< 2 Mafumu 11 >

1 Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
Atalia pak matka Ochoziášova viduci, že umřel syn její, vstavši, pomordovala všecko símě královské.
2 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
Ale Jozaba dcera krále Jehorama, sestra Ochoziášova, vzala Joasa syna Ochoziášova, a ukradši ho z prostředku synů královských, kteříž mordováni byli, skryla jej i s chůvou jeho v pokoji, kdež lůže byla. A tak skryli ho před Atalií, a není zamordován.
3 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
I byl s ní v domě Hospodinově tajně za šest let, v nichž Atalia kralovala nad zemí.
4 Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
Léta sedmého poslav Joiada, povolal setníků, hejtmanů a drabantů. I uvedl je k sobě do domu Hospodinova, a učinil s nimi smlouvu, a zavázav je přísahou v domě Hospodinově, ukázal jim syna králova.
5 Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
A přikázal jim, řka: Tato jest věc, kterouž učiníte: Třetí díl vás, kteříž přicházíte v sobotu, a držíte stráž, bude při domě králově,
6 gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
A díl třetí bude u brány Sur, a třetí díl bude u brány za drabanty, a budete stráž držeti, ostříhajíce domu tohoto před outokem.
7 Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
Vy pak všickni, kteříž byste odjíti měli v sobotu, po vykonání povinnosti při domě Hospodinově, ve dvě poboční stráže rozdělení, buďte při králi.
8 Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
A tak obstoupíte krále vůkol, jeden každý majíce braň svou v rukou svých. Kdož by pak šel do šiku vašeho, ať umře; a budete při králi, když bude vycházeti i když bude vcházeti.
9 Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
Protož učinili setníci ti všecky věci tak, jakž byl rozkázal Joiada kněz, a vzavše jeden každý muže své, kteříž přicházeli v sobotu a kteříž odcházeli v sobotu, přišli k Joiadovi knězi.
10 Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
I dal kněz setníkům kopí a pavézy, kteréž byly Davida krále, a kteréž byly v domě Hospodinově.
11 Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
Stáli pak ti drabanti, jeden každý držíce braň svou v ruce své, od pravé strany domu až do levé strany domu, proti oltáři a proti domu při králi vůkol.
12 Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
Tedy vyvedl syna králova, a vstavil na něj korunu a ozdobu. I ustanovili jej králem a pomazali ho, a plésajíce rukama, říkali: Živ buď král!
13 Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
V tom uslyševši Atalia hluk plésajícího lidu, vešla k lidu do domu Hospodinova.
14 Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
A když pohleděla, a aj, král stál na místě vyšším, vedlé obyčeje s knížaty, a trouby byly před králem, a všecken lid země byl vesel, i troubili v trouby. Tedy roztrhla Atalia roucho své a zkřikla: Spiknutí, spiknutí!
15 Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
Protož rozkázal Joiada kněz těm setníkům ustaveným nad vojskem, řka jim: Pusťte ji prostředkem řadu, a i toho, kdož by za ní šel, zabíte mečem. Nebo byl řekl kněz: Ať není zabita v domě Hospodinově.
16 Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
I pustili ji. Ale když přišla na cestu, kudy koni vcházejí do domu královského, tu jest zabita.
17 Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
Tedy učinil Joiada smlouvu mezi Hospodinem a mezi králem, i mezi lidem, aby byli lid Hospodinův; též mezi králem a mezi lidem.
18 Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
Potom šel všecken lid země do domu Bálova, a zbořili jej, i oltáře jeho a obrazy jeho v kusy stroskotali; Matana také kněze Bálova zabili před oltáři. Kněz pak znovu nařídil přisluhující v domě Hospodinově.
19 Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
A pojav ty setníky a hejtmany, i drabanty se vším lidem země, provázeli krále z domu Hospodinova, a přišli cestou k bráně drabantů do domu královského. Kdežto posadil se na stolici královské.
20 Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
I veselil se všecken lid země, a město se upokojilo. Atalii pak zabili mečem u domu královského.
21 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.
A byl Joas v sedmi letech, když počal kralovati.

< 2 Mafumu 11 >