< 2 Akorinto 8 >
1 Ndipo tsopano, abale, tikufuna kuti mudziwe za chisomo chimene Mulungu wapereka ku mipingo ya ku Makedoniya.
Musím vám teď povědět, jak ohromně zapůsobila Boží milost v křesťanských obcích v Makedonii.
2 Pakati pa mayesero owawitsa, chimwemwe chawo chosefukira ndi umphawi wawo otheratu, anapereka mowolowamanja kwambiri.
Ačkoliv se tam museli potýkat s všelijakými nesnázemi a podstoupit nejednu tvrdou zkoušku, byla radost věřících tak veliká, že při vší své chudobě sebrali mezi sebou neuvěřitelnou částku.
3 Motero ndikuchitira umboni kuti anapereka mmene akanathera, ndipo mwinanso kuposera mmene akathera kupereka. Anapereka mosakakamizidwa,
Nedávali jen to, co jim přebývalo, ale daleko víc.
4 ndipo anatipempha motiwumiriza kuti tiwapatse mwayi woti nawonso athandize anthu oyera mtima a ku Yudeya.
Pokládali to za vyznamenání, že se mohli podílet na sbírce pro jeruzalémské křesťany.
5 Iwo anachita moposera mmene ife timayembekezera. Choyamba anadzipereka kwa Ambuye ndipo kenaka kwa ife monga mwa chifuniro cha Mulungu.
Jejich obětavost předstihla všechna moje očekávání – tak úplně se dali k dispozici Bohu a v jeho jménu i nám.
6 Choncho tinamupempha Tito kuti atsirize poti nʼkuti atayamba kale ntchito yachisomoyi pakati panu.
Proto jsem požádal Tita, který u vás začal organizovat sbírku už dříve, aby se k vám znovu vypravil a pomohl vám toto dílo lásky dokončit.
7 Popeza pa zinthu zonse munachita bwino, monga pachikhulupiriro, poyankhula, pachidziwitso, pakhama lambiri ndi pachikondi chanu pa ife, onetsetsani kuti muchitenso bwino pachisomo ichi chopereka.
Není nic, čeho by se vám nedostávalo: víra, účinné slovo, poznání, dobrá vůle i vřelý vztah k nám – ve všem můžete být dáváni za vzor. Doufám, že i váš příspěvek k této službě lásky bude stejně příkladný.
8 Sindikukulamulirani, koma ndikufuna kuona ngati chikondi chanu nʼchoona pofananitsa ndi changu cha anthu ena.
Neberte to jako příkaz. Přál bych si jen, abyste dokázali svou lásku stejně horlivě.
9 Pakuti mukudziwa chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, kuti ngakhale anali wolemera, koma chifukwa cha inuyo anasanduka wosauka, kuti umphawi wakewo, inuyo mulemere.
Jistě jste nezapomněli, co pro vás udělal Kristus: sám bohatý, kvůli vám vzal na sebe dobrovolně chudobu, abyste vy jeho chudobou zbohatli.
10 Ndipo nawa malangizo anga pa zoyenera inu kuchita pa nkhaniyi. Chaka chatha munali oyamba, osati ongofuna kupereka kokha komanso okhala ndi mtima ofuna kupereka.
Měli byste tedy ten nápad, který se zrodil u vás, dotáhnout až do konce. Když jste začali s takovým nadšením, nepolevujte nyní a ochotně dávejte, kolik můžete. Kdo více dát nemůže, ať se netrápí. Bohu záleží na ochotě, a ne na velikosti daru.
11 Tsopano tsirizani ntchitoyi, ndipo changu chanu chofunitsitsa kugwira ntchitoyi ndi kuyitsiriza chichitike molingana ndi zimene muli nazo.
12 Ndipo ngati mtima ofunitsitsa ulipo, mphatsoyo imalandiridwa molingana ndi zimene munthuyo ali nazo, osati zimene alibe.
