< 2 Mafumu 12 >

1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
La septième année de Jéhu, Joas commença à régner, et il régna quarante ans à Jérusalem; sa mère avait nom Tsibja, [et] elle était de Béer-sebah.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
Joas fit ce qui est droit devant l'Eternel pendant tout le temps que Jéhojadah le Sacrificateur l'enseigna.
3 Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
Toutefois les hauts lieux ne furent point ôtés, le peuple sacrifiait encore et faisait des encensements dans les hauts lieux.
4 Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
Et Joas dit aux Sacrificateurs: Quant à tout l'argent consacré que l'on apporte dans la maison de l'Eternel, soit l'argent de tout homme qui passe par le dénombrement, soit l'argent des personnes selon l'estimation qu'en fait le Sacrificateur, [et] tout l'argent que chacun apporte volontairement dans la maison de l'Eternel;
5 Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
Que les Sacrificateurs le prennent par-devers eux, chacun de celui qu'il connaît, et qu'ils en réparent ce qui est à réparer du Temple, partout où l'on trouvera quelque chose à réparer.
6 Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
Mais il arriva que la vingt et troisième année du Roi Joas, les Sacrificateurs n'avaient point encore réparé ce qui était à réparer au Temple.
7 Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
Et le Roi Joas appela le Sacrificateur Jéhojadah, et les autres Sacrificateurs, et il leur dit: Pourquoi n'avez-vous pas réparé ce qui était à réparer au Temple? or maintenant ne prenez plus d'argent de ceux que vous connaissez, mais laissez-le pour ce qui est à réparer au Temple.
8 Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
Et les Sacrificateurs s'accordèrent à ne prendre plus l'argent du peuple, et à ne réparer point ce qui était à réparer au Temple.
9 Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
C'est pourquoi le Sacrificateur Jéhojadah prit un coffre, et fit un trou à son couvercle, et le mit auprès de l'autel à main droite, à l'endroit par où l'on entrait dans la maison de l'Eternel; et les Sacrificateurs qui gardaient les vaisseaux, mettaient là tout l'argent qu'on apportait à la maison de l'Eternel.
10 Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
Et dès qu'ils voyaient qu'il y avait beaucoup d'argent au coffre, le Secrétaire du Roi montait avec le grand Sacrificateur, et ils mettaient dans des sacs l'argent qui se trouvait dans la maison de l'Eternel, puis ils le comptaient.
11 Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
Et ils délivraient cet argent bien compté entre les mains de ceux qui avaient la charge de l'œuvre, [et] qui étaient commis sur la maison de l'Eternel, lesquels le distribuaient aux charpentiers et architectes qui refaisaient la maison de l'Eternel.
12 amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
Et aux maçons, et aux tailleurs de pierres, pour acheter du bois et des pierres de taille, afin de réparer ce qui était à réparer dans la maison de l'Eternel, et [pour acheter] tout ce qu'il fallait employer pour la réparation du Temple.
13 Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
Au reste, de cet argent qu'on apportait dans la maison de l'Eternel, on n'en faisait point de coupes d'argent, pour la maison de l'Eternel, ni de serpes, ni de bassins, ni de trompettes, ni aucun autre vaisseau d'or, ou vaisseau d'argent;
14 Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
Mais on le distribuait à ceux qui avaient la charge de l'œuvre, lesquels en réparaient la maison de l'Eternel.
15 Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
Et on ne faisait point rendre compte à ceux entre les mains de qui on avait délivré cet argent pour le distribuer à ceux qui faisaient le travail; car ils [le] faisaient fidèlement.
16 Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
L'argent [des sacrifices] pour le délit, et l'argent [des sacrifices] pour les péchés n'était point apporté dans la maison de l'Eternel; [car] il était aux Sacrificateurs.
17 Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
Alors Hazaël Roi de Syrie monta, et fit la guerre contre Gath, et la prit; puis Hazaël tourna visage pour monter contre Jérusalem.
18 Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
Mais Joas Roi de Juda prit tout ce qui était consacré, que Josaphat, Joram, et Achazia ses pères, Rois de Juda, avaient consacré, et tout ce que lui-même avait consacré, et tout l'or qui se trouva dans les trésors de la maison de l'Eternel et de la maison du Roi, et l'envoya à Hazaël Roi de Syrie, qui se retira de devant Jérusalem.
19 Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Le reste des faits de Joas, tout ce, dis-je, qu'il a fait, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois de Juda?
20 Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
r ses serviteurs se soulevèrent, et se liguèrent, et frappèrent Joas dans la maison de Millo, qui est à la descente de Silla.
21 Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Jozacar fils de Simhath, et Jozabad fils de Somer ses serviteurs le frappèrent, et il mourut; et on l'ensevelit avec ses pères dans la Cité de David; et Amatsia son fils régna en sa place.

< 2 Mafumu 12 >