< 2 Mafumu 11 >
1 Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
Der Athalia, Ahasias Moder, saa, at hendes Søn var død, da gjorde hun sig rede og udryddede al kongelig Sæd.
2 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
Men Joseba, Kong Jorams Datter, Ahasias Søster, tog Joas, Ahasias Søn, og stjal ham midt ud af Kongens Børn, som bleve dræbte, ham og hans Amme i Sengekammeret; og de skjulte ham for Athalias Ansigt, saa at han ikke blev dræbt.
3 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
Og han var hos hende i Herrens Hus skjult i seks Aar; men Athalia var Dronning i Landet.
4 Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
Men i det syvende Aar sendte Jojada og tog de øverste over hundrede for Livvagten og Drabanterne og lod dem komme til sig i Herrens Hus; og han gjorde en Pagt med dem og tog en Ed af dem i Herrens Hus og viste dem Kongens Søn.
5 Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
Og han bød dem og sagde: Dette er den Gerning, som I skulle gøre: Den tredje Part af eder, som træde til om Sabbaten, skal holde Vagt imod Kongens Hus.
6 gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
Og den tredje Part skal være ved Porten Sur og den tredie Part ved Porten, som er bag Drabanterne, og I skulle holde Vagt for Huset for at afspærre det.
7 Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
Men de to Parter af eder, nemlig alle, som træde fra om Sabbaten, de skulle holde Vagt i Herrens Hus om Kongen.
8 Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
Og I skulle omringe Kongen trindt omkring, enhver med sine Vaaben i sin Haand, og hvo som trænger ind igennem Rækkerne, skal dødes; og I skulle være hos Kongen, naar han gaar ud, og naar han gaar ind.
9 Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
Og de øverste for hundrede gjorde efter alt det, som Jojada, Præsten, bød, og de toge hver sine Mænd, som traadte til om Sabbaten, tillige med dem, som traadte fra om Sabbaten, og de kom til Præsten Jojada.
10 Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
Og Præsten gav Høvedsmændene for hundrede Spydene og Skjoldene, som havde hørt Kong David til, og som vare i Herrens Hus.
11 Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
Og Drabanterne stode, hver med sine Vaaben i sin Haand, fra den højre Side af Huset til den venstre Side af Huset, hen imod Alteret og Huset, trindt omkring Kongen.
12 Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
Siden førte han Kongens Søn ud og satte Kronen paa ham og overgav ham Vidnesbyrdet, og de gjorde ham til Konge og salvede ham, og de klappede i Hænderne og sagde: Kongen leve!
13 Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
Der Athalia hørte Drabanternes og Folkets Røst, da kom hun til Folket i Herrens Hus.
14 Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
Og hun saa, og se, da stod Kongen paa Forhøjningen, som Skik var, og Fyrsterne og Basunerne vare om Kongen, og alt Folket i Landet var glad og blæste i Basunerne; da sønderrev Athalia sine Klæder og raabte: Oprør! Oprør!
15 Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
Men Jojada, Præsten, bød de øverste over hundrede, som vare beskikkede over Hæren, og sagde til dem: Fører hende ud hen uden for Rækkerne, og hvo som følger hende, dræber ham med Sværd; thi Præsten havde sagt, at hun ikke skulde dræbes i Herrens Hus.
16 Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
Og de gjorde Plads for hende til begge Sider, og hun gik den Vej, ad hvilken Hestene gaa til Kongens Hus, og hun blev dræbt der.
17 Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
Da gjorde Jojada en Pagt imellem Herren og imellem Kongen og Folket, at de skulde være Herrens Folk, og imellem Kongen og imellem Folket.
18 Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
Da kom alt Folket i Landet ind i Baals Hus, og de nedbrøde hans Altre, og hans Billeder sønderbrøde de aldeles og sloge Matthan, Baals Præst, ihjel lige for Altrene; men Præsten beskikkede Tilsyn i Herrens Hus.
19 Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
Og han tog de øverste over hundrede og Livvagten og Drabanterne og alt Folket fra Landet, og de førte Kongen ned fra Herrens Hus og kom ad Vejen igennem Drabanternes Port til Kongens Hus; og han satte sig paa Kongernes Trone.
20 Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
Og alt Folket i Landet var glad, og Staden blev rolig, efter at de havde slaget Athalia ihjel med Sværd i Kongens Hus.
21 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.
Joas var syv Aar gammel, der han blev Konge.