< 2 Akorinto 13 >

1 Uwu ndi ulendo wachitatu ndikubwera kudzakuyenderani. “Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.”
This intended visit of mine is my third visit to you. "On the evidence of two or three witnesses every charge shall be sustained."
2 Ndinakuchenjezani kale pamene ndinali nanu ulendo wachiwiri uja. Tsopano ndikubwereza ndisanafike. Ndikabweranso sindidzachitira chifundo amene anachimwa poyamba paja kapena wina aliyense amene anachimwa,
Those who cling to their old sins, and indeed all of you, I have forewarned and still forewarn (as I did on my second visit when present, so I do now, though absent) that, when I come again, I shall not spare you;
3 popeza mufuna chitsimikizo chakuti Khristu akuyankhula kudzera mwa ine. Iye siwofowoka pofuna kuchita nanu koma ndi wamphamvu pakati panu.
since you want a practical proof of the fact that Christ speaks by my lips--He who is not feeble towards you, but powerful among you.
4 Pofuna kutsimikizira, anapachikidwa ali wofowoka koma ali ndi moyo mwamphamvu ya Mulungu. Chomwechonso, ife ndife ofowoka mwa Iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi naye ndi mphamvu ya Mulungu, potumikira pakati panu.
For though it is true that He was crucified through weakness, yet He now lives through the power of God. We also are weak, sharing His weakness, but with Him we shall be full of life to deal with you through the power of God.
5 Tadzisanthulani nokha kuti muone ngati muli mʼchikhulupiriro; dziyeseni nokha. Kodi simuzindikira kuti Khristu Yesu ali mwa inu, ngati si choncho mwalephera mayesowa?
Test yourselves to discover whether you are true believers: put your own selves under examination. Or do you not know that Jesus Christ is within you, unless you are insincere?
6 Ndipo ndikhulupirira kuti mudzazindikira kuti ife sitinalephere mayesowo.
But I trust that you will recognize that we are not insincere.
7 Tsopano tikupemphera kwa Mulungu kuti musadzachite kanthu kena kalikonse kolakwa. Osati chifukwa choti anthu aone kuti ife tapambana mayesowo koma kuti mudzachite zokhoza ngakhale anthu atamationa ngati olephera.
And our prayer to God is that you may do nothing wrong; not in order that our sincerity may be demonstrated, but that you may do what is right, even though our sincerity may seem to be doubtful.
8 Pakuti sitingachite chilichonse chotsutsana ndi choonadi, koma chokhacho chovomerezana ndi choonadi.
For we have no power against the truth, but only for the furtherance of the truth;
9 Ife timasangalala kuti pamene tafowoka, inu muli amphamvu; ndipo pemphero lathu ndi lakuti mukhale angwiro.
and it is a joy to us when we are powerless, but you are strong. This we also pray for--the perfecting of your characters.
10 Nʼchifukwa chake ndimalemba zinthu zoterezi pamene ndili kutali, kuti ndikabwera ndisadzagwiritse ntchito ulamuliro wanga mokalipa, uwu ndi ulamuliro umene Ambuye anandipatsa kuti ndikukuzeni inu osati kukuwonongani.
For this reason I write thus while absent, that when present I may not have to act severely in the exercise of the authority which the Lord has given me for building up, and not for pulling down.
11 Potsiriza abale, ndikuti tsalani bwino. Yesetsani kukhala angwiro, mvetsetsani pempho langa, khalani a mtima umodzi, khalani mwamtendere. Ndipo Mulungu wachikondi ndi mtendere adzakhala nanu.
Finally, brethren, be joyful, secure perfection of character, take courage, be of one mind, live in peace. And then God who gives love and peace will be with you.
12 Lonjeranani ndi mpsopsono wachiyero.
Salute one another with a holy kiss.
13 Anthu onse a Mulungu akupereka moni.
All God's people here send greetings to you.
14 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mulungu, ndi chiyanjano cha Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.
May the grace of the Lord Jesus Christ, the love of God, and the fellowship of the Holy Spirit, be with you all.

< 2 Akorinto 13 >