< 2 Akorinto 11 >
1 Ndikukhulupirira kuti mupirira nako pangʼono kupusa kwanga. Chonde tandipirirani!
Vajha elszenvednétek tőlem egy kevés balgatagságot! Sőt szenvedjetek el engem is.
2 Nsanje imene ndimakuchitirani ndi yofanana ndi ya Mulungu. Ndinakulonjezani mwamuna mmodzi yekha, mwamunayo ndiye Khristu, kuti ndidzakuperekeni inuyo kwa Iyeyo monga namwali wangwiro.
Mert isteni buzgósággal buzgok értetek; hisz eljegyeztelek titeket egy férfiúnak, hogy mint szeplőtlen szűzet állítsalak a Krisztus elé.
3 Koma ndikuopa kuti monga Hava ananyengedwa ndi kuchenjera kwa njoka, mitima yanunso ingasocheretsedwe kuleka nʼkudzipereka moona mtima ndi modzipereka kwenikweni kwa Khristu.
Félek azonban, hogy a miként a kígyó a maga álnokságával megcsalta Évát, akként a ti gondolataitok is megrontatnak és eltávolodnak a Krisztus iránt való egyenességtől.
4 Pakuti ngati wina abwera kwa inu nalalikira Yesu wina wosiyana ndi Yesu amene tinamulalikira, kapena ngati mulandira mzimu wina wosiyana ndi Mzimu amene munalandira, kapena uthenga wabwino wina wosiyana ndi umene munawuvomereza, inuyo mumangolandira mosavuta.
Mert hogyha az, a ki jő, más Jézust prédikál, a kit nem prédikáltunk, vagy más lelket vesztek, a mit nem vettetek, vagy más evangyéliomot, a mit be nem fogadtatok, szépen eltűrnétek.
5 Komatu sindikuganiza kuti ndine wotsika kwambiri kwa “atumwi apamwamba.”
Mert én azt gondolom, hogy semmiben sem vagyok alábbvaló a fő-fő apostoloknál.
6 Mwina ndikhoza kukhala wosaphunzitsidwa kayankhulidwe, koma ndili ndi chidziwitso. Izi tinakufotokozerani momveka bwinobwino.
Ha pedig avatatlan vagyok is a beszédben, de nem az ismeretben; sőt mindenben, mindenképen nyilvánvalókká lettünk előttetek.
7 Kodi linali tchimo kwa ine kudzichepetsa nʼcholinga chakuti ndikukwezeni pamene ndinkalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu kwa inu mwaulere?
Avagy vétkeztem-é, mikor magamat megaláztam, hogy ti felmagasztaltassatok, hogy ingyen hírdettem néktek az Isten evangyéliomát?
8 Ndinkalanda mipingo ina pomalandira thandizo kwa iwo kuti ndikutumikireni.
Más gyülekezeteket fosztottam meg, zsoldot vévén, hogy néktek szolgáljak; és mikor nálatok voltam és szűkölködtem, nem voltam terhére senkinek.
9 Ndipo pamene ndinali pakati panu, nditasowa kanthu, sindinalemetse munthu aliyense, pakuti abale ena amene anachokera ku Makedoniya anandipatsa zonse zimene ndinkazisowa. Ndayesetsa kuti ndisakhale cholemetsa kwa inu mʼnjira ina iliyonse, ndipo ndidzapitiriza kutero.
Mert az én szükségemet kipótolták a Macedóniából jött atyafiak; és rajta voltam és rajta is leszek, hogy semmiben se legyek terhetekre.
10 Kunena moona mtima molingana ndi chilungamo cha Khristu chimene chili mwa ine, palibe amene angandiletse kudzitamandira mʼzigawo za ku Akaya.
Krisztus igazsága bennem, hogy én ettől a dicsekvéstől nem esem el Akhája vidékén.
11 Nʼchifukwa chiyani ndikutero? Kodi nʼchifukwa choti sindikukondani? Mulungu akudziwa kuti ndimakukondani!
Miért? Hogy nem szeretlek titeket? Tudja az Isten.
12 Ndipo ndipitiriza kuchita zomwe ndikuchitazi nʼcholinga chakuti ndisapereke mpata kwa amene akufuna kupezera mwayi woti afanane nafe pa zinthu zimene iwowo amadzitamandira.
De a mit cselekszem, cselekedni is fogom, hogy elvágjam az alkalmat az alkalomkeresők elől; hogy a mivel dicsekesznek, olyanoknak találtassanak abban, mint mi is.
13 Pakuti anthu oterewa ndi atumwi onama, antchito achinyengo, odzizimbayitsa ngati atumwi a Khristu.
Mert az ilyenek hamis apostolok, álnok munkások, a kik a Krisztus apostolaivá változtatják át magukat.
14 Sizododometsa zimenezi, pakuti Satana mwini amadzizimbayitsa kuoneka ngati mngelo wowunikira anthu.
Nem is csoda; hisz maga a Sátán is átváltoztatja magát világosság angyalává.
15 Nʼzosadabwitsa tsono ngati atumiki ake akudzizimbayitsa ngati otumikira chilungamo. Matsiriziro awo adzalandira zoyenerana ndi ntchito zawo.
Nem nagy dolog azért, ha az ő szolgái is átváltoztatják magokat az igazság szolgáivá; a kiknek végök az ő cselekedeteik szerint lészen.
16 Ndibwereze kunena kuti, wina aliyense asandiyese chitsiru. Koma ngati mutero, mundilandire monga mmene mukhoza kulandirira chitsiru, kuti ndinyadirepo pangʼono.
Ismét mondom: ne tartson engem senki esztelennek; de ha mégis, fogadjatok be mint esztelent is, hogy egy kicsit én is dicsekedhessem.
