< 2 Akorinto 7 >
1 Abwenzi okondedwa, popeza tili ndi malonjezo amenewa, tiyeni tidziyeretse, kusiyana nazo zilizonse zimene zikhoza kudetsa thupi ndi mzimu, ndipo tiyesetse kukhala oyera mtima poopa Mulungu.
Having therefore, my beloved, these promises, let us purify ourselves from all defilement of flesh and spirit, perfecting holiness in the fear of God.
2 Mutipatse malo mʼmitima mwanu. Ife sitinalakwire munthu aliyense, kapena kuyipitsa munthu aliyense, kapena kumuchenjerera munthu aliyense.
Receive us---we have injured no man, we have corrupted no one, we have over-reached no one.
3 Sindikunena izi kuti mupezeke olakwa. Ndinanena kale kuti ife timakuganizirani kwambiri kotero kuti tili pamodzi, ngakhale tikhale moyo kapena timwalire.
I speak not this to condemn you: for I said before that ye are so much in our hearts that we could live and die with you.
4 Ndimakukhulupirirani kwambiri ndipo ndimakunyadirani kwambiri. Ndikulimbikitsidwa kwambiri; mʼmasautso athu onse, chimwemwe changa chilibe malire.
I use much freedom of speech to you, and I boast much of you: I am filled with comfort, and superabound in joy above all our affliction.
5 Pakuti titafika ku Makedoniya, sitinapume nʼkomwe, koma tinavutitsidwa mbali zonse. Kunja kunali mikangano, ndipo mʼmitima mwathu munali mantha.
For when we came into Macedonia, our flesh had no rest, but we were afflicted on every side; without were fightings, within were fears.
6 Koma Mulungu, amene amatonthoza mtima wopsinjika, anatitonthoza mtima ndi kufika kwa Tito,
But God, who comforteth those that are brought low, comforted us by the coming of Titus:
7 sikubwera kwake kokhako, komanso mawu achilimbikitso amene analandira kuchokera kwa inu. Iye anatiwuza kuti mukufuna kundiona, zachisoni chanu chachikulu, ndi kudzipereka kwanu kwa ine, motero chimwemwe changa chinachuluka kuposa kale.
and not only by his coming, but especially by the consolation wherewith he was comforted on your account, acquainting us with your earnest desire towards us, your grief, and your zeal for me; so that I rejoiced greatly.
8 Ngakhale kalata yanga ija inakupwetekani mtima, sindikudandaula kuti ndinalemberanji. Ngakhale zinandikhudza, ndikudziwa kuti kalata yanga inakupwetekani, koma kwa kanthawi kochepa.
For though I grieved you by my letter, I do not repent, though I did repent; for I perceive that that epistle grieved you, though it was but for a little while.
9 Koma tsopano ndine wokondwa, osati chifukwa chakuti kalatayo inakupwetekani, koma chifukwa chakuti chisoni chanu chinakuthandizani kutembenuka mtima. Pakuti munamva chisoni monga mmene Mulungu amafunira, choncho simunapwetekedwe mwanjira iliyonse.
However, now I rejoice, not that ye were made sorry, but that ye sorrowed to repentance; for ye were grieved after a godly manner, so that ye received no damage from us.
10 Chisoni chimene Mulungu amafuna chimabweretsa kutembenuka mtima komwe kumabweretsa chipulumutso, ndipo sichikhumudwitsa. Koma chisoni cha dziko lapansi chimabweretsa imfa.
For godly sorrow worketh repentance to salvation not to be repented of: but the sorrow of the world worketh death.
11 Taonani zimene chisoni chimene Mulungu amafuna chatulutsa mwa inu. Chatulutsa khama lalikulu, chakuthandizani kuti mudzikonze nokha, chakukwiyitsani kwambiri, komanso chakupatsani mantha aakulu. Chakuchititsani kuti mufune kundiona ine, mwakhudzidwa kwambiri ndipo mukufuna kuonetsetsa kuti chilungamo chachitikadi. Pa nkhani yonseyi, mwaonetsadi kuti ndinu osalakwa.
For behold this very thing, that ye sorrowed after a godly manner, what diligence it wrought in you! yea, what apology, what indignation, what fear, what earnest desire, what zeal, what revenge! by all which ye have shewn yourselves to be clear in the affair.
12 Choncho ngakhale ndinakulemberani kalata ija, sindinayilembe ndi chifukwa cha amene analakwayo kapena wolakwiridwa, koma ndinayilemba kuti inuyo muone kudzipereka kwanu kwa ife pamaso a Mulungu.
Wherefore if I wrote in such a manner to you, it was not merely on his account who had done the wrong, nor for his sake who had been injured; but that our care for you in the sight of God might be manifested among you.
13 Zimenezi zatilimbikitsa kwambiri. Kuwonjezera pa zotilimbikitsazo, tinakondwa kwambiri poona chisangalalo cha Tito, chifukwa nonsenu munamuthandiza kukhazikitsa mtima wake pansi.
We were therefore comforted by your consolation; and rejoiced the more at the joy of Titus, because his spirit was refreshed by you all;
14 Ndinamuwuza kuti ndimakunyadirani, ndipo simunandichititse manyazi. Koma monga zonse zimene tinakuwuzani zinali zoona, tsono zomwe ndinawuza Tito zokunyadirani zinali zoona.
and because if I boasted of any thing to him concerning you, I was not ashamed; but as we have spoken all things to you in truth, so likewise our boasting of you to Titus was truth.
15 Ndipo chikondi chake pa inu nʼchachikulu kwambiri akakumbukira kuti nonse munali omvera, munamulandira ndi mantha ndi kunjenjemera.
And his bowels are exceedingly moved towards you, when he calls to mind the obedience of you all, how with fear and trembling ye received him.
16 Ndine wokondwa kuti ndingathe kukukhulupirirani pa zonse.
I rejoice therefore that in every thing I have confidence in you.