< 2 Mbiri 7 >

1 Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo.
Kwathi uSolomoni eseqedile ukukhuleka, umlilo wehla uvela emazulwini, wadla umnikelo wokutshiswa lemihlatshelo, lenkazimulo yeNkosi yagcwalisa indlu.
2 Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova.
Njalo abapristi babengelakho ukungena endlini yeNkosi, ngoba inkazimulo yeNkosi yayigcwalise indlu yeNkosi.
3 Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti, “Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala chikhalire”
Lapho bonke abantwana bakoIsrayeli bebona ukwehla komlilo lenkazimulo yeNkosi phezu kwendlu, bakhothama ngobuso babo emhlabathini endaweni egandelweyo, bakhonza bedumisa iNkosi, ukuthi ilungile, ukuthi umusa wayo umi phakade.
4 Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
Inkosi labo bonke abantu banikela-ke imihlatshelo phambi kweNkosi.
5 Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu.
Inkosi uSolomoni yasinikela imihlatshelo yezinkabi ezizinkulungwane ezingamatshumi amabili, lezimvu ezizinkulungwane ezilikhulu lamatshumi amabili. Ngokunjalo inkosi labo bonke abantu bayehlukanisa indlu kaNkulunkulu.
6 Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.
Abapristi basebesima ezikhundleni zabo; lamaLevi elezinto zokuhlabelela zikaJehova inkosi uDavida ayezenzele ukudumisa uJehova, ngoba umusa wakhe umi phakade, lapho uDavida edumisa ngenkonzo yabo; labapristi bakhalisa impondo phambi kwabo, loIsrayeli wonke wema.
7 Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.
USolomoni wasengcwelisa iphakathi leguma elaliphambi kwendlu yeNkosi, ngoba wenza lapho iminikelo yokutshiswa lamahwahwa eminikelo yokuthula, ngoba ilathi lethusi uSolomoni ayelenzile lalingenele umnikelo wokutshiswa, lomnikelo wokudla, lamahwahwa.
8 Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto.
Langalesosikhathi uSolomoni wenza umkhosi okwensuku eziyisikhombisa, loIsrayeli wonke kanye laye, ibandla elikhulu kakhulu, kusukela ekungeneni kweHamathi kusiya esifuleni seGibhithe.
9 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero.
Langosuku lwesificaminwembili benza umhlangano onzulu, ngoba benza ukwehlukaniswa kwelathi okwensuku eziyisikhombisa, lomkhosi okwensuku eziyisikhombisa.
10 Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.
Ngosuku lwamatshumi amabili lantathu lwenyanga yesikhombisa waseyekela abantu bahamba baya emathenteni abo, bethokoza bejabula enhliziyweni ngokuhle iNkosi eyayikwenzele uDavida loSolomoni loIsrayeli abantu bayo.
11 Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu,
Ngokunjalo uSolomoni waqeda indlu kaJehova lendlu yenkosi; lakho konke okwakuvela enhliziyweni kaSolomoni ukukwenza endlini yeNkosi lendlini yakhe wakuphumelelisa.
12 Yehova anamuonekera usiku ndipo anati: “Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.
INkosi yasibonakala kuSolomoni ebusuku yathi kuye: Ngizwile umkhuleko wakho, sengizikhethele lindawo ukuba yindlu yomhlatshelo.
13 “Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu,
Uba ngivala amazulu ukuze kungabi lazulu, kumbe uba ngilaya intethe ukuqeda ilizwe, kumbe uba ngithumela umatshayabhuqe wesifo phakathi kwabantu bami,
14 ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo.
uba abantu bami ibizo lami elibizwa phezu kwabo bezithoba, bakhuleke badinge ubuso bami, baphenduke ezindleleni zabo ezimbi, mina-ke ngizakuzwa ngisemazulwini, ngithethelele isono sabo, ngelaphe ilizwe labo.
15 Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano.
Khathesi amehlo ami azavuleka, lendlebe zami zilalele umkhuleko walindawo.
16 Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.
Ngoba sengiyikhethile ngayingcwelisa lindlu ukuze ibizo lami libe khona kuze kube nininini; lamehlo ami lenhliziyo yami kuzakuba lapho zonke izinsuku.
17 “Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
Wena-ke, uba uhamba phambi kwami njengokuhamba kukaDavida uyihlo, wenze njengakho konke engikulaye khona, ugcine izimiso zami lezahlulelo zami,
18 Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’
ngizaqinisa-ke isihlalo sobukhosi sombuso wakho, njengokwenza kwami isivumelwano loDavida uyihlo ngisithi: Kakuyikusweleka muntu kuwe obusa koIsrayeli.
19 “Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
Kodwa uba libuyela emuva lina, litshiya izimiso zami lemilayo yami engikubeke phambi kwenu, lihambe likhonze abanye onkulunkulu libakhothamele,
20 pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
ngizabasiphuna-ke elizweni engibanike lona, lalindlu engiyingcwelisele ibizo lami ngizayilahla isuke phambi kwami, ngiyenze ibe yisiga lento yokuhozwa phakathi kwezizwe zonke.
21 Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
Lalindlu ephakemeyo izakuba yisimangaliso kulowo lalowo odlula kuyo, aze athi: INkosi ikwenzeleni okunje kulelilizwe lakulindlu?
22 Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
Bazakuthi-ke: Kungoba beyidelile iNkosi uNkulunkulu waboyise eyabakhupha elizweni leGibhithe, babambelela kwabanye onkulunkulu, babakhonza babasebenzela; ngenxa yalokho ibehlisele bonke lobububi.

< 2 Mbiri 7 >