< 2 Yohane 1 >

1 Ndine mkulu wampingo, kulembera: Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi.
From the elder to the chosen lady and her children, whom I love in truth—and not only I, but also all those who have known the truth—
2 Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn g165)
because of the truth that remains in us and will be with us forever. (aiōn g165)
3 Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.
Grace, mercy, and peace will be with us from God the Father and from Jesus Christ, the Son of the Father, in truth and love.
4 Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira.
I rejoice greatly that I have found some of your children walking in truth, just as we have received this commandment from the Father.
5 Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake.
Now I plead with you, lady—not as though I were writing to you a new commandment, but one that we have had from the beginning—that we should love one another.
6 Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.
This is love, that we should walk according to his commandments. This is the commandment, just as you heard from the beginning, that you should walk in it.
7 Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu.
For many deceivers have gone out into the world, and they do not confess that Jesus Christ came in the flesh. This is the deceiver and the antichrist.
8 Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse.
Look to yourselves, that you do not lose the things for which we all have worked, but so that you may receive a full reward.
9 Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana.
Whoever goes on ahead and does not remain in the teaching of Christ does not have God. The one who remains in the teaching, this one has both the Father and the Son.
10 Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni.
If anyone comes to you and does not bring this teaching, do not receive him into your house and do not greet him.
11 Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.
For the one who greets him participates in his evil deeds.
12 Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.
I have many things to write to you, but I did not wish to write them with paper and ink. However, I expect to come to you and speak face to face, so that our joy will be complete.
13 Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.
The children of your chosen sister greet you.

< 2 Yohane 1 >