< 2 Akorinto 10 >

1 Mwa kufatsa ndi kuleza mtima kwa Khristu, ndikukupemphani, ine Paulo amene anthu ena amati ndimachita manyazi tikaonana maso ndi maso ndi inu, koma wosaopa pamene ndili kutali nanu!
Unene ne Paulo, unene kumupepeelya kuupolo nuang'wa Kilisto. Unene nemupolo itungo nenhole ntongeela anyu, kuite nkete ugimya kitalanyu itungo nenkole kuli nunye.
2 Ndikukupemphani kuti ndikadzafika kumeneko ndisadzachite kuyankhula mwamphamvu monga mmene ndimayembekezera kudzachita kwa anthu ena amene amaganiza kuti machitidwe athu ndi ofanana ndi anthu a dziko lapansi.
Kumulompa unye kena, itungu nenkole palung'wi nunye, shangakutula nuugimya itungo nekuagilya awa neasegile kena kikie kemuile.
3 Ngakhale ife timakhala mʼdziko lapansi, sitimenya nkhondo monga mmene dziko lapansi limachitira.
Kunsoko ataeze anga kuugenda kimuili, shanga kikua embita kimuili.
4 Pakuti zida zathu zankhondo si zida za dziko lapansi. Koma ndi mphamvu zochokera kwa Mulungu zotha kugwetsa malinga.
Kunsoko iyege nekutumela kikuila singa yamuili, kuleka ite ikete ngulu ung'wi Tunda kubipya ukulu. Yukuheja lukulu udui nuakubepya.
5 Timagonjetsa maganizo onse onyenga ndiponso kudzikuza kulikonse kolimbana ndi anthu kuti asadziwe Mulungu. Ndipo timagonjetsa ganizo lililonse kuti limvere Khristu.
Inge kuubepya kehi nekikete uuhumi nekikulya ntongeela ang'wi Tunda. Kuuletenda mateka kukela uhumi nukumugomba Ukilisto.
6 Ndipo ife tidzakhala okonzeka kulanga aliyense wosamvera ngati inuyo mutakhala omvera kwenikweni.
Hange kuulija ugombinuakulamula kela intendo nimbe, nkua udu ugombi wanyu nuukutula wakonda.
7 Inu mukuweruza potengera zimene maso anu akuona. Ngati wina akutsimikiza kuti ndi wake wa Khristu, iye aganizenso kuti ifenso ndife a Khristu monga iye.
Goza eki nekikole ng'walye ntongeela anyu ang'wi wili ukupepeleka kena nuanso wang'wa Kilisto, nuikembushe nuanso ung'wenso kena anga uu udu nuile wang'wa Kilisto, ite uu nusese kile gwa.
8 Tsono ngakhale nditadzitama momasuka za ulamuliro umene Ambuye anatipatsa woti tikukuzeni osati kukuwonongani, ndithu sindidzachita manyazi.
Kunsoko atanitogole inino udu kukeela uhumi witu, nu Mukulu aupumilye kunsoko ilu kumuzenga unyenye singa kumubipya, singa kuona imenyala.
9 Ine sindikufuna kuoneka ngati ndikukuopsezani ndi makalata anga.
Singa ndoilwe ele ligele kena kumutumbaunye kumabada ane.
10 Pakuti ena amati, “Makalata ake ndi awukali ndi amphamvu koma maonekedwe a thupi lake ndi wosagwira mtima ndipo mayankhulidwe ake ndi achabechabe.”
Kuite antu ang'wi elunga, “Ibada yakwe itaki hange ikete ngulu, kuite nuanso munegetu ekumuili Inkani yakwe singa inonee kutegeligwa.”
11 Anthu oterewa ayenera kuzindikira kuti zomwe timalemba mʼmakalata tili kutali ndi zomwe tidzakhale tili komweko.
Embu iantu anga awa nealengile kena lehi nekutambula kibada itungo nekukole kuli, inge anga uu ite nekika tende itungo nekukole pang'wanso.
12 Sitikudziyika kapena kudzifananiza tokha ndi anthu ena amene amadziyenereza okha. Pamene akudzifanizira okha podziyerekeza ndi anzawo a mʼgulu lawo lomwe, ndi opanda nzeru.
Shakinzu nkuli du anga kilingeile usese ang'wi kigemela usese nawa neikulya ienso. Kuite neigemeelya ienso kukela ung'wi wao, agila anga mahala.
13 Komabe, ifeyo sitidzitama modutsa malire ake enieni, koma kudzitama kwathu kudzalekeza mʼmalire amene Mulungu anatiyikira, malire ake ndi mpaka kwa inu.
Usese, ata uu, singa kuitogola kukeela membi. Kuteka ite, kutenda uu udu mumembi izi ni Tunda ukupimie usese, membi niigeile kuli anga nianyu niele.
14 Pakuti sitikudzitama modutsa malire ngati kuti sitinafike kwa inu, popeza tinali oyamba kufika kwa inu ndi Uthenga Wabwino wa Khristu.
Kunsoko usese shanga aekiongeeye naekumizee unyenye. Ae kiang'wendyo kupika kuukuli anga nuanyu kunsoko ang'wa Kilisto.
15 Choncho sitinyadiranso ntchito imene ena anayigwira. Chiyembekezo chathu nʼchakuti, pamene chikhulupiriro chanu chikukulirakulira, dera lathu la ntchito pakati panu lidzakulanso kwambiri,
Shanga kiloiye kukeela membi kumilemo aangiza. Kuleke ite, kuhuie uhueli wanyu uukuli wakwe kena ikianza kitu nehamelemu kekugalempigwa lukulu hange keli mumimbi lukulu.
16 kuti tikalalikire Uthenga Wabwino mu zigawo zina kupitirira kwanuko. Pakuti sitikufuna kudzitama pa ntchito yogwira ena kale mʼdera la munthu wina.
Kuhuie kuile, nsoko kena kuhume kutanantya ulukani ata mumekoa kukila nanyu. Shanga kuutogola kukeila milimo nekitung'wa muianza nungeza.
17 Koma, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
“Kuite wehi nuitogole, nuitogola Mumukulu.”
18 Pakuti munthu amene amavomerezedwa, si amene amadziyenereza yekha, koma munthu amene Ambuye amuyenereza.
Kundogoilyo singa uwo nuigeela ung'wenso ukigela. Inge uyu nu Mukulu wimigelya.

< 2 Akorinto 10 >