13 Cholinga chathu sikuti tipeputse ena pamene inuyo mukuvutika, koma kuti pakhale kufanana.
Nejde o to, aby si jiní mohli dopřávat na váš účet. Ale jestliže se vám nyní vede lépe, rozdělte se s potřebnějšími. Vždyť oni mohou zase pomoci vám, když se situace změní. Tak budete mít každý právě tolik, kolik potřebujete,
14 Zambiri zimene muli nazo pakati panu muthandize nazo osowa, kuti nawonso akadzakhala nazo zambiri adzakuthandizeni pa zosowa zanu. Cholinga nʼkuchita mofanana,
15 monga kwalembedwa kuti, “Iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere.”
jak čteme v Písmu o Izraelcích sbírajících pokrm na poušti: „Kdo nashromáždil více, tomu nepřebývalo, kdo nasbíral méně, neměl nedostatek.“
16 Tithokoze Mulungu amene anayika mu mtima wa Tito changu chomwecho chimene ine ndili nacho pa inu.
Jsem vděčný Bohu za to, že Titus k vám přilnul stejně jako já.
17 Pakuti Tito sanangovomera kokha pempho lathu, koma yekha anafunitsitsa kwambiri kubwera kwa inu mwa iye yekha.
Můj návrh hned s radostí přijal, ale myslím, že by byl tak jako tak využil první příležitosti vydat se opět k vám.
18 Ndipo tikumutumiza pamodzi ndi mʼbale amene mipingo yonse yamuyamikira chifukwa cha utumiki wake wa Uthenga Wabwino.
Posílám s ním ještě jednoho bratra, kterého si pro jeho oddanost ve službě Kristu váží ve všech církvích.
19 Chowonjezera china nʼchakuti anasankhidwa ndi mipingo kuti atiperekeze pamene ife tikukapereka zopereka, zimene tikuchita pofuna kupereka ulemu kwa Ambuye mwini ndi kuonetsa kufunitsitsa kwathu pothandiza.
Byl vybrán, aby mě doprovázel do Jeruzaléma s výtěžkem sbírky, jež má oslavit našeho Pána a veřejně prokázat naši horlivost k službě.
20 Tikufuna kupewa kutikayikira kulikonse za mmene tikuyendetsera mphatso zochulukazi.
Předejde se tak možným pozdějším dohadům, zda se opravdu všechny peníze dostaly tam, kam byly určeny.
21 Pakuti tikuyesetsa kuchita zolondola, osati pamaso pa Ambuye pokha komanso pamaso pa anthu.
Bůh ví, že nikoho z nás by ani ve snu nenapadlo zpronevěřit jediný haléř, ale abychom vyloučili i sebenepatrnější podezření, zařídili jsme to raději takto.
22 Kuwonjezera apo, tikuwatumiza pamodzi ndi mʼbale wathu, amene nthawi zambiri watitsimikizira mʼnjira zosiyanasiyana kuti ndi wachangu ndiponso chifukwa ali ndi chikhulupiriro chachikulu mwa inu.
Doprovází je ještě další bratr, mnohokrát již osvědčený jako upřímný křesťan. Těší se k vám, protože jsem mu vyprávěl o vašem nadšení pro pomoc druhým. Přijměte je tedy všechny přívětivě.
23 Kunena za Tito, ndiye mnzanga ndi wogwira naye ntchito pakati panu. Kunena za abale athu, ndiwo oyimirira mipingo ndi olemekezetsa Khristu.
Titus je v této věci mým zplnomocněným zástupcem. Je to můj nejbližší spolupracovník. Ostatní dva vyslaly zdejší církve jako své nejlepší představitele.
24 Choncho anthu amenewa atsimikizireni za chikondi chanu ndipo adziwe chifukwa chimene ife timakunyadirani, kuti mipingo yonse iwone chimenechi.
Ukažte jim, že všechny moje chvály na vás nebyly plané.