< 2 Mafumu 11 >
1 Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
Or Athalie, mère d’Achazia, vit que son fils était mort, et elle se leva et fit périr toute la semence royale.
2 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
Mais Jehoshéba, fille du roi Joram, sœur d’Achazia, prit Joas, fils d’Achazia, et le déroba du milieu des fils du roi qu’on mettait à mort [et le cacha], lui et sa nourrice, dans la chambre à coucher; et on le cacha de devant Athalie, et il ne fut pas mis à mort.
3 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
Et il fut caché six ans auprès d’elle dans la maison de l’Éternel. Et Athalie régna sur le pays.
4 Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
Et la septième année, Jehoïada envoya, et prit les chefs de centaines des gardes et des coureurs; et il les fit entrer vers lui dans la maison de l’Éternel, et fit un pacte avec eux et les fit jurer dans la maison de l’Éternel, et leur montra le fils du roi.
5 Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
Et il leur commanda, disant: C’est ici ce que vous ferez: un tiers d’entre vous qui entrez le [jour du] sabbat, fera la garde de la maison du roi;
6 gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
et un tiers sera à la porte de Sur; et un tiers sera à la porte qui est derrière les coureurs; et vous veillerez à la garde de la maison, pour tenir à distance [tout étranger].
7 Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
Et les deux tiers d’entre vous, tous ceux qui sortent le [jour du] sabbat, feront la garde de la maison de l’Éternel, auprès du roi.
8 Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
Et vous entourerez le roi de tous côtés, chacun ses armes à la main; et celui qui entrera dans les rangs sera mis à mort; et soyez avec le roi quand il sortira et quand il entrera.
9 Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
Et les chefs de centaines firent selon tout ce que Jehoïada, le sacrificateur, avait commandé; et ils prirent chacun ses hommes, ceux qui entraient le [jour du] sabbat et ceux qui sortaient le [jour du] sabbat; et ils vinrent auprès de Jehoïada, le sacrificateur.
10 Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
Et le sacrificateur donna aux chefs de centaines les lances et les boucliers qui avaient appartenu au roi David, et qui étaient dans la maison de l’Éternel.
11 Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
Et les coureurs se tinrent là, chacun ses armes à la main, depuis le côté droit de la maison jusqu’au côté gauche de la maison, vers l’autel et vers la maison, auprès du roi, tout autour.
12 Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
Et on fit sortir le fils du roi, et on mit sur lui la couronne et le témoignage; et ils le firent roi, et l’oignirent, et frappèrent des mains, et dirent: Vive le roi!
13 Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
Et Athalie entendit le cri des coureurs [et] du peuple, et elle entra vers le peuple dans la maison de l’Éternel.
14 Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
Et elle regarda, et voici, le roi se tenait sur l’estrade, suivant l’usage, et les chefs et les trompettes étaient auprès du roi, et tout le peuple du pays se réjouissait et sonnait des trompettes. Et Athalie déchira ses vêtements, et s’écria: Conspiration! Conspiration!
15 Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
Et Jehoïada, le sacrificateur, commanda aux chefs de centaines qui étaient préposés sur l’armée, et leur dit: Faites-la sortir en dehors des rangs, et celui qui la suivra mettez-le à mort par l’épée; car le sacrificateur dit: Qu’elle ne soit pas mise à mort dans la maison de l’Éternel.
16 Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
Et ils lui firent place; et elle alla par le chemin de l’entrée des chevaux dans la maison du roi, et là elle fut mise à mort.
17 Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
Et Jehoïada fit une alliance entre l’Éternel et le roi et le peuple, qu’ils seraient le peuple de l’Éternel, – et entre le roi et le peuple.
18 Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
Et tout le peuple du pays entra dans la maison de Baal, et ils la démolirent; ses autels et ses images, ils les brisèrent entièrement; et ils tuèrent devant les autels Matthan, sacrificateur de Baal. Et le sacrificateur établit des gardes sur la maison de l’Éternel.
19 Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
Et il prit les chefs de centaines, et les gardes, et les coureurs, et tout le peuple du pays, et ils firent descendre le roi de la maison de l’Éternel, et entrèrent dans la maison du roi par le chemin de la porte des coureurs; et il s’assit sur le trône des rois.
20 Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
Et tout le peuple du pays se réjouit, et la ville fut tranquille: et ils avaient mis à mort Athalie par l’épée, dans la maison du roi.
21 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.
Joas était âgé de sept ans lorsqu’il commença de régner.