< 2 Yohane 1 >

1 Ndine mkulu wampingo, kulembera: Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi.
Tape ciimazappe; tumappe ta dosiza doretida godateysinne izi naytas, tana xala gidonta tumu erizayti wuri dosizaris, kitetida kita;
2 Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn g165)
Gasoykka haysi tummay ha7ikka nu giddon dizaysanne sinthafekka medhinas danaysakko. (aiōn g165)
3 Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.
Xoossa awappenne iza na Yesuss Kirstosappe Kiyatethi, marotethiine saroy tumanine siqqon nunara giido.
4 Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira.
Ne naytape bagati aawape nus imetida azazoza mala tuman miini dizayta ta beyida gish daro ufa7istadis.
5 Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake.
Ha7ikka Godateye, kassepeka dizaro attiin ta nes hara ooratha azazo xafikke; hesiikka nu nu garsan siqistanaysakko.
6 Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.
He siqoykka nu iza azazoza mala danaysako. Azazozikka inte koyro siyda mala siqqon deyana malako.
7 Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu.
Yesus Kirstossay asa asho maydi yibeyna giza amanonta daro balethizayti alame bolla laletida. Heyta malay ay assikka as ballethizadene Kirstosara eqetizadeko.
8 Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse.
Inte gidikko inte dabura wagape mella atontamalanne kumetha woyytto ekana mala inte hu7es nagetite.
9 Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana.
Kirstossa timrte mala donta urayinne iza tmirteppe baletidi kare keziza ura oonanikka Xoossi deena. Kirstosa timrten dizadey gidiko izas aawayne aawa nay deetes.
10 Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni.
Oonikka intekko yishe hessa he timrteza ekii yonta ura mokkii ekofiitene saro gopiite.
11 Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.
Moki ekiddii ba so gelthizadey he ura oothon izara isino gidees.
12 Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.
Ta intes xafanas koyza daro miish des shin waraqataninne qalamen xafana mala koyke. Gidiikokka nu ufaysay kumeth gidana mala ta inteko bada inte sinthan intenara hasa7anas ufays oothays.
13 Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.
Doretidari naytii ne miicheyi nayti nena saro geetes.

< 2 Yohane 1 >