< 2 Mafumu 1 >

1 Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
Moab se révolta contre Israël après la mort d’Achab.
2 Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
Achazia tomba par le treillis, de l’étage supérieur de son palais de Samarie, et se blessa grièvement. Il fit partir des émissaires en leur disant: "Allez vous informer auprès de Baal-Zeboub, divinité d’Ekrôn, si j’ai espoir de guérir de ma blessure."
3 Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
Mais un ange du Seigneur dit à Elie le Tisbite: "Va à la rencontre des messagers du roi de Samarie et demande-leur: N’Y a-t-il donc pas de Dieu en Israël, pour que vous alliez consulter Baal-Zeboub, dieu d’Ekrôn?
4 Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
Or, voici la parole de l’Eternel: Tu ne descendras plus du lit où tu es monté, mais certes, tu mourras." Elle obéit.
5 Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
Les messagers retournèrent alors auprès du roi, qui leur dit: "Que signifie votre retour?"
6 Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
lis répondirent: "Un homme est venu à notre rencontre et nous a dit: Retournez auprès du roi qui vous a envoyés, et dites-lui: Ainsi a parlé l’Eternel: N’Y a-t-il donc pas de Dieu en Israël pour que tu envoies consulter Baal-Zeboub, dieu d’Ekrôn? C’Est pourquoi, tu ne redescendras pas du lit où tu es monté, mais certes, tu mourras.
7 Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
Et quels signes distinctifs avait l’homme qui vous a abordés et vous a tenu ce langage? demanda le roi.
8 Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
Cet homme, répondirent-ils, avait un vêtement de poil, et une ceinture de cuir entourait ses reins." Le roi dit: "C’Était Elie le Tisbite."
9 Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
Et il envoya contre lui un chef de cinquante hommes avec sa troupe. Cet officier monta vers le prophète, qui se tenait sur le sommet de ta montagne, et lui dit: "Homme de Dieu, le roi t’ordonne de descendre.
10 Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
Aussi vrai que je suis un homme de Dieu, répondit Elie à l’officier, un feu descendra du ciel et te consumera, toi et tes cinquante hommes." Aussitôt, un feu descendit du ciel, et le consuma avec ses hommes.
11 Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
Le roi envoya un autre capitaine, accompagné de cinquante hommes. Celui-ci dit à son tour à Elie: "Homme de Dieu, par ordre du roi, hâte-toi de descendre."
12 Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
Le prophète répliqua et leur dit: "Aussi vrai que je suis un homme de Dieu, un feu descendra du ciel et te consumera, toi et tes cinquante hommes." Aussitôt un feu descendit du ciel, et le consuma avec ses hommes.
13 Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
Le roi envoya une troisième fois un capitaine à la tête de cinquante hommes. Mais celui-ci, après être monté, se mit à genoux devant Elie, et lui adressa une supplication en disant: "Homme de Dieu, respecte, de grâce, ma vie et celle de ces cinquante hommes, tes serviteurs.
14 Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
Voilà qu’un feu est descendu du ciel et a consumé les deux premiers capitaines avec leurs cinquante hommes; mais maintenant, que ma vie soit sacrée à tes yeux!"
15 Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
Alors un ange du Seigneur dit à Elie: "Descends avec lui, sans rien craindre de sa part." Il descendit avec lui et se rendit auprès du roi,
16 Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
à qui il dit: "Ainsi à parlé l’Eternel: Parce que tu as envoyé des messagers pour interroger Baal-Zeboub, dieu d’Ekrôn, comme s’il n’y avait pas de Dieu en Israël pour consulter son oracle, tu ne descendras plus du lit où tu es monté, mais tu mourras certainement."
17 Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
Il mourut, en effet, comme le Seigneur l’avait annoncé par la bouche d’Elfe. Joram lui succéda, la deuxième année du règne de Joram, fils de Josaphat, roi de Juda; car il n’avait pas de fils.
18 Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Le reste des faits accomplis par Achazia est consigné dans le livre des annales des rois d’Israël.

< 2 Mafumu 1 >