< 2 Mbiri 7 >

1 Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo.
Og der Salomo havde fuldendt at bede, da faldt Ild ned fra Himmelen og fortærede Brændofferet og Slagtofrene, og Herrens Herlighed fyldte Huset.
2 Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova.
Og Præsterne kunde ikke gaa ind i Herrens Hus; thi Herrens Herlighed fyldte Herrens Hus.
3 Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti, “Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala chikhalire”
Der alle Israels Børn saa Ilden og Herrens Herlighed nedfalde over Huset, da bøjede de sig ned med Ansigtet til Jorden imod Gulvet og tilbade og takkede Herren, at han er god, at hans Miskundhed er evindelig.
4 Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
Og Kongen og alt Folket ofrede Slagtoffer for Herrens Ansigt.
5 Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu.
Og Kong Salomo ofrede som Slagtoffer to og tyve Tusinde Okser og hundrede og tyve Tusinde Faar; og Kongen og alt Folket indviede Guds Hus.
6 Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.
Men Præsterne stode i deres Tjeneste og Leviterne med Herrens Sanginstrumenter, som Kong David havde ladet gøre til at takke Herren med, at hans Miskundhed er evindelig, der David ved dem lovede Gud; og Præsterne blæste i Basunerne tværs over for dem, og det hele Israel stod.
7 Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.
Og Salomo helligede den mellemste Part af Forgaarden, som var foran Herrens Hus; thi han tillavede der Brændofrene og Fedtstykkerne af Takofrene, fordi det Kobberalter, som Salomo havde ladet gøre, ikke kunde tage imod Brændofferet og Madofferet og Fedtstykkerne.
8 Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto.
Og Salomo holdt paa den samme Tid en Højtid paa syv Dage og al Israel med ham, en saare stor Forsamling, fra Strækningen imellem Hamath og Ægyptens Bæk.
9 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero.
Og paa den ottende Dag holdt de en Slutningshøjtid; thi de holdt Alterets Indvielse i syv Dage og Højtiden i syv Dage.
10 Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.
Men paa den tre og tyvende Dag i den syvende Maaned lod han Folket fare til deres Telte, glade og ved et godt Mod over det gode, som Herren havde gjort imod David og Salomo og sit Folk Israel.
11 Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu,
Saa fuldendte Salomo Herrens Hus og Kongens Hus; og alt det, som var opkommet i Salomos Hjerte at gøre i Herrens Hus og i sit Hus, det fik han Lykke til.
12 Yehova anamuonekera usiku ndipo anati: “Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.
Og Herren aabenbarede sig for Salomo om Natten og sagde til ham: Jeg har hørt din Bøn og udvalgt mig dette Sted til et Offerhus.
13 “Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu,
Se, naar jeg tillukker Himmelen, at der ikke vorder Regn, og se, naar jeg byder Græshopper at æde Landet, eller naar jeg lader Pest komme iblandt mit Folk,
14 ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo.
og mit Folk, som er kaldet efter mit Navn, ydmyger sig, og de bede og søge mit Ansigt og omvende sig fra deres onde Vej: Saa vil jeg høre fra Himmelen af og forlade dem deres Synder og gøre deres Land sundt.
15 Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano.
Nu skulle mine Øjne være aabnede og mine Øren give Agt paa den Bøn, som sker paa dette Sted.
16 Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.
Og nu har jeg udvalgt og helliget mig dette Hus, at mit Navn skal være der indtil evig Tid, og mine Øjne og mit Hjerte skulle være der alle Dage.
17 “Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
Og du, om du vandrer for mit Ansigt, ligesom David, din Fader, har vandret, saa at du gør efter alt det, som jeg befalede dig, at du holder mine Skikke og mine Befalinger:
18 Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’
Saa vil jeg ogsaa stadfæste dit Riges Trone, ligesom jeg har gjort en Pagt med din Fader David og sagt: Dig skal ikke fattes en Mand, som skal herske i Israel.
19 “Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
Men dersom I vende eder bort og forlade mine Skikke og mine Bud, som jeg har givet for eders Ansigt, og I gaa hen og tjene andre Guder og tilbede dem:
20 pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
Da vil jeg oprykke eder af mit Land, som jeg har givet eder, og dette Hus, som jeg har helliget til mit Navn, vil jeg forkaste fra mit Ansigt, og jeg vil gøre det til et Ordsprog og til en Spot iblandt alle Folk.
21 Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
Og dette Hus, som har været højt, skulle alle, som gaa forbi det, grue for og sige: Hvorfor har Herren gjort saa imod dette Land og imod dette Hus?
22 Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
Og de skulle sige: Fordi de forlode Herren, deres Fædres Gud, som udførte dem af Ægyptens Land, og holdt fast ved andre Guder og tilbade dem og tjente dem: Derfor har han ladet alt dette onde komme over dem.

< 2 Mbiri 7 >