< 2 Mafumu 11 >

1 Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
And Athalia the mother of Ochozias seeing that her son was dead, arose, and slew all the royal seed.
2 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
But Josaba the daughter of king Joram, sister of Ochozias, took Joas the son of Ochozias, and stole him from among the king’s sons that were slain, out of the bedchamber with his nurse: and hid him from the face of Athalia, so that he was not slain.
3 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
And he was with her six years hid in the house of the Lord. And Athalia reigned over the land.
4 Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
And in the seventh year Joiada seat, and taking the centurions and the soldiers, brought them in to him into the temple of the Lord, and made a covenant with them: and taking an oath of them in the house of the Lord, shewed them the king’s son:
5 Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
And he commanded them, saying: This is the thing that you must do:
6 gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
Let a third part of you go in on the sabbath, and keep the watch of the king’s house. And let a third part be at the gate of Sur: and let a third part be at the gate behind the dwelling of the shieldbearers: and you shall keep the watch of the house of Messa.
7 Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
But let two parts of you, all that go forth on the sabbath, keep the watch of the house of the Lord about the king.
8 Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
And you shall compass him round about, having weapons in your hands: and if any man shall enter the precinct of the temple, let him be slain: and you shall be with the king coming in and going out.
9 Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
And the centurions did according to all things that Joiada the priest had commanded them: and taking every one their men, that went in on the sabbath, with them that went out on the sabbath, came to Joiada the priest.
10 Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
And he gave them the spears, and the arms of king David, which were in the house of the Lord.
11 Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
And they stood having every one their weapons in their hands, from the right side of the temple, unto the left side of the altar, and of the temple, about the king.
12 Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
And he brought forth the king’s son, and put the diadem upon him, and the testimony: and they made him king, and anointed him: and clapping their hands. they said, God save the king.
13 Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
And Athalia heard the noise of the people running: and going in to the people into the temple of the Lord,
14 Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
She saw the king standing upon a tribunal, as the manner was, and the singers, and the trumpets near him, and all the people of the land rejoicing, and sounding the trumpets: and she rent her garments, and cried: A conspiracy, a conspiracy.
15 Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
But Joiada commended the centurions that were over the army, and said to them: Have her forth without the precinct of the temple, and whosoever shall follow her, let him be slain with the sword. For the priest had said: Let her not be slain in the temple of the Lord.
16 Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
And they laid hands on her: and thrust her out by the way by which the horses go in, by the palace, and she was slain there.
17 Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
And Joiada made a covenant between the Lord, and the king, and the people, that they should be the people of the Lord, and between the king and the people.
18 Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
And all the people of the land went into the temple of Baal, and broke down his altars, and his images they broke in pieces thoroughly: they slew also Mathan the priest of Baal before the altar. And the priest set guards in the house of the Lord.
19 Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
And he took the centurions, and the bands of the Cerethi and the Phelethi, and all the people of the land, and they brought the king from the house of the Lord: and they came by the way of the gate of the shieldbearers into the palace. and he sat on the throne of the kings.
20 Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
And all the people of the land rejoiced, and the city was quiet: but Athalia was slain with the sword in the king’s house.
21 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.
Now Joas was seven years old, when he began to reign.

< 2 Mafumu 11 >