< 2 Akorinto 8 >

1 Ndipo tsopano, abale, tikufuna kuti mudziwe za chisomo chimene Mulungu wapereka ku mipingo ya ku Makedoniya.
Men vi kundgøre eder, Brødre! den Guds Nåde, som er given i Makedoniens Menigheder,
2 Pakati pa mayesero owawitsa, chimwemwe chawo chosefukira ndi umphawi wawo otheratu, anapereka mowolowamanja kwambiri.
at under megen Trængsels Prøvelse har deres overstrømmende Glæde og deres dybe Fattigdom strømmet over i deres Gavmildheds Rigdom.
3 Motero ndikuchitira umboni kuti anapereka mmene akanathera, ndipo mwinanso kuposera mmene akathera kupereka. Anapereka mosakakamizidwa,
Thi efter Evne (det vidner jeg) gave de, ja, over Evne af egen Drift,
4 ndipo anatipempha motiwumiriza kuti tiwapatse mwayi woti nawonso athandize anthu oyera mtima a ku Yudeya.
idet de med megen Overtalelse bade os om den Nåde at måtte tage Del i Hjælpen til de hellige,
5 Iwo anachita moposera mmene ife timayembekezera. Choyamba anadzipereka kwa Ambuye ndipo kenaka kwa ife monga mwa chifuniro cha Mulungu.
og ikke alene som vi havde håbet, men sig selv gav de først og fremmest til Herren og så til os, ved Guds Villie,
6 Choncho tinamupempha Tito kuti atsirize poti nʼkuti atayamba kale ntchito yachisomoyi pakati panu.
så at vi opfordrede Titus til, ligesom han forhen havde begyndt, således også til at tilendebringe hos eder også denne Gave.
7 Popeza pa zinthu zonse munachita bwino, monga pachikhulupiriro, poyankhula, pachidziwitso, pakhama lambiri ndi pachikondi chanu pa ife, onetsetsani kuti muchitenso bwino pachisomo ichi chopereka.
Men ligesom I ere rige i alt, i Tro og Tale og Erkendelse og al Iver og i eders Kærlighed til os: måtte I da være rige også i denne Gave!
8 Sindikukulamulirani, koma ndikufuna kuona ngati chikondi chanu nʼchoona pofananitsa ndi changu cha anthu ena.
Jeg siger det ikke som en Befaling, men for ved andres Iver at prøve også eders Kærligheds Ægthed.
9 Pakuti mukudziwa chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemera, koma chifukwa cha inuyo anasanduka wosauka, kuti umphawi wakewo, inuyo mulemere.
I kende jo vor Herres Jesu Kristi Nåde, at han for eders Skyld blev fattig, da han var rig, for at I ved hans Fattigdom skulde blive rige.
10 Ndipo nawa malangizo anga pa zoyenera inu kuchita pa nkhaniyi. Chaka chatha munali oyamba, osati ongofuna kupereka kokha komanso okhala ndi mtima ofuna kupereka.
Og jeg giver min Mening herom til Kende; thi dette er eder gavnligt, I, som jo i Fjor vare de første til at begynde, ikke alene med Gerningen, men endogså med Villien dertil.
11 Tsopano tsirizani ntchitoyi, ndipo changu chanu chofunitsitsa kugwira ntchitoyi ndi kuyitsiriza chichitike molingana ndi zimene muli nazo.
Men fuldbringer da nu også Gerningen, for at, ligesom I vare redebonne til at ville, I også må fuldbringe det efter eders Evne.
12 Ndipo ngati mtima ofunitsitsa ulipo, mphatsoyo imalandiridwa molingana ndi zimene munthuyo ali nazo, osati zimene alibe.
Thi når Redebonheden er til Stede, da er den velbehagelig efter, hvad den evner, ikke efter, hvad den ikke evner.
13 Cholinga chathu sikuti tipeputse ena pamene inuyo mukuvutika, koma kuti pakhale kufanana.
Det er nemlig ikke Meningen, at andre skulle have Lettelse og I Trængsel; nej, det skal være ligeligt. Nu for Tiden må eders Overflod komme hines Trang til Hjælp,
14 Zambiri zimene muli nazo pakati panu muthandize nazo osowa, kuti nawonso akadzakhala nazo zambiri adzakuthandizeni pa zosowa zanu. Cholinga nʼkuchita mofanana,
for at også hines Overflod kan komme eders Trang til Hjælp, for at der kan blive Ligelighed,
15 monga kwalembedwa kuti, “Iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere.”
som der er skrevet: "Den, som sankede meget, fik ikke for meget, og den, som sankede lidet, fik ikke for lidt."
16 Tithokoze Mulungu amene anayika mu mtima wa Tito changu chomwecho chimene ine ndili nacho pa inu.
Men Gud ske Tak, som giver den samme Iver for eder i Titus's Hjerte!
17 Pakuti Tito sanangovomera kokha pempho lathu, koma yekha anafunitsitsa kwambiri kubwera kwa inu mwa iye yekha.
Thi vel har han modtaget min Opfordring; men da han er så ivrig, så er det af egen Drift, at han rejser til eder.
18 Ndipo tikumutumiza pamodzi ndi mʼbale amene mipingo yonse yamuyamikira chifukwa cha utumiki wake wa Uthenga Wabwino.
Og sammen med ham sende vi den Broder, hvis Ros i Evangeliet går igennem alle Menighederne,
19 Chowonjezera china nʼchakuti anasankhidwa ndi mipingo kuti atiperekeze pamene ife tikukapereka zopereka, zimene tikuchita pofuna kupereka ulemu kwa Ambuye mwini ndi kuonetsa kufunitsitsa kwathu pothandiza.
og ikke det alene, men han er også udvalgt af Menighederne til at rejse med os med denne Gave, som besørges af os, for at fremme selve Herrens Ære og vor Redebonhed,
20 Tikufuna kupewa kutikayikira kulikonse za mmene tikuyendetsera mphatso zochulukazi.
idet vi undgå dette, at nogen skulde kunne laste os i Anledning af denne rige Hjælp, som besørges af os;
21 Pakuti tikuyesetsa kuchita zolondola, osati pamaso pa Ambuye pokha komanso pamaso pa anthu.
thi vi lægge Vind på, hvad der er godt ikke alene i Herrens, men også i Menneskers Øjne.
22 Kuwonjezera apo, tikuwatumiza pamodzi ndi mʼbale wathu, amene nthawi zambiri watitsimikizira mʼnjira zosiyanasiyana kuti ndi wachangu ndiponso chifukwa ali ndi chikhulupiriro chachikulu mwa inu.
Men sammen med dem sende vi vor Broder, hvis Iver vi ofte i mange Måder have prøvet, men som nu er langt ivrigere på Grund af sin støre Tillid til eder.
23 Kunena za Tito, ndiye mnzanga ndi wogwira naye ntchito pakati panu. Kunena za abale athu, ndiwo oyimirira mipingo ndi olemekezetsa Khristu.
Hvad Titus angår, da er han min Fælle og Medarbejder hos eder, og hvad vore Brødre angår, da ere de Menighedsudsendinge, Kristi Ære.
24 Choncho anthu amenewa atsimikizireni za chikondi chanu ndipo adziwe chifukwa chimene ife timakunyadirani, kuti mipingo yonse iwone chimenechi.
Så giver dem da for Menighedernes Åsyn Beviset på eders Kærlighed og for det, vi have rost eder for.

< 2 Akorinto 8 >