< 2 Akorinto 1 >
1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo, Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.
Paul, an Apostle of Christ Jesus by the will of God--and our brother Timothy: To the Church of God in Corinth, with all God's people throughout Greece.
2 Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
May grace and peace be granted to you from God our Father and the Lord Jesus Christ.
3 Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse.
Heartfelt thanks be to the God and Father of our Lord Jesus Christ--the Father who is full of compassion and the God who gives all comfort.
4 Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu.
He comforts us in our every affliction so that we may be able to comfort those who are in any kind of affliction by means of the comfort with which we ourselves are comforted by God.
5 Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri.
For just as we have more than our share of suffering for the Christ, so also through the Christ we have more than our share of comfort.
6 Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife.
But if, on the one hand, we are enduring affliction, it is for your comfort and salvation; and if, on the other hand, we are receiving comfort, it is for your comfort which is produced within you through your patient fortitude under the same sufferings as those which we also are enduring.
7 Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.
And our hope for you is stedfast; for we know that as you are partners with us in the sufferings, so you are also partners in the comfort.
8 Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo.
For as for our troubles which came upon us in the province of Asia, we would have you know, brethren, that we were exceedingly weighed down, and felt overwhelmed, so that we renounced all hope even of life.
9 Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa.
Nay, we had, as we still have, the sentence of death within our own selves, in order that our confidence may repose, not on ourselves, but on God who raised the dead to life.
10 Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe.
He it is who rescued us from so imminent a death, and will do so again; and we have a firm hope in Him that He will also rescue us in all the future,
11 Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.
while you on your part lend us your aid in entreaty for us, so that from many lips thanksgivings may rise on our behalf for the boon granted to us at the intercession of many.
12 Tsono chonyadira chathu nʼchakuti, chikumbumtima chathu chimatitsimikizira kuti timakhala bwino mʼdziko lapansi, makamaka pa ubale wathu ndi inu. Takhala moona mtima ndi oyera mtima. Sitinachite chomwechi mwa nzeru ya dziko lapansi koma monga mwa chisomo cha Mulungu.
For the reason for our boasting is this--the testimony of our own conscience that it was in holiness and with pure motives before God, and in reliance not on worldly wisdom but on the gracious help of God, that we have conducted ourselves in the world, and above all in our relations with you.
13 Pakuti sitikukulemberani zoti simungawerenge kapena kumvetsetsa.
For we are writing to you nothing different from what we have written before, or from what indeed you already recognize as truth and will, I trust, recognize as such to the very end;
14 Monga mwamva pangʼono chabe, ndikuyembekeza kuti mudzamvetsa kwenikweni, kuti mutha kutinyadira monga ife tidzakunyadirani, pa tsiku la Ambuye Yesu.
just as some few of you have recognized us as your reason for boasting, even as you will be ours, on the day of Jesus our Lord.
15 Popeza ndinatsimikiza mtima za ichi, nʼchifukwa chake ndinafuna kuti poyamba, ndidzakuchezereni kuti mupindule pawiri.
It was because I entertained this confidence that I intended to visit you before going elsewhere--so that you might receive a twofold proof of God's favour--
16 Ndinafuna kuti ndidzakuchezereni pa ulendo wanga wopita ku Makedoniya ndi kudzakuonaninso pochokera ku Makedoniyako kuti inu mudzandithandize pa ulendo wanga wopita ku Yudeya.
and to pass by way of Corinth into Macedonia. Then my plan was to return from Macedonia to you, and be helped forward by you to Judaea.
17 Kodi pamene ndinkakonzekera zimenezi, mukuganiza kuti ndinkachita mwachibwana? Kapena kuti ndinkaganiza ngati mwa dziko lapansi; kuti ndikhoza kumanena kuti, “Inde, Inde,” nthawi yomweyo nʼkumatinso “Ayi, Ayi?”
Did I display any vacillation or caprice in this? Or the purposes which I form--do I form them on worldly principles, now crying "Yes, yes," and now "No, no"?
18 Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.”
As certainly as God is faithful, our language to you is not now "Yes" and now "No."
19 Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.”
For Jesus Christ the Son of God--He who was proclaimed among you by us, that is by Silas and Timothy and myself--did not show Himself a waverer between "Yes" and "No." But it was and always is "Yes" with Him.
20 Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu.
For all the promises of God, whatever their number, have their confirmation in Him; and for this reason through Him also our "Amen" acknowledges their truth and promotes the glory of God through our faith.
21 Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife,
But He who is making us as well as you stedfast through union with the Anointed One, and has anointed us, is God,
22 nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.
and He has also set His seal upon us, and has put His Spirit into our hearts as a pledge and foretaste of future blessing.
23 Mulungu ndi mboni yanga kuti sindinabwererenso ku Korinto kuno kuti ndisakumvetseni chisoni.
But as for me, as my soul shall answer for it, I appeal to God as my witness, that it was to spare you pain that I gave up my visit to Corinth.
24 Sikuti ife tikufuna kukhala olamulira chikhulupiriro chanu, koma timagwira nanu ntchito pamodzi kuti mukhale achimwemwe, chifukwa ndinu okhazikika kwambiri mʼchikhulupiriro.
Not that we want to lord it over you in respect of your faith--we do, however, desire to help your joy--for in the matter of your faith you are standing firm.