< 2 Mafumu 11 >

1 Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
Or Hathalia mère d'Achazia, ayant vu que son fils était mort, s'éleva, et extermina toute la race Royale.
2 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
Mais Jéhosébah fille du Roi Joram, sœur d'Achazia prit Joas fils d'Achazia, et le déroba d'entre les fils du Roi qu'on faisait mourir, [et le mit] avec sa nourrice dans la chambre aux lits; et on le cacha de devant Hathalia, de sorte qu'on ne le fit point mourir.
3 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
Et il fut caché avec elle dans la maison de l'Eternel, l'espace de six ans; cependant Hathalia régnait sur le pays.
4 Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
Et la septième année Jéhojadah envoya, et prit des centeniers, des capitaines, et des archers, et les fit entrer vers soi dans la maison de l'Eternel, et traita alliance avec eux, et les fit jurer dans la maison de l'Eternel, et leur montra le fils du Roi.
5 Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
Puis il leur commanda, en disant: [C'est] ici ce que vous ferez: La troisième partie d'entre vous qui entrez en semaine, fera la garde de la maison du Roi;
6 gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
Et la troisième partie sera à la porte de Sur; et la troisième partie sera à la porte qui est derrière les archers; ainsi vous ferez le guet pour garder le Temple, afin que personne n'y entre par force.
7 Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
Et les deux compagnies d'entre vous qui sortez de semaine, feront le guet pour garder la maison de l'Eternel, auprès du Roi.
8 Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
Et vous environnerez le Roi tout autour, chacun ayant ses armes en sa main, et si quelqu'un entre dans les rangs, qu'il soit mis à mort; vous serez avec le Roi quand il sortira, et quand il entrera.
9 Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
Les centeniers donc firent comme Jéhojadah le Sacrificateur avait commandé; ils prirent chacun ses gens, tant ceux qui entraient en semaine, que ceux qui sortaient de semaine; et ils vinrent vers le Sacrificateur Jéhojadah.
10 Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
Et le sacrificateur donna aux centeniers des hallebardes et des boucliers qui avaient été au Roi David, [et] qui étaient dans la maison de l'Eternel.
11 Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
Et les archers se tinrent rangés auprès du Roi tout alentour, ayant chacun les armes à la main, depuis le côté droit du Temple jusqu'au côté gauche, tant pour l'autel que pour le Temple.
12 Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
Et [Jéhojadah] fit amener le fils du Roi, et mit sur lui la couronne, et le Témoignage, et ils l'établirent Roi, et l'oignirent, et frappant des mains, ils dirent: Vive le Roi!
13 Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
Et Hathalia entendant le bruit des archers, et du peuple, entra vers le peuple dans la maison de l'Eternel.
14 Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
Et elle regarda, et voilà, le Roi était près de la colonne, selon la coutume des Rois, et les capitaines et les trompettes étaient près du Roi, et tout le peuple du pays éclatait de joie, et on sonnait des trompettes. Alors Hathalia déchira ses vêtements, et cria: Conjuration! conjuration!
15 Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
Et le Sacrificateur Jéhojadah commanda aux centeniers qui avaient la charge de l'armée, et leur dit: Menez-la hors des rangs, et que celui qui la suivra soit mis à mort par l'épée; car le Sacrificateur avait dit: Qu'on ne la mette point à mort dans la maison de l'Eternel.
16 Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
Ils lui firent donc place; et elle revint dans la maison du Roi par le chemin de l'entrée des chevaux, et elle fut tuée là.
17 Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
Et Jéhojadah traita alliance entre l'Eternel, le Roi, et le peuple, qu'ils seraient pour peuple à l'Eternel; [il traita] de même [alliance] entre le Roi et le peuple.
18 Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
Alors tout le peuple du pays entra dans la maison de Bahal, la démolirent, avec ses autels, et ils brisèrent entièrement ses images; ils tuèrent aussi Mattam Sacrificateur de Bahal, devant les autels; et le Sacrificateur ordonna des gardes en la maison de l'Eternel.
19 Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
Et il prit les centeniers, les capitaines, les archers, et tout le peuple du pays, et ils firent descendre le Roi de la maison de l'Eternel, et ils entrèrent dans la maison du Roi par le chemin de la porte des archers, et [Joas] s'assit sur le trône des Rois.
20 Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
Et tout le peuple du pays fut dans la joie, et la ville fut en repos; quoiqu'on eût mis à mort Hathalia par l'épée dans la maison du Roi.
21 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.
Joas était âgé de sept ans quand il commença à régner.

< 2 Mafumu 11 >