ano do rei Jehoash os padres não haviam reparado os danos da casa.
7 Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
Então o rei Jehoash chamou o sacerdote Jehoiada e os outros sacerdotes, e disse-lhes: “Por que vocês não estão reparando os danos da casa? Agora, portanto, não aceitem mais dinheiro de seus tesoureiros, mas entreguem-no para reparar os danos à casa”.
8 Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
Os padres consentiram que não aceitassem mais dinheiro do povo, e que não reparassem os danos à casa.
9 Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
Mas Jehoiada o padre pegou uma arca e fez um buraco em sua tampa, e a colocou ao lado do altar, do lado direito, ao entrar na casa de Yahweh; e os padres que mantiveram o limiar colocaram todo o dinheiro que foi trazido para a casa de Yahweh dentro dela.
10 Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
Quando viram que havia muito dinheiro na arca, o escriba do rei e o sumo sacerdote subiram, colocaram-no em sacos e contaram o dinheiro que foi encontrado na casa de Yahweh.
11 Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
Eles deram o dinheiro que foi pesado nas mãos daqueles que fizeram o trabalho, que tinham a supervisão da casa de Iavé; e o pagaram aos carpinteiros e construtores que trabalharam na casa de Iavé,
12 amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
e aos pedreiros e cortadores de pedra, e para comprar madeira e pedra cortada para reparar os danos à casa de Iavé, e por tudo o que foi disposto para que a casa a reparasse.
13 Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
Mas não foram feitos para a casa de Iavé copos de prata, rapé, bacias, trombetas, quaisquer vasos de ouro ou vasos de prata, do dinheiro que foi trazido para a casa de Iavé;
14 Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
pois eles deram isso para aqueles que fizeram o trabalho, e repararam a casa de Iavé com ele.
15 Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
Moreover eles não exigiram uma contabilidade dos homens em cujas mãos entregaram o dinheiro para dar àqueles que fizeram o trabalho; pois eles lidaram fielmente.
16 Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
O dinheiro para as ofertas de transgressão e o dinheiro para as ofertas pelo pecado não foi trazido para a casa de Yahweh. Era dos sacerdotes.
17 Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
Então Hazael, rei da Síria, subiu e lutou contra Gate, e tomou-a; e Hazael preparou seu rosto para subir a Jerusalém.
18 Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
Jehoash rei de Judá tomou todas as coisas sagradas que Jeosafá e Jeorão e Acazias, seus pais, reis de Judá, tinham dedicado, e suas próprias coisas sagradas, e todo o ouro que foi encontrado nos tesouros da casa de Javé, e da casa do rei, e o enviou a Hazael, rei da Síria; e ele foi embora de Jerusalém.
19 Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Now o resto dos atos de Joás, e tudo o que ele fez, não estão escritos no livro das crônicas dos reis de Judá?
20 Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
seus servos se levantaram e fizeram uma conspiração, e atingiram Joás na casa de Millo, no caminho que desce até Silla.
21 Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Pois Jozacar, filho de Shimeath, e Jehozabad, filho de Shomer, seus servos, o atingiram e ele morreu; e o enterraram com seus pais na cidade de David; e Amaziah, seu filho, reinou em seu lugar.