< 2 Mafumu 11 >

1 Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
And Athaliah [the] mother of Ahaziah (she saw *Q(K)*) that he was dead son her and she arose and she destroyed all [the] offspring of royalty.
2 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
And she took Jehosheba [the] daughter of the king Joram [the] sister of Ahaziah Joash [the] son of Ahaziah and she stole him from among [the] sons of the king (who were about to be put to death *Q(K)*) him and suckling-nurse his in [the] chamber of the beds and they hid him from before Athaliah and not he was put to death.
3 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
And he was with her [the] house of Yahweh hiding himself six years and Athaliah [was] reigning over the land.
4 Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
And in the year seventh he sent Jehoiada and he took - [the] commanders of (the hundreds *Q(k)*) of the Carian[s] and of the runners and he brought them to himself [the] house of Yahweh and he made to them a covenant and he made to swear an oath with them in [the] house of Yahweh and he showed them [the] son of the king.
5 Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
And he commanded them saying this [is] the thing which you will do! the third [part] of you [who] come the sabbath and [who] keep [the] watch of [the] house of the king.
6 gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
And the third [part] [will be] at [the] gate of Sur and the third [part] [will be] at the gate behind the runners and you will keep [the] watch of the house by turns.
7 Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
And [the] two the hands in you all [those who] go out the sabbath and they will keep [the] watch of [the] house of Yahweh to the king.
8 Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
And you will surround the king all around everyone and weapons his in hand his and the [one who] comes into the ranks he will be put to death and be with the king when goes out he and when comes he.
9 Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
And they did [the] commanders of (the hundreds *Q(k)*) according to all that he commanded Jehoiada the priest and they took each men his [those who] came the sabbath with [those who] went out the sabbath and they came to Jehoiada the priest.
10 Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
And he gave the priest to [the] commanders of (the hundreds *Q(k)*) the spear and the shields which [had belonged] to the king David which [were] in [the] house of Yahweh.
11 Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
And they stood the runners everyone - and weapons his in hand his from [the] side of the house south to [the] side of the house north to the altar and to the house at the king all around.
12 Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
And he brought out [the] son of the king and he put on him the crown and the testimony and they made king him and they anointed him and they struck a palm and they said may he live the king.
13 Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
And she heard Athaliah [the] sound of the runners the people and she went to the people [the] house of Yahweh.
14 Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
And she saw and there! the king [was] standing at the pillar according to the custom and the commanders and the trumpets [were] with the king and all [the] people of the land [was] joyful and [was] giving a blast on trumpets and she tore Athaliah clothes her and she called out treason treason.
15 Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
And he commanded Jehoiada the priest [the] commanders of (the hundreds *Q(k)*) [the] officers of the army and he said to them bring out her to from between to the ranks and the [one who] comes behind her put to death with the sword for he had said the priest may not she be put to death [the] house of Yahweh.
16 Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
And they put to her hands and she went [the] way of [the] entrance of the horses [the] house of the king and she was put to death there.
17 Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
And he made Jehoiada the covenant between Yahweh and between the king and between the people to become a people of Yahweh and between the king and between the people.
18 Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
And they went all [the] people of the land [the] house of Baal and they pulled down it (altars its *Q(K)*) and images its they broke thoroughly and Mattan [the] priest of Baal they killed before the altars and he appointed the priest overseers over [the] house of Yahweh.
19 Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
And he took [the] commanders of the hundreds and the Carian[s] and the runners and - all [the] people of the land and they took down the king from [the] house of Yahweh and they came [the] way of [the] gate of the runners [the] house of the king and he sat on [the] throne of the kings.
20 Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
And it rejoiced all [the] people of the land and the city it was at peace and Athaliah they had put to death with the sword [the] house of (the king. *Q(K)*)
21 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.
[was] a son of Seven years Jehoash when became king he.

< 2 Mafumu 11 >