< 2 Akorinto 2 >
1 Kotero ndinatsimikiza maganizo anga kuti ndisachitenso ulendo wina owawa wobwera kwanuko.
Azt tettem pedig fel magamban, hogy nem megyek hozzátok ismét szomorúsággal.
2 Pakuti ngati ndikumvetsani chisoni, kodi angandisangalatse ndani, kupatula inuyo amene ndakumvetsani chisoni?
Mert ha én megszomorítlak titeket, ugyan ki az, aki megvidámít engem, hacsak nem az, a kit én megszomorítok?
3 Nʼchifukwa chake ndinakulemberani monga ndinachitiramo kuti nditabwera kwanuko ndisadzamve chisoni ndi anthu oyenera kundisangalatsa. Ndinali ndi chikhulupiriro ndi inu nonse kuti inuyo mukakhala ndi chimwemwe poona kuti inenso ndili ndi chimwemwe.
És azért írtam nektek éppen azt, hogy amikor odamegyek, ne szomorodjak meg azok miatt, akiknek örülnöm kellene, mert meg vagyok győződve arról, hogy az én örömöm mindnyájatoké.
4 Pakuti ndinakulemberani kalata ija ndili wopsinjika ndi wowawidwa mtima kwambiri ndi kutuluka misozi yambiri, osati pofuna kukumvetsani chisoni koma kuti ndikudziwitseni kuti ndimakukondani kwambiri.
Mert sok szorongattatás és szívbeli háborgás között írtam nektek, sok könnyhullatással, de nem azért, hogy megszomorodjatok, hanem hogy megismerjétek azt a szeretetet, amelyet kiváltképpen irántatok érzek.
5 Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera.
Ha pedig valaki megszomorított, nem engem szomorított meg, hanem részben, hogy azt ne terheljem, titeket, mindnyájatokat.
6 Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira.
Elég ilyennek a többség részéről való megbüntetése.
7 Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima.
Most már inkább ti is bocsássatok meg neki és vigasztaljátok, hogy a felettébb való bánat meg ne eméssze.
8 Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye.
Azért kérlek titeket, tanúsítsatok iránta szeretetet.
9 Cholinga china chimene ndinakulemberani kalata ija chinali chofuna kukuonani ngati mudzandimvera pa zonse.
Mert azért is írtam, hogy bizonyosan megtudjam, hogy mindenben engedelmesek vagytok-e.
10 Aliyense amene mumukhululukire, inenso ndimukhululukira. Ndipo ndikakhululukira, ngati pali kanthu koti ndikhululukire, ndiye kuti ndakhululuka chifukwa cha inu pamaso pa Khristu,
Akinek pedig megbocsáttok valamit, annak én is megbocsátok. Mert ha volt mit megbocsátanom, én megbocsátottam. Tiértetek cselekedtem ezt a Krisztus színe előtt, hogy meg ne csaljon minket a sátán,
11 kupewa kuti Satana angapezere mpata pa ife, pajatu timadziwa machenjerero ake.
mert jól ismerjük az ő szándékait.
12 Tsono nditafika ku Trowa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Khristu, nʼkupeza kuti Ambuye anditsekulira khomo,
Amikor pedig Tróászba mentem a Krisztus evangéliuma ügyében, és kapu nyílt előttem az Úrban, nem volt a lelkemnek nyugalma, mivel nem találtam Tituszt, az én atyámfiát,
13 ndinasowa mtendere mu mtima mwanga, chifukwa sindinapezeko mʼbale wanga Tito. Choncho ndinatsanzikana ndi anthu kumeneko nʼkupita ku Makedoniya.
elbúcsúztam tehát tőlük és elmentem Macedóniába.
14 Koma tithokoze Mulungu amene amatitsogolera nthawi zonse monga ogwidwa ku nkhondo a Khristu pa chipambano chake. Tsono amatigwiritsa ntchito yofalitsa ponseponse nzeru zodziwira Khristu ngati fungo labwino.
De legyen hála az Istennek, aki mindenkor diadalra vezet minket a Krisztusban, és az ő ismeretének illatát terjeszti általunk.
15 Pakuti kwa Mulungu ndife fungo labwino la Khristu pakati pa iwo amene akupulumutsidwa ndi amene akuwonongeka.
Mert Krisztus jó illata vagyunk Isten számára, mind az üdvözülők, mind az elkárhozók között.
16 Kwa amene akuwonongeka ndife fungo la imfa, limawapha. Ndipo kwa amene akupulumuka ndife fungo lamoyo, limawapatsa moyo. Ndani angayithe ntchito yotereyi?
Ezeknek a halál illata halálra, azoknak pedig az élet illata életre. És ki alkalmas erre?
17 Kusiyana ndi ena ambiri, ife sitilalikira Mawu a Mulungu kuti tipeza phindu. Mʼmalo mwake, ife mwa Khristu timayankhula pamaso pa Mulungu moona mtima, monga anthu otumidwa ndi Mulungu.
Mert nem olyanok vagyunk, mint sokan, akik meghamisítják az Isten igéjét, hanem tisztán, sőt szinte Istenből szólunk Isten előtt a Krisztusban.