< 2 Akorinto 7 >
1 Abwenzi okondedwa, popeza tili ndi malonjezo amenewa, tiyeni tidziyeretse, kusiyana nazo zilizonse zimene zikhoza kudetsa thupi ndi mzimu, ndipo tiyesetse kukhala oyera mtima poopa Mulungu.
Derfor, efterdi vi have disse Forjættelser, I elskede! så lader os rense os selv fra al Kødets og Åndens Besmittelse, så vi gennemføre Hellighed i Guds Frygt!
2 Mutipatse malo mʼmitima mwanu. Ife sitinalakwire munthu aliyense, kapena kuyipitsa munthu aliyense, kapena kumuchenjerera munthu aliyense.
Giver os Rum; ingen have vi gjort Uret, ingen ødelagt, ingen bedraget.
3 Sindikunena izi kuti mupezeke olakwa. Ndinanena kale kuti ife timakuganizirani kwambiri kotero kuti tili pamodzi, ngakhale tikhale moyo kapena timwalire.
Jeg siger det ikke for at fælde Dom; jeg har jo sagt tilforn, at I ere i vore Hjerter, så at vi dø sammen og leve sammen.
4 Ndimakukhulupirirani kwambiri ndipo ndimakunyadirani kwambiri. Ndikulimbikitsidwa kwambiri; mʼmasautso athu onse, chimwemwe changa chilibe malire.
Jeg har stor Frimodighed over for eder; jeg roser mig meget af eder, jeg er fuld af Trøst, jeg strømmer over af Glæde under al vor Trængsel.
5 Pakuti titafika ku Makedoniya, sitinapume nʼkomwe, koma tinavutitsidwa mbali zonse. Kunja kunali mikangano, ndipo mʼmitima mwathu munali mantha.
Thi også da vi kom til Makedonien, havde vort Kød ingen Ro, men vi trængtes på alle Måder: udadtil Kampe, indadtil Angster.
6 Koma Mulungu, amene amatonthoza mtima wopsinjika, anatitonthoza mtima ndi kufika kwa Tito,
Men han, som trøster de nedbøjede, Gud, han trøstede os ved Titus's Komme;
7 sikubwera kwake kokhako, komanso mawu achilimbikitso amene analandira kuchokera kwa inu. Iye anatiwuza kuti mukufuna kundiona, zachisoni chanu chachikulu, ndi kudzipereka kwanu kwa ine, motero chimwemwe changa chinachuluka kuposa kale.
dog ikke alene ved hans Komme, men også ved den Trøst, hvormed han var bleven trøstet over eder, idet han fortalte os om eders Længsel, eders Gråd, eders Nidkærhed for mig, så at jeg glædede mig end mere.
8 Ngakhale kalata yanga ija inakupwetekani mtima, sindikudandaula kuti ndinalemberanji. Ngakhale zinandikhudza, ndikudziwa kuti kalata yanga inakupwetekani, koma kwa kanthawi kochepa.
Thi om jeg end har bedrøvet eder ved Brevet, fortryder jeg det ikke. Om jeg også har fortrudt det, - jeg ser jo, at hint Brev, ihvorvel kun til en Tid, har bedrøvet eder, -
9 Koma tsopano ndine wokondwa, osati chifukwa chakuti kalatayo inakupwetekani, koma chifukwa chakuti chisoni chanu chinakuthandizani kutembenuka mtima. Pakuti munamva chisoni monga mmene Mulungu amafunira, choncho simunapwetekedwe mwanjira iliyonse.
så glæder jeg mig nu, ikke over, at I bleve bedrøvede, men over, at I bleve bedrøvede til Omvendelse; thi I bleve bedrøvede efter Guds Sind, for at I ikke i nogen Måde skulde lide Skade af os.
10 Chisoni chimene Mulungu amafuna chimabweretsa kutembenuka mtima komwe kumabweretsa chipulumutso, ndipo sichikhumudwitsa. Koma chisoni cha dziko lapansi chimabweretsa imfa.
Thi den Bedrøvelse, der er efter Guds Sind, virker Omvendelse til Frelse, som ikke fortrydes; men Verdens Bedrøvelse virker Død.
11 Taonani zimene chisoni chimene Mulungu amafuna chatulutsa mwa inu. Chatulutsa khama lalikulu, chakuthandizani kuti mudzikonze nokha, chakukwiyitsani kwambiri, komanso chakupatsani mantha aakulu. Chakuchititsani kuti mufune kundiona ine, mwakhudzidwa kwambiri ndipo mukufuna kuonetsetsa kuti chilungamo chachitikadi. Pa nkhani yonseyi, mwaonetsadi kuti ndinu osalakwa.
Thi se, just dette, at I bleve bedrøvede efter Guds Sind, hvor stor en Iver virkede det ikke hos eder, ja Forsvar, ja Harme, ja Frygt, ja Længsel, ja Nidkærhed, ja Straf! På enhver Måde beviste I, at I selv vare rene i den Sag.
12 Choncho ngakhale ndinakulemberani kalata ija, sindinayilembe ndi chifukwa cha amene analakwayo kapena wolakwiridwa, koma ndinayilemba kuti inuyo muone kudzipereka kwanu kwa ife pamaso a Mulungu.
Altså, når jeg skrev til eder, var det ikke for hans Skyld, som gjorde Uret, ikke heller for hans Skyld, som led Uret, men for at eders Iver for os skulde blive åbenbar hos eder for Guds Åsyn.
13 Zimenezi zatilimbikitsa kwambiri. Kuwonjezera pa zotilimbikitsazo, tinakondwa kwambiri poona chisangalalo cha Tito, chifukwa nonsenu munamuthandiza kukhazikitsa mtima wake pansi.
Derfor ere vi blevne trøstede. Men til vor Trøst kom end yderligere Glæden over Titus's Glæde, fordi hans Ånd har fået Vederkvægelse fra eder alle.
14 Ndinamuwuza kuti ndimakunyadirani, ndipo simunandichititse manyazi. Koma monga zonse zimene tinakuwuzani zinali zoona, tsono zomwe ndinawuza Tito zokunyadirani zinali zoona.
Thi i hvad jeg end har rost mig af eder for ham, er jeg ikke bleven til Skamme; men ligesom vi i alle Ting have talt Sandhed til eder, således er også vor Ros for Titus bleven Sandhed.
15 Ndipo chikondi chake pa inu nʼchachikulu kwambiri akakumbukira kuti nonse munali omvera, munamulandira ndi mantha ndi kunjenjemera.
Og hans Hjerte drages inderligere til eder, når han mindes Lydigheden hos eder alle, hvorledes I modtoge ham med Frygt og Bæven.
16 Ndine wokondwa kuti ndingathe kukukhulupirirani pa zonse.
Jeg glæder mig over, at jeg i alt kan lide på eder.