< 2 Akorinto 2 >

1 Kotero ndinatsimikiza maganizo anga kuti ndisachitenso ulendo wina owawa wobwera kwanuko.
Men også for min egen skyld foresatte jeg mig at jeg ikke atter vilde komme til eder med sorg.
2 Pakuti ngati ndikumvetsani chisoni, kodi angandisangalatse ndani, kupatula inuyo amene ndakumvetsani chisoni?
For hvis jeg gjør eder sorg, hvem er det da som gjør mig glad, uten den som jeg gjør sorg?
3 Nʼchifukwa chake ndinakulemberani monga ndinachitiramo kuti nditabwera kwanuko ndisadzamve chisoni ndi anthu oyenera kundisangalatsa. Ndinali ndi chikhulupiriro ndi inu nonse kuti inuyo mukakhala ndi chimwemwe poona kuti inenso ndili ndi chimwemwe.
Og just i det øiemed skrev jeg, forat jeg ikke, når jeg kom, skulde få sorg av dem som jeg burde ha glede av, idet jeg har den tillit til eder alle at min glede er eders alles glede.
4 Pakuti ndinakulemberani kalata ija ndili wopsinjika ndi wowawidwa mtima kwambiri ndi kutuluka misozi yambiri, osati pofuna kukumvetsani chisoni koma kuti ndikudziwitseni kuti ndimakukondani kwambiri.
For med megen trengsel og angst i hjertet skrev jeg til eder under mange tårer, ikke for å gjøre eder sorg, men forat I skulde kjenne den kjærlighet som jeg særlig har til eder.
5 Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera.
Men er det nogen som har voldt sorg, da er det ikke mig han har voldt sorg, men delvis - at jeg ikke skal være for hård - eder alle.
6 Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira.
Det er nok for ham med den straff han har fått av de fleste,
7 Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima.
så at I derimot heller skal tilgi og trøste ham, forat han ikke skal gå til grunne i ennu større sorg.
8 Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye.
Derfor ber jeg eder å la kjærlighet råde mot ham.
9 Cholinga china chimene ndinakulemberani kalata ija chinali chofuna kukuonani ngati mudzandimvera pa zonse.
For derfor var det også jeg skrev, for å få vite om I holder prøve, om I er lydige i alt.
10 Aliyense amene mumukhululukire, inenso ndimukhululukira. Ndipo ndikakhululukira, ngati pali kanthu koti ndikhululukire, ndiye kuti ndakhululuka chifukwa cha inu pamaso pa Khristu,
Men den som I tilgir noget, ham tilgir og jeg; for det jeg har tilgitt - om jeg har hatt noget å tilgi - det har jeg gjort for eders skyld, for Kristi åsyn, forat vi ikke skal dåres av Satan;
11 kupewa kuti Satana angapezere mpata pa ife, pajatu timadziwa machenjerero ake.
for ikke er vi uvitende om hans tanker.
12 Tsono nditafika ku Trowa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Khristu, nʼkupeza kuti Ambuye anditsekulira khomo,
Da jeg kom til Troas for Kristi evangeliums skyld, og en dør var mig oplatt i Herren, hadde jeg ingen ro i min ånd, fordi jeg ikke fant Titus, min bror,
13 ndinasowa mtendere mu mtima mwanga, chifukwa sindinapezeko mʼbale wanga Tito. Choncho ndinatsanzikana ndi anthu kumeneko nʼkupita ku Makedoniya.
men jeg sa farvel til dem og drog videre til Makedonia.
14 Koma tithokoze Mulungu amene amatitsogolera nthawi zonse monga ogwidwa ku nkhondo a Khristu pa chipambano chake. Tsono amatigwiritsa ntchito yofalitsa ponseponse nzeru zodziwira Khristu ngati fungo labwino.
Men Gud være takk, som alltid lar oss vinne seier i Kristus og ved oss åpenbarer sin kunnskaps duft på hvert sted!
15 Pakuti kwa Mulungu ndife fungo labwino la Khristu pakati pa iwo amene akupulumutsidwa ndi amene akuwonongeka.
For vi er en Kristi vellukt for Gud, blandt dem som blir frelst, og blandt dem som går fortapt,
16 Kwa amene akuwonongeka ndife fungo la imfa, limawapha. Ndipo kwa amene akupulumuka ndife fungo lamoyo, limawapatsa moyo. Ndani angayithe ntchito yotereyi?
for disse en duft av død til død, for hine en duft av liv til liv. Og hvem er vel duelig til dette?
17 Kusiyana ndi ena ambiri, ife sitilalikira Mawu a Mulungu kuti tipeza phindu. Mʼmalo mwake, ife mwa Khristu timayankhula pamaso pa Mulungu moona mtima, monga anthu otumidwa ndi Mulungu.
For vi er ikke, som de mange, slike at vi forfalsker Guds ord til egen vinning; men som i renhet, ja som av Gud, taler vi for Guds åsyn i Kristus.

< 2 Akorinto 2 >