< 2 Mafumu 10 >

1 Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati,
A HE kanahiku na keiki a Ahaba ma Samaria. A kakau iho la o Iehu i na palapala, hoouna aku i Samaria, na na luna o Iezereela, na na luna kahiko, a na na kahu o na keiki a Ahaba, i ka i ana'e,
2 “Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo,
Ano, a hiki aku keia palapala io oukou la, no ka noho ana o na keiki a ko oukou haku me oukou, a ia oukou na halekaa a me na lio, a me ke kulanakauhale paa i ka papohaku, a me na mea kaua;
3 sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”
E imi aku oukou i ka mea maikai a me ka mea pono o na keiki a ko oukou haku, a e hoonoho ia ia maluna o ka nohoalii o kona makuakane, a e kaua mai no ko ka hale o ko oukou haku.
4 Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”
A makau loa iho la lakou, i ae la, Aia hoi, aole i ku na'lii elua imua ona; pehea la kakou e ku ai?
5 Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”
A o ka luna o ko ka hale, a me ka luna o ke kulanakauhale, o na lunakahiko, a me na haku, hoouna aku la lakou io Iehu la, i aku la, He poe kauwa makou nau, a e hana no makou i na mea a pau au e olelo mai ai; aole e hoaliiia kekahi; e hana oe i ka mea pono i kou manao.
6 Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera.
Alaila palapala hou aku la oia ia lakou, i aku la, ina no'u oukou, a e hoolohe hoi i ko'u leo, alaila, e lawe oukou i na poo o na kanaka, o na keiki a ko oukou haku, a e hele mai i o'u nei i Iezereela ma keia manawa i ka la apopo. (A o na keiki a ke alii, he kanahiku lakou e noho ana me na kanaka koikoi o ke kulanakauhale, nana lakou i hanai.)
7 Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu.
A hiki aku ka palapala io lakou la, lawe lakou i na keiki a ke alii, a pepehi iho la i na mea he kanahiku, a waiho lakou i na poo maloko o na hinai, a hoouna aku io na la ma Iezereela.
8 Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.” Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”
A hele mai kekahi elele a hai aku ia ia, i aku la, Ua lawe mai lakou i na poo o na keiki a ke alii. I mai la ia, E waiho ia lakou ma na puu elua, ma kahi i komo ai i ka ipuka, a kakahiaka.
9 Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani?
A i kakahiaka, hele aku ia, a ku, i aku la i na kanaka a pau, Ua pono oukou: aia hoi, ua kipi aku au i kuu haku, a pepehi aku ia ia: aka, owai la ka i pepehi i keia mau mea a pau?
10 Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.”
E ike ana oukou, aole e haule i ka honua kekahi o ka olelo a Iehova i olelo mai ai no ko ka hale o Ahaba: no ka mea, ua hana mai o Iehova i ka mea ana i olelo mai ai ma o Elia la kana kauwa.
11 Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.
A pepehi aku la o Iehu i na mea a pau i koe no ko ka hale o Ahaba ma Iezereela, a me kona poe koikoi a pau, a me kona poe hoalauna, a me kana poe kahuna, aole ia i hookoe i kekahi nona.
12 Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa,
A ku ae la ia, a hele aku la a hiki i Samaria. Aia no ia ma ka hale hoopaa o na kahuhipa ma ke aia.
13 Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?” Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”
A loaa ia Iehu na hoahanau o Ahazia ke alii o ka Iuda, a ninau aku la, Owai oukou? I mai la lakou, He mau hoahanau makou no Ahazia, a e iho ana makou e ike i na keiki a ke alii a me na keiki a ke aliiwahine.
14 Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.
I aku la, E hoopaa ola aku ia lakou: a hoopaa ola aku la na kanaka ia lakou, a luku aku la ia lakou ma ka luawai o ka hale hoopaa, he kanaha kumamalua na kanaka; aole ia i hookoe i kekahi o lakou.
15 Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?” Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.” Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake.
A hele ia mailaila aku a loaa ia ia o Iehonadaba ke keiki a Rekaba e halawai me ia: a hoomaikai aku o Iehu ia ia, i aku la, Ua pono anei kou naau, e like me ko'u naau me kou naau? I mai la o Iehonadaba, Oia no. Ina pela, e haawi mai oe i kou lima. A haawi aku ia i kona lima, a hoee aku la ia ia ma ka halekaa me ia.
16 Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.
I aku la ia, E hele pu oe me au, a ike oe i kuu ikaika no Iehova. A hooholo lakou ia ia ma kona halekaa.
17 Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.
A hiki aku la ia i Samaria, pepehi aku la ia i na mea a pau i koe no Ahaba ma Samaria, a pau ia i ka lukuia, e like me ka olelo a Iehova ana i olelo mai ai ma o Elia la.
