< 2 Mafumu 1 >

1 Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
Moab s'est rebellé contre Israël après la mort d'Achab.
2 Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
Achazia tomba par le treillis dans sa chambre haute qui était à Samarie, et il fut malade. Il envoya des messagers, et leur dit: « Allez consulter Baal Zebub, le dieu d'Ékron, pour savoir si je guérirai de cette maladie. »
3 Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
Mais l'ange de Yahvé dit à Elie le Tishbite: « Lève-toi, monte à la rencontre des messagers du roi de Samarie, et dis-leur: « Est-ce parce qu'il n'y a pas de Dieu en Israël que tu vas consulter Baal Zebub, le dieu d'Ekron?
4 Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
Maintenant, Yahvé dit: « Tu ne descendras pas du lit sur lequel tu es monté, mais tu mourras ». Et Élie s'en alla.
5 Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
Les messagers revinrent vers lui, et il leur dit: « Pourquoi êtes-vous revenus? »
6 Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
Ils lui dirent: « Un homme est monté à notre rencontre et nous a dit: « Allez, retournez vers le roi qui vous a envoyés, et dites-lui: « Yahvé dit: C'est parce qu'il n'y a pas de Dieu en Israël que tu envoies consulter Baal Zebub, le dieu d'Ekron? C'est pourquoi tu ne descendras pas du lit où tu es monté, mais tu mourras certainement.'""
7 Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
Il leur dit: « Quelle sorte d'homme était-ce, qui est venu à votre rencontre et vous a dit ces paroles? »
8 Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
Ils lui répondirent: « C'était un homme velu, et il portait une ceinture de cuir autour de la taille. » Il a dit: « C'est Élie le Tishbite. »
9 Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
Alors le roi envoya vers lui un capitaine de cinquante avec ses cinquante. Il monta vers lui; et voici qu'il était assis sur le sommet de la colline. Il lui dit: « Homme de Dieu, le roi a dit: « Descends! »
10 Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
Élie répondit au chef des cinquante: « Si je suis un homme de Dieu, que le feu descende du ciel et te consume, toi et tes cinquante hommes! ». Le feu descendit du ciel et le consuma, lui et ses cinquante hommes.
11 Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
Il envoya de nouveau vers lui un autre capitaine de cinquante avec ses cinquante. Il lui répondit: « Homme de Dieu, le roi a dit: 'Descends vite'. »
12 Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
Elie leur répondit: « Si je suis un homme de Dieu, que le feu descende du ciel et qu'il vous consume, vous et vos cinquante. » Alors le feu de Dieu descendit du ciel et le consuma, lui et ses cinquante.
13 Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
Il envoya de nouveau le chef d'un troisième cinquante avec ses cinquante. Le troisième chef de cinquante monta, vint se jeter à genoux devant Élie, le supplia et lui dit: « Homme de Dieu, fais que ma vie et celle de ces cinquante de tes serviteurs soient précieuses à tes yeux.
14 Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
Voici que le feu est descendu du ciel et a consumé les deux derniers chefs de cinquante avec leurs cinquante. Mais maintenant, fais que ma vie soit précieuse à tes yeux. »
15 Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
L'ange de Yahvé dit à Elie: « Descends avec lui. N'aie pas peur de lui. » Puis il se leva et descendit avec lui auprès du roi.
16 Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
Il lui dit: « Yahvé dit: « Parce que tu as envoyé des messagers consulter Baal Zebub, le dieu d'Ékron, est-ce parce qu'il n'y a pas de Dieu en Israël pour consulter sa parole? C'est pourquoi tu ne descendras pas du lit où tu es monté, mais tu mourras certainement. »
17 Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
Il mourut donc selon la parole de l'Éternel qu'Élie avait prononcée. Joram commença à régner à sa place la deuxième année de Joram, fils de Josaphat, roi de Juda, car il n'avait pas de fils.
18 Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Le reste des actes d'Achazia, qu'il a accomplis, n'est-il pas écrit dans le livre des Chroniques des rois d'Israël?

< 2 Mafumu 1 >