< 2 Mbiri 1 >

1 Solomoni mwana wa Davide anakhazikika molimbika mu ufumu wake, pakuti Yehova Mulungu wake anali naye ndipo anamukweza kwambiri.
Og Salomo, Davids Søn, vandt Magt i sit Rige; og Herren, hans Gud, var med ham og gjorde ham overmaade stor.
2 Tsono Solomoni anayankhula kwa Aisraeli onse, olamulira a anthu 1,000, olamulira a anthu 100, oweruza ndiponso kwa atsogoleri onse a Israeli ndi atsogoleri amabanja.
Og Salomo gav Befaling til al Israel, til Øversterne over tusinde og hundrede og til Dommerne og til alle Øversterne for al Israel, Øversterne for Fædrenehusene,
3 Solomoni pamodzi ndi gulu lonse la anthu anapita ku malo ofunika kwambiri pachipembedzo ku Gibiyoni. Tenti ya msonkhano ya Mulungu inali kumeneko, imene Mose mtumiki wa Yehova anayipanga mʼchipululu muja.
og de gik hen, Salomo og hele Forsamlingen med ham, til Højen, som var i Gibeon; thi der var Guds Forsamlings Paulun, hvilket Mose, Herrens Tjener, havde gjort i Ørken.
4 Davide anabweretsa Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriyati Yearimu, ndi kulikhazika kumalo kumene analikonzera popeza analimangira tenti mu Yerusalemu.
Men David havde ført Guds Ark op fra Kirjath-Jearim til Stedet, som David havde beredt til den; thi han havde opslaaet et Paulun til den i Jerusalem.
5 Koma guwa lansembe lamkuwa limene Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri analipanga linali ku Gibiyoni kutsogolo kwa tenti ya Yehova. Kotero kuti Solomoni ndi gulu lonse anakapembedza kumeneko.
Og det Kobberalter, som Bezaleel, en Søn af Uri, Hurs Søn, havde forfærdiget, var sat foran Herrens Tabernakel; og Salomo og Forsamlingen søgte hen til det.
6 Solomoni anapita pamene panali guwa lansembe lamkuwa pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano ndipo anapereka nsembe zopsereza 1,000.
Og Salomo ofrede for Herrens Ansigt paa Kobberalteret, som var for Forsamlingens Paulun, og han ofrede paa det tusinde Brændofre.
7 Usiku umenewo Mulungu anaonekera kwa Solomoni ndipo anati kwa iye, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
I samme Nat aabenbarede Gud sig for Salomo og sagde til ham: Begær, hvad jeg skal give dig.
8 Solomoni anayankha Mulungu kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwakukulu kwa Davide abambo anga ndipo mwayika ine kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Og Salomo sagde til Gud: Du har gjort stor Miskundhed imod David, min Fader, og gjort mig til Konge i hans Sted.
9 Tsopano Inu Yehova Mulungu, lolani kuti lonjezo lanu kwa abambo anga Davide likwaniritsidwe, pakuti mwandiyika kukhala mfumu ya anthu anu amene ndi ochuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi.
Lad nu, Herre, Gud! dit Ord til min Fader David blive Sandhed; thi du har gjort mig til Konge over et Folk, som er talrigt som Støv paa Jorden.
10 Mundipatse nzeru ndi luntha zolamulira anthu awa, pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
Giv mig nu Visdom og Kundskab, at jeg kan gaa ud og gaa ind for dette Folk; thi hvo kan ellers dømme dette dit store Folk?
11 Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza izi ndi zokhumba za mtima wako ndipo sunapemphe katundu, chuma kapena ulemu, kapena imfa ya adani ako, ndiponso poti sunapemphe moyo wautali koma nzeru ndi luntha kuti ulamulire anthu anga amene Ine ndakuyika kukhala mfumu yawo,
Da sagde Gud til Salomo: Efterdi dette var i dit Hjerte, at du ikke har begæret Rigdom, Gods og Ære, eller deres Liv, som hade dig, og end ikke har begæret et langt Liv, men begæret dig Visdom og Kundskab, at du kan dømme mit Folk, over hvilket jeg har gjort dig til Konge:
12 Ine ndidzakupatsa nzeru ndi chidziwitso. Ndipo ndidzakupatsanso katundu, chuma ndi ulemu, zinthu zoti palibe mfumu imene inali nazo iwe usanakhalepo ndipo palibe wina amene adzakhale nazo iweyo ukadzafa.”
Saa være Visdom og Kundskab givet dig; tilmed vil jeg give dig Rigdom og Gods og Ære, saadant som de Konger, der have været før dig, ikke have haft, og som ingen efter dig skal have.
13 Kotero Solomoni anabwerera ku Yerusalemu kuchoka kumalo opembedzerako a ku Gibiyoni, ku tenti ya msonkhano ndipo analamulira Israeli.
Og Salomo kom til Jerusalem fra Højen, som var i Gibeon, fra Forsamlingens Paulun, og regerede over Israel.
14 Solomoni anasonkhanitsa magaleta ndi akavalo; anali ndi magaleta 1,400 ndi akavalo 12,000, amene anawayika mʼmizinda yosungira magaleta ndipo ena anali ndi iye mu Yerusalemu.
Og Salomo samlede Vogne og Ryttere, og han havde tusinde og fire Hundrede Vogne og tolv Tusinde Ryttere; og han lod dem blive i Vognstæderne og hos Kongen i Jerusalem.
15 Mfumu inasandutsa siliva ndi golide kukhala ngati miyala wamba mu Yerusalemu. Inasandutsanso mkungudza kukhala wochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa.
Og Kongen gjorde Sølvet og Guldet i Jerusalem som Stenene, og Cedertræerne gjorde han som Morbærtræerne, der ere i Lavlandet i Mangfoldighed.
16 Solomoni amagula akavalo ku Igupto ndi Kuwe pakuti anthu amalonda a mfumu amakawagula ku Kuwe.
Og Udførselen af Heste skete for Salomo fra Ægypten; og en Skare af Kongens Købmænd hentede en Skare for rede Penge.
17 Anthu ankagula galeta ku Igupto pa mtengo wa masekeli asiliva 600 ndipo kavalo pa mtengo wa ndalama zasiliva 150. Iwo ankazigulitsanso kwa mafumu onse a Ahiti ndi a Aramu.
Og de droge op og udførte fra Ægypten en Vogn for seks Hundrede Sekel Sølv, og en Hest for hundrede og halvtredsindstyve; og saaledes førte de dem ud til alle Hethithernes Konger og til Kongerne i Syrien ved egen Haand.

< 2 Mbiri 1 >