18 Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri.
Houluulu ae la o Iehu i na kanaka a pau, a i aku la ia lakou, Malama uuku aku o Ahaba ia Baala, e malama nui auanei o Iehu ia ia.
19 Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.
Ano hoi, e hoakoakoa mai oukou i na kaula a pau a Baala, a me kana poe kauwa a pau, a me kana poe kahuna a pau io'u nei, mai hookoeia kekahi; no ka mea, he mohai nui ka'u no Baala; o kela mea keia mea e koe ana, aole ia e ola. Aka, hana no o Iehu me ka hoopunipuni, i luku aku ai ia i ka poe malama ia Baala.
20 Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo.
I aku la o Iehu, E hoolaa aku i ka houluulu ana no Baala. A hoolaa aku la lakou.
21 Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina.
A hoouna aku la o Iehu i ka Iseraela a puni; a hele mai na kauwa a pau a Baala, aole i koe aku kekahi i hele ole mai. A komo lakou i ka hale o Baala, a piha loa ka hale o Baala mai kela aoao a i keia aoao.
22 Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.
I aku la ia i ka mea nana i malama ke keena lole, E lawe mai iwaho i ka lole no na kauwa a Baala. A lawe mai no ia i ka lole no lakou.
23 Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.”
Komo aku o Iehu, a me Iehonadaba, ke keiki a Rekaba, iloko o ka hale o Baala, a i aku la i na kauwa a Baala, E nana oukou a ike, i ole maanei me oukou kekahi o na kauwa a Iehova, o na kauwa a Baala wale no.
24 Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”
A komo aku la lakou e kaumaha aku i ka mohai, a me na mohaikuni, alaila hoonoho iho la o Iehu i na kanaka, he kanawalu mawaho, i aku la, O ka mea nana e hoopakele kekahi o na kanaka a'u i lawe mai nei iloko o ko oukou lima, o lilo no kona ola no ko ia la ola.
25 Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala.
A pau kana kaumaha ana'ku i ka mohaikuni, i aku la o Iehu i ka poe kiai, a i na luna, E komo iloko, e luku ia lakou; mai puka iwaho kekahi. A luku aku la ua poe la ia lakou me ka maka o ka pahikaua; a o ka poe kiai a me na luna hoolei aku la ia lakou, a hele aku la i ke kulanakauhale o Baala.
26 Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha.
A lawe mai lakou i na kii mawaho o ka hale o Baala, a puhi aku la i ke ahi.
27 Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.
A wawahi lakou i ke kii o Baala, a wawahi hoi i ka hale o Baala, a hoolilo lakou ia mea i hale kiona a hiki i keia la.
28 Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli.
A luku aku la o Iehu ia Baala mai loko aku o ka Iseraela.
29 Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.
Aka hoi, o na hewa o Ieroboama ke keiki a Nebata, nana i hoolilo ka Iseraela i ka hewa, aole i haalele o Iehu i ka hahai ana mamuli o lakou, o na keikibipi gula ma Betela a ma Dana.
30 Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
A olelo mai o Iehova ia Iehu, no ka mea, ua maikai oe i ka hana ana i ka pono ia'u, a ua hana aku oe i ko ka hale o Ahaba, e like me ka mea a pau ma ko'u naau, e noho auanei kau poe keiki maluna o ka nohoalii o ka Iseraela a hiki i ke kualua.
31 Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.
Aka, aole o Iehu i malama i ka hele ana ma ke kanawai o Iehova ke Akua o ka Iseraela me kona naau a pau: no ka mea, aole ia i haalele i na hewa o Ieroboama, nana i hoolilo ka Iseraela i ka hewa.
32 Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli,
I kela manawa i hoomaka ai o Iehova e paipai i ka Iseraela: a luku mai la o Hazaela ia lakou ma na mokuna a pau o ka Iseraela;
33 kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.
Mai Ioredane, mai ka hikina o ka la, i ka aina a pau o Gileada, i ka Gada, a me ka Reubena, a me ka Manase, mai Aroera ma ke kahawai o Arenona, a hiki i Gileada a me Basana.
34 Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
A o na mea i koe a Iehu, a o na mea a pau ana i hana'i, a me kona ikaika a pau, aole anei i kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iseraela?
35 Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A hiamoe iho la o Iehu me kona poe makua; a kanu lakou ia ia ma Samaria. A noho alii o Iehoahaza kana keiki ma kona wahi.
36 Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.
A o ka manawa a Iehu i alii ai maluna o ka Iseraela ma Samaria, he iwakalua na makahiki ia a me kumamawalu.

< 2 Mafumu 10 >