< 2 Akorinto 13 >

1 Uwu ndi ulendo wachitatu ndikubwera kudzakuyenderani. “Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.”
Voilà que pour la troisième fois je viens vers vous; sur le témoignage de deux ou trois témoins tout sera jugé.
2 Ndinakuchenjezani kale pamene ndinali nanu ulendo wachiwiri uja. Tsopano ndikubwereza ndisanafike. Ndikabweranso sindidzachitira chifundo amene anachimwa poyamba paja kapena wina aliyense amene anachimwa,
Je l’ai déjà dit, et je le dis encore, absent, comme si j’étais présent, que si je reviens, je n’aurai aucune indulgence pour ceux qui ont péché auparavant, ni pour tous les autres.
3 popeza mufuna chitsimikizo chakuti Khristu akuyankhula kudzera mwa ine. Iye siwofowoka pofuna kuchita nanu koma ndi wamphamvu pakati panu.
Est-ce que vous voulez éprouver celui qui parle en moi, le Christ, qui n’est pas affaibli, mais qui est puissant parmi vous?
4 Pofuna kutsimikizira, anapachikidwa ali wofowoka koma ali ndi moyo mwamphamvu ya Mulungu. Chomwechonso, ife ndife ofowoka mwa Iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi naye ndi mphamvu ya Mulungu, potumikira pakati panu.
Car, quoiqu’il ait été crucifié selon la faiblesse, il vit cependant par la puissance de Dieu. Nous aussi nous sommes faibles en lui; mais nous vivrons avec lui, par la vertu de Dieu parmi vous.
5 Tadzisanthulani nokha kuti muone ngati muli mʼchikhulupiriro; dziyeseni nokha. Kodi simuzindikira kuti Khristu Yesu ali mwa inu, ngati si choncho mwalephera mayesowa?
Examinez-vous vous-mêmes, si vous êtes dans la foi: éprouvez-vous vous-mêmes. Ne connaissez-vous pas vous-mêmes que le Christ est en vous? à moins que vous ne soyez dignes d’être rejetés.
6 Ndipo ndikhulupirira kuti mudzazindikira kuti ife sitinalephere mayesowo.
Mais j’espère que vous connaîtrez que pour nous, nous ne sommes pas dignes d’être rejetés.
7 Tsopano tikupemphera kwa Mulungu kuti musadzachite kanthu kena kalikonse kolakwa. Osati chifukwa choti anthu aone kuti ife tapambana mayesowo koma kuti mudzachite zokhoza ngakhale anthu atamationa ngati olephera.
Nous prions Dieu que vous ne fassiez rien de mal, non pas pour que nous paraissions nous-mêmes approuvés, mais que vous fassiez, vous, ce qui est bon, et que nous, nous passions pour dignes d’être rejetés.
8 Pakuti sitingachite chilichonse chotsutsana ndi choonadi, koma chokhacho chovomerezana ndi choonadi.
Car nous ne pouvons rien contre la vérité, mais pour la vérité.
9 Ife timasangalala kuti pamene tafowoka, inu muli amphamvu; ndipo pemphero lathu ndi lakuti mukhale angwiro.
Aussi nous nous réjouissons de ce que nous sommes faibles et de ce que vous, vous êtes forts. Et ce que nous demandons, c’est votre perfection.
10 Nʼchifukwa chake ndimalemba zinthu zoterezi pamene ndili kutali, kuti ndikabwera ndisadzagwiritse ntchito ulamuliro wanga mokalipa, uwu ndi ulamuliro umene Ambuye anandipatsa kuti ndikukuzeni inu osati kukuwonongani.
C’est pourquoi je vous écris ceci, absent, afin que présent, je n’agisse pas plus sévèrement, selon la puissance que le Seigneur m’a donnée pour l’édification et non pour la destruction.
11 Potsiriza abale, ndikuti tsalani bwino. Yesetsani kukhala angwiro, mvetsetsani pempho langa, khalani a mtima umodzi, khalani mwamtendere. Ndipo Mulungu wachikondi ndi mtendere adzakhala nanu.
Du reste, mes frères, réjouissez-vous, soyez parfaits, exhortez-vous les uns les autres, n’ayez qu’un sentiment, conservez la paix, et le Dieu de paix et de dilection sera avec vous.
12 Lonjeranani ndi mpsopsono wachiyero.
Saluez-vous les uns les autres par un saint baiser.
13 Anthu onse a Mulungu akupereka moni.
Tous les saints vous saluent.
14 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mulungu, ndi chiyanjano cha Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.
Que la grâce du Seigneur Jésus-Christ, et la charité de Dieu, et la communication du Saint-Esprit soient avec vous tous. Amen.

< 2 Akorinto 13 >