< 2 Mafumu 10 >
1 Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati,
Or Achab avait soixante-dix fils à Samarie. Jéhu écrivit des lettres et les envoya à Samarie, aux chefs de Jizreel, aux anciens, et à ceux qui avaient élevé les fils d'Achab, en disant:
2 “Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo,
« Maintenant, dès que cette lettre vous parviendra, puisque les fils de votre maître sont avec vous, et que vous avez des chars et des chevaux, une ville fortifiée et des armes,
3 sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”
choisissez le meilleur et le plus apte des fils de votre maître, mettez-le sur le trône de son père, et combattez pour la maison de votre maître. »
4 Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”
Mais ils eurent très peur et dirent: « Voici, les deux rois ne se sont pas tenus devant lui! Comment allons-nous donc nous tenir debout? »
5 Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”
Celui qui était à la tête de la maison, celui qui était à la tête de la ville, les anciens aussi, et ceux qui élevaient les enfants, envoyèrent dire à Jéhu: « Nous sommes tes serviteurs, et nous ferons tout ce que tu nous demanderas. Nous ne ferons pas de roi un autre homme. Fais ce qui est bon à tes yeux. »
6 Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera.
Puis il leur écrivit une seconde fois une lettre dans laquelle il disait: « Si vous êtes de mon côté, et si vous écoutez ma voix, prenez les têtes des hommes qui sont les fils de vos maîtres, et venez me voir à Jizreel demain à cette heure-ci. » Or les fils du roi, au nombre de soixante-dix personnes, étaient avec les grands de la ville, qui les firent monter.
7 Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu.
Lorsque la lettre leur parvint, ils prirent les fils du roi, les tuèrent, soit soixante-dix personnes, mirent leurs têtes dans des paniers, et les envoyèrent à Jizreel.
8 Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.” Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”
Un messager vint lui dire: « On a apporté les têtes des fils du roi. » Il dit: « Disposez-les en deux tas à l'entrée de la porte jusqu'au matin. »
9 Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani?
Au matin, il sortit, se tint debout, et dit à tout le peuple: « Vous êtes justes. Voici, j'ai conspiré contre mon maître et je l'ai tué, mais qui a tué tous ceux-là?
10 Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.”
Sachez maintenant que rien ne tombera à terre de la parole de l'Éternel, que l'Éternel a prononcée sur la maison d'Achab. Car Yahvé a accompli ce qu'il avait annoncé par son serviteur Élie. »
11 Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.
Et Jéhu frappa tout ce qui restait de la maison d'Achab à Jizreel, avec tous ses grands, ses familiers et ses prêtres, jusqu'à ce qu'il ne lui restât plus personne.
12 Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa,
Il se leva, partit, et se rendit à Samarie. Comme il se trouvait en chemin dans la bergerie des bergers,
13 Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?” Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”
Jéhu rencontra les frères d'Achazia, roi de Juda, et dit: « Qui êtes-vous? » Ils répondirent: « Nous sommes les frères d'Achazia. Nous descendons saluer les enfants du roi et les enfants de la reine. »
14 Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.
Il a dit: « Prenez-les vivants! » Ils les prirent vivants, et les tuèrent à la fosse de la tondeuse, même quarante-deux hommes. Il n'en a laissé aucun.
15 Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?” Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.” Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake.
Comme il était parti de là, il rencontra Jehonadab, fils de Rechab, qui venait à sa rencontre. Il le salua, et lui dit: « Ton cœur est-il droit, comme mon cœur est avec ton cœur? » Jehonadab a répondu: « C'est vrai. » « Si c'est le cas, donne-moi ta main. » Il lui donna sa main, et il le fit monter vers lui dans le char.
16 Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.
Il dit: « Viens avec moi, et vois mon zèle pour Yahvé. » Et ils le firent monter dans son char.
17 Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.
Lorsqu'il arriva à Samarie, il frappa tous ceux qui restaient à Achab à Samarie, jusqu'à ce qu'il les eût détruits, selon la parole de l'Éternel qu'il avait adressée à Élie.
