< 2 Akorinto 6 >
1 Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe.
Ja, vi såsom medhjelpare förmane eder, att I icke undfången Guds nåd fåfängt.
2 Pakuti akunena kuti, “Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera, ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza. Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”
Ty han säger: Jag hafver bönhört dig i behagelig tid, och jag hafver hulpit dig på salighetenes dag: Si, nu är den behageliga tiden; si, nu är salighetens dag.
3 Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke.
Låter oss ingom i någor måtto förargelse gifva, på det vårt ämbete må ostraffadt blifva;
4 Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa.
Utan låter oss i all ting bevisa oss såsom Guds tjenare; i stort tålamod, i bedröfvelse, i nöd, i ångest;
5 Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya;
I slag, i fängelse, i uppror, i arbete, i vako, i fasto;
6 pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi
I renlefnad, i förstånd, i långmodighet, i mildhet, i den Helga Anda, i en oskrymtad kärlek;
7 ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo.
I sanningenes ord, i Guds kraft, genom rättfärdighetenes vapen till högra sidon, och till den venstra;
8 Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza.
Genom äro och smälek, genom ondt rykte och godt rykte; såsom bedragare, och dock sannfärdige;
9 Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa.
Såsom okände, och dock kände; såsom de der dö, och si, vi lefvom; såsom näpste, och dock icke dräpne;
10 Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.
Såsom bedröfvade, och dock alltid glade; såsom fattige, och dock många rika görande; såsom intet hafvande, och dock all ting ägande.
11 Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu.
O I Corinthier, vår mun hafver öppnat sig till eder; vårt hjerta är gladt.
12 Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife.
För våra skull behöfven I icke ängslas; men att I ängslens, det gören I af en hjertelig mening.
13 Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.
Jag talar med eder såsom med min barn, att I ock så ställen eder emot mig; och varer ock så glade.
14 Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima?
Drager icke uti främmande ok med de otrogna; ty hvad hafver rättfärdigheten beställa med orättfärdighetene? Eller hvad delaktighet hafver ljuset med mörkret?
15 Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira?
Eller huru förlika sig Christus och Belial? Eller hvad del hafver den trogne med dem otrogna?
16 Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti, “Ndidzakhala mwa iwo ndipo ndidzayendayenda pakati pawo, ndipo ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo adzakhala anthu anga.”
Eller huru kommer Guds tempel öfverens med afgudar? Ty I ären lefvandes Guds tempel, såsom Gud säger: Jag vill bo uti dem, och vandra uti dem; och jag vill vara deras Gud, och de skola vara mitt folk.
17 Nʼchifukwa chake “Tulukani pakati pawo ndi kudzipatula, akutero Ambuye. Musakhudze chodetsedwa chilichonse, ndipo ndidzakulandirani.”
Derföre går ut ifrå dem, och skiljens ifrå dem, säger Herren, och kommer intet vid det orent är; och så skall jag undfå eder;
18 Ndipo “Ndidzakhala Atate anu, ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi, akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”
Och vara edar Fader, och I skolen vara mine söner och döttrar, säger allsvåldige Herren.