17 Kudzinyadira kwangaku, sindikuyankhula monga mmene Ambuye akufunira koma ngati chitsiru.
A mit mondok, nem az Úr szerint mondom, hanem mintegy esztelenül a dicsekvésnek ezzel a merészségével,
18 Popeza ambiri akudzitama monga dziko lapansi limachitira, inenso ndidzitamanso.
Mivelhogy sokan dicsekesznek test szerint, dicsekeszem én is.
19 Inu mumalolera kukhala ndi zitsiru mokondwera chifukwa mumati ndinu anzeru!
Hisz okosak lévén, örömest eltűritek az eszteleneket.
20 Kunena zoona mumangololera aliyense; amene amakusandutsani akapolo, kapena amene amakudyerani masuku pamutu, kapena amene amakupezererani, kapena amene amadzitukumula, kapena amene amakumenyani khofi.
Mert eltűritek, ha valaki leigáz titeket, ha valaki felfal, ha valaki megfog, ha valaki felfuvalkodik, ha valaki arczul ver titeket.
21 Ndikuvomera mwamanyazi kuti ife sitinali olimba mtima kuti nʼkuchita zinthu zimenezi. Ndikuyankhula ngati chitsiru kuti chimene wina aliyense akhoza kudzitama nacho, Inenso ndikhoza kudzitama nachonso.
Szégyenkezve mondom, mivelhogy mi erőtelenek voltunk; de a miben merész valaki, esztelenül szólok, merész vagyok én is.
22 Kodi iwo ndi Ahebri? Inenso ndine Mhebri. Kodi iwo ndi Aisraeli? Inenso ndine Mwisraeli. Kodi iwo ndi zidzukulu za Abrahamu? Inenso ndine mdzukulu wa Abrahamu.
Héberek ők? Én is. Izráeliták-é? Én is. Ábrahám magva-é? Én is.
23 Kodi iwo ndi atumiki a Khristu? Ndikuyankhula ngati wamisala. Ine ndine woposa iwowo. Ndagwira ntchito kwambiri kupambana iwo, ndakhala ndikuyikidwa mʼndende kawirikawiri, ndakwapulidwapo kwambiri, kawirikawiri ndinali pafupi kufa.
Krisztus szolgái-é? (balgatagul szólok) én méginkább; több fáradság, több vereség, több börtön, gyakorta való halálos veszedelem által.
24 Andikwapulapo kasanu zikoti zija za Ayuda, makumi anayi kuchotsapo chimodzi.
A zsidóktól ötször kaptam negyvenet egy híján.
25 Katatu anandimenya ndi ndodo. Kamodzi anandigendapo miyala. Katatu sitima yathu ya panyanja inasweka, ndipo ndinakhala usiku ndi usana ndi kuyandama pa nyanja.
Háromszor megostoroztak, egyszer megköveztek, háromszor hajótörést szenvedtem, éjt-napot a mélységben töltöttem;
26 Ndakhala ndikuyenda maulendo ataliatali. Moyo wanga wakhala ukukumana ndi zoopsa pa mitsinje, zoopsa za achifwamba, zoopsa zochokera kwa abale anga Ayuda, zoopsa zochokera kwa anthu akunja. Ndinakumana ndi zoopsa mʼmizinda, mʼmidzi, pa nyanja, ndi pakati pa abale onyenga.
Gyakorta való utazásban, veszedelemben folyó vizeken, veszedelemben rablók közt, veszedelemben népem között, veszedelemben pogányok között, veszedelemben városban, veszedelemben pusztában, veszedelemben tengeren, veszedelemben hamis atyafiak közt;
27 Ndakhala ndikugwira ntchito molimbika ndipo kawirikawiri ndakhala ndikuchezera usiku wonse osagona. Ndakhala ndikumva njala ndi ludzu ndipo kawirikawiri ndakhala wopanda chakudya. Ndakhala ndi kuzizidwa ndi wosowa zovala.
Fáradságban és nyomorúságban, gyakorta való virrasztásban, éhségben és szomjúságban, gyakorta való bőjtölésben, hidegben és mezítelenségben.
28 Kuwonjezera pa zonsezi, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa chipsinjo cha nkhawa ya mipingo yonse.
Mindezeken kívül van az én naponkénti zaklattatásom, az összes gyülekezetek gondja.
29 Ndani ali wofowoka, ine wosakhala naye mʼkufowoka kwakeko? Ndani amene mnzake amuchimwitsa, ine wosavutika mu mtima?
Ki beteg, hogy én is beteg ne volnék? Ki botránkozik meg, hogy én is ne égnék?
30 Ngati nʼkoyenera kudzitamandira, ndidzadzitamandira pa zinthu zimene zimaonetsa kufowoka kwanga.
Ha dicsekednem kell, az én gyengeségemmel dicsekszem.
31 Mulungu, Atate a Ambuye Yesu, amene tiyenera kumutamanda nthawi zonse, akudziwa kuti sindikunama. (aiōn )
Az Isten és a mi Urunk Jézus Krisztusnak Atyja, a ki mindörökké áldott, tudja, hogy nem hazudom. (aiōn )
32 Ku Damasiko, bwanamkubwa woyimira Mfumu Areta, anayika alonda kuzungulira mzinda wonse kuti andigwire.
Damaskusban Aretás király helytartója őrzette a damaskusiak városát, akarván engem megfogni;
33 Koma abale anandiyika mʼdengu nanditsitsira pa chipupa kudzera pa zenera la mpandawo, motero ndinapulumuka mʼmanja mwake.
És az ablakon át, kosárban bocsátottak le a kőfalon, és megmenekültem kezei közül.