< 2 Mafumu 1 >

1 Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
А по смрти Ахавовој одметнуше се Моавци од Израиља.
2 Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
А Охозија паде кроз решетку из горње собе своје у Самарији, и разболе се; па посла посланике и рече им: Идите, питајте Велзевула бога акаронског хоћу ли оздравити од ове болести.
3 Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
Али анђео Господњи рече Илији Тесвићанину: Устани, изађи на сусрет посланицима цара самаријског и реци им: Еда ли нема Бога у Израиљу, те идете да питате Велзевула бога у Акарону?
4 Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
А зато овако вели Господ: Нећеш се дигнути са постеље на коју си легао, него ћеш умрети. Потом отиде Илија.
5 Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
А слуге се вратише к Охозији, и он им рече: Што сте се вратили?
6 Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
А они му рекоше: Срете нас један човек, и рече нам: Идите, вратите се к цару који вас је послао, и реците му: Овако вели Господ: Еда ли нема Бога у Израиљу, те шаљеш да питаш Велзевула бога у Акарону? Зато нећеш се дигнути с постеље на коју си легао, него ћеш умрети.
7 Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
А он им рече: Какав беше на очи тај човек који вас срете и то вам рече?
8 Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
А они му одговорише: Беше сав космат и опасан кожним појасом. А он рече: То је Илија Тесвићанин.
9 Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
Тада посла к њему педесетника с његовом педесеторицом; и он отиде к њему; и гле, он сеђаше наврх горе: и педесетник му рече: Човече Божји, цар је заповедио, сиђи.
10 Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
А Илија одговарајући рече педесетнику: Ако сам човек Божји, нека сиђе огањ с неба и прождре тебе и твоју педесеторицу. И сиђе огањ с неба и прождре њега и његову педесеторицу.
11 Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
Опет посла к њему другог педесетника с његовом педесеторицом, који проговори и рече му: Човече Божји, цар је тако заповедио, сиђи брже.
12 Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
А Илија одговори и рече им: Ако сам човек Божји, нека сиђе огањ с неба и прождре тебе и твоју педесеторицу. И сиђе огањ Божји с неба и прождре њега и његову педесеторицу.
13 Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
Тада опет посла трећег педесетника с његовом педесеторицом. А овај трећи педесетник кад дође, клече на колена своја пред Илијом, и молећи га рече му: Човече Божји, да ти је драга душа моја и душа ове педесеторице, слуга твојих.
14 Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
Ето, сишао је огањ с неба и прождрао прва два педесетника с њиховом педесеторицом; али сада да ти је драга душа моја.
15 Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
А анђео Господњи рече Илији: Иди с њим, и не бој га се. И уста Илија и отиде с њим к цару.
16 Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
И рече му: Овако вели Господ: зато што си слао посланике да питају Велзевула бога у Акарону као да нема Бога у Израиљу да би Га питао, нећеш се дигнути с постеље на коју си легао, него ћеш умрети.
17 Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
И умре по речи Господњој, коју рече Илија, а на његово се место зацари Јорам, друге године царовања Јорама сина Јосафатовог над Јудом, јер он нема сина.
18 Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
А остала дела Охозијина што је чинио, нису ли записана у дневнику царева Израиљевих?

< 2 Mafumu 1 >