< 2 Akorinto 2 >

1 Kotero ndinatsimikiza maganizo anga kuti ndisachitenso ulendo wina owawa wobwera kwanuko.
А я постановив у собі те, щоб до вас не прийти знов у смутку.
2 Pakuti ngati ndikumvetsani chisoni, kodi angandisangalatse ndani, kupatula inuyo amene ndakumvetsani chisoni?
Бо коли я засму́чую вас, то хто той, хто потішить мене, як не той, кого я засмути́в?
3 Nʼchifukwa chake ndinakulemberani monga ndinachitiramo kuti nditabwera kwanuko ndisadzamve chisoni ndi anthu oyenera kundisangalatsa. Ndinali ndi chikhulupiriro ndi inu nonse kuti inuyo mukakhala ndi chimwemwe poona kuti inenso ndili ndi chimwemwe.
І це саме писав я до вас, щоб, прийшовши, я смутку не мав би від тих, що від них мені тішитися нале́жало, про всіх вас бувши певний, що радість моя — то радість усіх вас!
4 Pakuti ndinakulemberani kalata ija ndili wopsinjika ndi wowawidwa mtima kwambiri ndi kutuluka misozi yambiri, osati pofuna kukumvetsani chisoni koma kuti ndikudziwitseni kuti ndimakukondani kwambiri.
Бо з великого горя та з ту́ги сердечної я написав вам з рясни́ми слізьми́ не на те, щоб були ви засму́чені, але щоб пізнали любов, що в мене її пребагато до вас!
5 Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera.
А як хто засмутив, не мене засмутив, а поча́сти — щоб не пригніти́ти — і всіх вас.
6 Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira.
До́сить такому кара́ння того, що від багатьох,
7 Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima.
через те навпаки́, — краще простити й поті́шити, щоб смуток великий його не поже́р.
8 Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye.
Через те вас благаю: зміцніть до нього любов!
9 Cholinga china chimene ndinakulemberani kalata ija chinali chofuna kukuonani ngati mudzandimvera pa zonse.
Бо на це я й писав, щоб пізнати ваш до́свід, чи в усім ви слухня́ні.
10 Aliyense amene mumukhululukire, inenso ndimukhululukira. Ndipo ndikakhululukira, ngati pali kanthu koti ndikhululukire, ndiye kuti ndakhululuka chifukwa cha inu pamaso pa Khristu,
А кому ви прощаєте що, тому й я; бо й я, як простив що кому, то кому я простив, зробив те через вас від Особи Христа,
11 kupewa kuti Satana angapezere mpata pa ife, pajatu timadziwa machenjerero ake.
щоб нас сатана не перехитрував, — відо́мі бо нам його задуми!
12 Tsono nditafika ku Trowa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Khristu, nʼkupeza kuti Ambuye anditsekulira khomo,
А коли я прийшов до Троа́ди звіщати Христову Єва́нгелію, і були двері для мене відчинені в Господі,
13 ndinasowa mtendere mu mtima mwanga, chifukwa sindinapezeko mʼbale wanga Tito. Choncho ndinatsanzikana ndi anthu kumeneko nʼkupita ku Makedoniya.
не мав я споко́ю для духа свого, бо я не знайшов був свого брата Тита; але, попрощавшися з ними, я пішов в Македонію.
14 Koma tithokoze Mulungu amene amatitsogolera nthawi zonse monga ogwidwa ku nkhondo a Khristu pa chipambano chake. Tsono amatigwiritsa ntchito yofalitsa ponseponse nzeru zodziwira Khristu ngati fungo labwino.
А Богові подяка, що Він постійно чинить нас переможцями в Христі, і запа́шність знання́ про Себе через нас виявляє на всякому місці!
15 Pakuti kwa Mulungu ndife fungo labwino la Khristu pakati pa iwo amene akupulumutsidwa ndi amene akuwonongeka.
Ми бо для Бога Христова запа́шність серед тих, хто спасається, і тих, які гинуть,
16 Kwa amene akuwonongeka ndife fungo la imfa, limawapha. Ndipo kwa amene akupulumuka ndife fungo lamoyo, limawapatsa moyo. Ndani angayithe ntchito yotereyi?
для одних бо смертельна запа́шність на смерть, а для других запа́шність життє́ва в життя. І хто здатен на це?
17 Kusiyana ndi ena ambiri, ife sitilalikira Mawu a Mulungu kuti tipeza phindu. Mʼmalo mwake, ife mwa Khristu timayankhula pamaso pa Mulungu moona mtima, monga anthu otumidwa ndi Mulungu.
Бо ми не такі, як багато-хто, що Боже Слово фальшують, але ми провіщаємо, як із щирости, як від Бога, перед Богом, у Христі!

< 2 Akorinto 2 >