18 Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri.
Jéhu rassembla tout le peuple et leur dit: « Achab a un peu servi Baal, mais Jéhu le servira beaucoup.
19 Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.
Maintenant, appelez-moi tous les prophètes de Baal, tous ses adorateurs et tous ses prêtres. Que personne ne soit absent, car j'ai un grand sacrifice à offrir à Baal. Celui qui sera absent ne vivra pas. » Mais Jéhu agit de manière trompeuse, avec l'intention de détruire les adorateurs de Baal.
20 Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo.
Jéhu a dit: « Sanctifiez une assemblée solennelle pour Baal! » Et ils le proclamèrent.
21 Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina.
Jéhu envoya par tout Israël; et tous les adorateurs de Baal vinrent, de sorte qu'il ne resta pas un homme qui ne vint pas. Ils entrèrent dans la maison de Baal, et la maison de Baal fut remplie d'un bout à l'autre.
22 Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.
Il dit à celui qui gardait l'armoire: « Sortez des robes pour tous les adorateurs de Baal! ». Il leur apporta donc des robes.
23 Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.”
Jéhu entra avec Jéhonadab, fils de Réchab, dans la maison de Baal. Il dit alors aux adorateurs de Baal: « Cherchez, et voyez qu'il n'y a ici avec vous aucun des serviteurs de Yahvé, mais seulement les adorateurs de Baal. »
24 Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”
Et ils entrèrent pour offrir des sacrifices et des holocaustes. Or Jéhu s'était désigné quatre-vingts hommes à l'extérieur, et il avait dit: « Si l'un des hommes que je livre entre tes mains s'échappe, celui qui le laissera partir en aura pour sa vie. »
25 Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala.
Dès qu'il eut fini d'offrir l'holocauste, Jéhu dit à la garde et aux chefs: « Entrez et tuez-les! Que personne n'échappe. » Ils les frappèrent donc du tranchant de l'épée. La garde et les chefs jetèrent les cadavres dehors et allèrent dans le sanctuaire intérieur de la maison de Baal.
26 Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha.
Ils sortirent les colonnes qui étaient dans la maison de Baal et les brûlèrent.
27 Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.
Ils démolirent la colonne de Baal, ils démolirent la maison de Baal, et ils en firent une latrine, jusqu'à ce jour.
28 Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli.
Ainsi Jéhu détruisit Baal hors d'Israël.
29 Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.
Cependant, Jéhu ne se détourna pas des péchés de Jéroboam, fils de Nebat, par lesquels il avait fait pécher Israël, à savoir les veaux d'or qui étaient à Béthel et ceux qui étaient à Dan.
30 Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
Yahvé dit à Jéhu: « Parce que tu as bien exécuté ce qui est juste à mes yeux, et que tu as fait à la maison d'Achab tout ce qui était dans mon cœur, tes descendants s'assiéront sur le trône d'Israël jusqu'à la quatrième génération. »
31 Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.
Mais Jéhu ne prit pas garde de marcher de tout son cœur dans la loi de Yahvé, le Dieu d'Israël. Il ne s'est pas détourné des péchés de Jéroboam, par lesquels il avait fait pécher Israël.
32 Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli,
En ces jours-là, l'Éternel commença à retrancher des parties d'Israël, et Hazaël les frappa dans tout le territoire d'Israël
33 kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.
depuis le Jourdain vers l'orient, tout le pays de Galaad, les Gadites, les Rubénites et les Manassites, depuis Aroër, qui est près du torrent de l'Arnon, jusqu'à Galaad et Basan.
34 Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Et le reste des actes de Jéhu, et tout ce qu'il a fait, et toute sa puissance, n'est-ce pas écrit dans le livre des chroniques des rois d'Israël?
35 Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Jéhu se coucha avec ses pères, et on l'enterra à Samarie. Joachaz, son fils, régna à sa place.
36 Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.
Le temps que Jéhu régna sur Israël à Samarie fut de vingt-huit ans.