< 2 Mafumu 1 >
1 Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
Efter Alkahs Død faldt Moab fra Israel.
2 Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
Og Ahazja faldt ud gennem Vinduesgitteret for sin Stue på Taget i Samaria og blev syg; da sendte han Sendebud af Sted og sagde til dem: "Gå hen og spørg Ekrons Gud Ba'al-Zebub, om jeg kommer mig af min Sygdom!"
3 Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
Men HERRENs Engel sagde til Tisjbiten Elias: "Gå Sendebudene fra Samarias Konge i Møde og sig til dem: Mon det er, fordi der ingen Gud er i Israel, at I drager hen for at rådspørge Ekrons Gud Ba'al-Zebub?
4 Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
Derfor, så siger HERREN: Det Leje, du steg op på, kommer du ikke ned fra, thi du skal dø!" Dermed gik Elias bort.
5 Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
Da Sendebudene kom tilbage til ham, spurgte han dem: "Hvorfor kommer I tilbage?"
6 Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
De svarede: "En Mand kom os i Møde og sagde til os: Vend tilbage til Kongen, som har sendt eder, og sig: Så siger HERREN: Mon det er, fordi der ingen Gud er i Israel, at du sender Bud for at rådspørge Ekrons Gud Ba'al-Zebub? Derfor: Det Leje, du steg op på, kommer du ikke ned fra, thi du skal dø!"
7 Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
Han spurgte dem da: "Hvorledes så den Mand ud, som kom eder i Møde og sagde disse Ord til eder?"
8 Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
De svarede: "Det var en Mand i en lådden Kappe med et Læderbælte om Lænderne." Da sagde han: "Det er Tisjbiten Elias."
9 Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
Derpå sendte han en Halvhundredfører med hans halvtredsindstyve Mand ud efter ham; og da han kom op til ham på Bjergets Top, hvor han sad, sagde han til ham: "Du Guds Mand! Kongen byder: Kom ned!"
10 Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
Men Elias svarede Halvhundredføreren: "Er jeg en Guds Mand, så fare Ild ned fra Himmelen og fortære dig og dine halvtredsindstyve Mand!" Da for Ild ned fra Himmelen og fortærede ham og hans halvtredsindstyve Mand.
11 Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
Atter sendte Kongen en Halvhundredfører med hans halvtredsindstyve Mand ud efter ham; og da han kom derop, sagde han til ham: "Du Guds Mand! Således siger Kongen: Kom straks ned!"
12 Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
Men Elias svarede ham: "Er jeg en Guds Mand, så fare Ild ned fra Himmelen og fortære dig og dine halvtredsindstyve Mand!" Da for Guds Ild ned fra Himmelen og fortærede ham og hans halvtredsindstyve Mand.
13 Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
Atter sendte Kongen en Halvhundredfører ud efter ham: men da den tredje Halvhundredfører kom derop, kastede han sig på Knæ for Elias, bønfaldt ham og sagde: "du Guds Mand! Lad dog mit og disse dine halvtredsindstyve Trælles Liv være dyrebarl i dine Øjne!
14 Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
Se, Ild for ned fra Himmelen og fortærede de to første Halvhundredførere og deres halvtredsindstyve Mand, men lad nu mit Liv være dyrebart i dine Øjne!"
15 Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
Da sagde HERRENs Engel til Elias: "Gå ned med ham, frygt ikke for ham!" Så gik han ned med ham og fulgte ham til Kongen.
16 Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
Og han sagde til Kongen: "Så siger HERREN: Fordi du har sendt Sendebud hen at rådspørge Ekrons Gud Ba'al-Zebub - men det er, fordi der ingen Gud er i Israel, du kunde rådspørge? - derfor: Det Leje, du steg op på, kommer du ikke ned fra, thi du skal dø!"
17 Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
Og han døde efter det HERRENs Ord, som Elias havde talt. Og hans Broder Joram blev Konge i hans Sted i Josafats Søns, Kong Joram af Judas, andet Regeringsår; thi han havde ingen Søn.
18 Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Hvad der ellers er at fortælle om Ahazja, hvad han udførte, står jo optegnet i Israels Kongers Krønike.