< 2 Akorinto 10 >
1 Mwa kufatsa ndi kuleza mtima kwa Khristu, ndikukupemphani, ine Paulo amene anthu ena amati ndimachita manyazi tikaonana maso ndi maso ndi inu, koma wosaopa pamene ndili kutali nanu!
Ini aku Paulus, secara pribadi memohon kepadamu melalui kebaikan dan kelembutan Kristus, orang yang “pemalu” ketika aku harus menghadapimu tetapi yang “berani” ketika aku tidak ada.
2 Ndikukupemphani kuti ndikadzafika kumeneko ndisadzachite kuyankhula mwamphamvu monga mmene ndimayembekezera kudzachita kwa anthu ena amene amaganiza kuti machitidwe athu ndi ofanana ndi anthu a dziko lapansi.
Aku memohon padamu, agar lain kali aku bersamamu, aku tidak harus sekuat yang kupikirkan, dengan berani berurusan dengan mereka yang berpikir kita berperilaku duniawi.
3 Ngakhale ife timakhala mʼdziko lapansi, sitimenya nkhondo monga mmene dziko lapansi limachitira.
Meskipun kita hidup di dunia ini, kita tidak bertarung seperti dunia.
4 Pakuti zida zathu zankhondo si zida za dziko lapansi. Koma ndi mphamvu zochokera kwa Mulungu zotha kugwetsa malinga.
Senjata kita bukan dari dunia ini, tetapi kekuatan besar Allah yang menghancurkan benteng pemikiran manusia, menghancurkan teori-teori yang menyesatkan.
5 Timagonjetsa maganizo onse onyenga ndiponso kudzikuza kulikonse kolimbana ndi anthu kuti asadziwe Mulungu. Ndipo timagonjetsa ganizo lililonse kuti limvere Khristu.
Setiap tembok tinggi yang berdiri tegak dan bangga dengan pengetahuan tentang Allah dirobohkan. Setiap ide pemberontak ditangkap dan dibawa ke dalam persetujuan yang taat dengan Kristus.
6 Ndipo ife tidzakhala okonzeka kulanga aliyense wosamvera ngati inuyo mutakhala omvera kwenikweni.
Ketika kalian sepenuhnya menaati Kristus, maka kami siap menghukum setiap ketidaktaatan.
7 Inu mukuweruza potengera zimene maso anu akuona. Ngati wina akutsimikiza kuti ndi wake wa Khristu, iye aganizenso kuti ifenso ndife a Khristu monga iye.
Lihat apa yang menatap wajahmu! Siapapun yang menganggap bahwa mereka adalah milik Kristus harus berpikir lagi — sama seperti mereka adalah milik Kristus, kita juga!
8 Tsono ngakhale nditadzitama momasuka za ulamuliro umene Ambuye anatipatsa woti tikukuzeni osati kukuwonongani, ndithu sindidzachita manyazi.
Meskipun saya mungkin tampak terlalu menyombongkan otoritas kami, saya tidak malu karenanya. Tuhan memberikan wewenang ini kepada kami untuk membangun kalian, bukan untuk menjatuhkan kalian.
9 Ine sindikufuna kuoneka ngati ndikukuopsezani ndi makalata anga.
Aku tidak bermaksud menakut-nakutimu dengan surat-suratku.
10 Pakuti ena amati, “Makalata ake ndi awukali ndi amphamvu koma maonekedwe a thupi lake ndi wosagwira mtima ndipo mayankhulidwe ake ndi achabechabe.”
Orang-orang berkata, “Surat-suratnya keras dan berat, tetapi secara pribadi dia lemah, dan dia pembicara yang tidak berguna.”
11 Anthu oterewa ayenera kuzindikira kuti zomwe timalemba mʼmakalata tili kutali ndi zomwe tidzakhale tili komweko.
Orang-orang seperti itu harus menyadari bahwa apa yang kita katakan melalui surat ketika kita tidak di sana, akan kita lakukan ketika kita ada di sana!
12 Sitikudziyika kapena kudzifananiza tokha ndi anthu ena amene amadziyenereza okha. Pamene akudzifanizira okha podziyerekeza ndi anzawo a mʼgulu lawo lomwe, ndi opanda nzeru.
Kita tidak terlalu sombong untuk membandingkan diri kita dengan mereka yang terlalu memikirkan diri sendiri. Mereka yang mengukur diri mereka sendiri, dan membandingkan diri mereka sendiri dengan diri mereka sendiri, benar-benar bodoh!
13 Komabe, ifeyo sitidzitama modutsa malire ake enieni, koma kudzitama kwathu kudzalekeza mʼmalire amene Mulungu anatiyikira, malire ake ndi mpaka kwa inu.
Tapi kami tidak akan menyombongkan diri dengan cara yang berlebihan yang tidak bisa diukur. Kami hanya mengukur apa yang telah kami lakukan dengan menggunakan sistem pengukuran Allah yang Dia berikan kepada kami — dan itu termasuk kalian.
14 Pakuti sitikudzitama modutsa malire ngati kuti sitinafike kwa inu, popeza tinali oyamba kufika kwa inu ndi Uthenga Wabwino wa Khristu.
Kami tidak terlalu memaksakan wewenang kami untuk mengatakan ini, seolah-olah kami tidak mencapai kalian, karena kami telah sampai kepada kalian dan membagikan kabar baik tentang Kristus kepada kalian.
15 Choncho sitinyadiranso ntchito imene ena anayigwira. Chiyembekezo chathu nʼchakuti, pamene chikhulupiriro chanu chikukulirakulira, dera lathu la ntchito pakati panu lidzakulanso kwambiri,
Kami tidak membual dalam istilah-istilah boros yang tidak dapat diukur, mengklaim penghargaan atas apa yang telah dilakukan orang lain. Sebaliknya, kami berharap bahwa ketika kepercayaan kalian kepada Allah tumbuh, pekerjaan kami di antara kalian akan meningkat pesat.
16 kuti tikalalikire Uthenga Wabwino mu zigawo zina kupitirira kwanuko. Pakuti sitikufuna kudzitama pa ntchito yogwira ena kale mʼdera la munthu wina.
Kemudian kami dapat membagikan kabar baik di tempat-tempat yang jauh di luar kalian, tanpa membual tentang apa yang telah dilakukan di tempat orang lain telah bekerja.
17 Koma, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
“Jika ada orang yang ingin bermegah, bermegahlah tentang Tuhan.”
18 Pakuti munthu amene amavomerezedwa, si amene amadziyenereza yekha, koma munthu amene Ambuye amuyenereza.
Bukan mereka yang memuji diri sendiri yang dihormati, tetapi mereka yang dipuji Tuhan.