< 2 Mafumu 11 >

1 Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
Cuando Atalía, la madre de Ocozías, vio que su hijo estaba muerto, ella hizo que todo el resto de la simiente del reino fuera muerto.
2 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
Más Josaba, la hija del rey Joram, hermana de Ocozías, tomó en secreto a Joás, hijo de Ocozías, con la mujer que lo cuidaba, lejos de entre los hijos del rey que fueron ejecutados, y él y la nodriza se escondieron en el dormitorio; y lo mantuvieron a salvo de Atalía, para que no fuera condenado a muerte.
3 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
Y por seis años lo mantuvo a salvo en la casa del Señor, mientras Atalía estaba gobernando la tierra.
4 Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
Luego, en el séptimo año, Joiada mandó llamar a los capitanes de cientos de cereteos hombres armados, y llevándolos a la casa del Señor, hizo un acuerdo con ellos y les hizo prestar juramento la casa del Señor, y les mostró al hijo del rey.
5 Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
Y les dio órdenes, diciendo: Esto es lo que deben hacer: la tercera parte de ustedes, vigile la casa del rey el día de reposo, el sábado,
6 gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
Otra tercera parte estaré en el Sur, y la otra tercera parte parte en la puerta posterior del cuartel de la guardia. Así cubrirán ustedes por turnos la guardia del palacio.
7 Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
Y las dos divisiones de ustedes, que salen el sábado y vigilan el templo del Señor junto al rey.
8 Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
Harán un círculo alrededor del rey, cada uno de los hombres armados; y el que entre dentro de tus líneas ha de ser muerto; acompañarán al rey, cuando sale y cuando entra.
9 Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
Y los capitanes de centenares hicieron como el sacerdote Joiada les dio órdenes; Todos tomaron con él a sus hombres, los que entraron y los que salieron el sábado, y se presentaron al sacerdote Joiada.
10 Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
Y el sacerdote dio a los capitanes de centenares las lanzas y escudos que habían sido del rey David, y que se guardaban en la casa del Señor.
11 Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
Entonces los hombres armados tomaron sus posiciones, cada uno con sus instrumentos de guerra en la mano, desde el lado derecho de la casa hacia la izquierda, alrededor del altar y la casa.
12 Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
Luego sacó al hijo del rey, puso la corona sobre él y los brazaletes, y lo hizo rey, y puso aceite santo sobre él. y todos ellos, haciendo sonidos de alegría con sus manos, dijeron: Larga vida al rey.
13 Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
Ahora, Atalía, oyendo el ruido hecho por la gente, vino a la gente en el templo del Señor;
14 Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
Al mirar, vio al rey en su lugar habitual junto a la columna, y los capitanes y los cuernos cerca de él; y toda la gente de la tierra dando señales de alegría y haciendo sonar los cuernos. Entonces Atalía, separando violentamente sus ropas, lanzó un grito, diciendo: ¡Traición!
15 Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
Entonces el sacerdote Joiada dio órdenes a los que estaban en autoridad sobre el ejército, diciendo: Llévala fuera de las filas, y que cualquiera que la persiga sea condenado a muerte con espada, porque él dijo: No se le dé muerte en la casa del Señor.
16 Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
De modo que pusieron sus manos sobre ella, y ella fue a la casa del rey junto a la puerta de los caballos, y allí la mataron.
17 Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
Y Joiada llegó a un acuerdo entre el Señor, el rey y el pueblo, de que serían el pueblo del Señor; y de la misma manera entre el rey y el pueblo.
18 Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
Entonces todos los habitantes de la tierra fueron a la casa de Baal y la derribaron, sus altares y sus imágenes se rompieron en pedazos, y Matan, el sacerdote de Baal, lo mataron ante los altares. Y el sacerdote puso supervisores sobre él templo del Señor.
19 Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
Luego tomó a los capitanes de cientos, a los cereteos, a los hombres armados y a toda la gente de la región; y descendieron con el rey de la casa del Señor, a través de la puerta de los hombres armados, a la casa del rey. Y él tomó su lugar en el asiento de los reyes.
20 Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
Y se alegraron todos los habitantes de la tierra, y el pueblo quedó en silencio; y mataron a Atalía con la espada en la casa del rey.
21 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.
Y Joás tenía siete años cuando comenzó a reinar.

< 2 Mafumu 11 >