< 2 Mbiri 6 >
1 Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda;
Alors Salomon dit: Le Seigneur a promis qu’il habiterai dans une nuée;
2 ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”
Et moi j’ai élevé une maison à son nom, afin qu’il y habitât à perpétuité.
3 Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa.
Et le roi tourna sa face et bénit toute la multitude d’Israël (car toute la foule était debout et attentive), et il dit:
4 Ndipo inati, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati,
Béni soit le Seigneur Dieu d’Israël, qui a mis à effet ce qu’il promit à David, mon père, disant:
5 ‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba kuti ndizikhalamo kapena munthu wina aliyense kuti akhale mtsogoleri wa Aisraeli anthu anga.
Depuis le jour que j’ai retiré mon peuple de la terre d’Égypte, je n’ai point choisi de ville d’entre toutes les tribus d’Israël pour y bâtir une maison à mon nom, et je n’ai choisi aucun autre homme pour qu’il fût chef sur mon peuple Israël;
6 Koma tsopano ndasankha Yerusalemu kuti Dzina langa likhale kumeneko ndiponso ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’
Mais j’ai choisi Jérusalem pour que mon nom y soit, et j’ai choisi David pour l’établir sur mon peuple Israël.
7 “Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire Nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
Et lorsqu’il fut dans la volonté de David mon père de bâtir une maison au nom du Seigneur Dieu d’Israël,
8 Koma Yehova ananena kwa abambo anga Davide kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira Nyumba dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo.
Le Seigneur lui dit: Puisque ta volonté a été de bâtir une maison à mon nom, tu as certainement bien fait d’avoir une pareille volonté;
9 Komatu si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye amene adzandimangire Nyumba.’
Cependant ce ne sera pas toi qui bâtiras la maison; mais ton fils, qui sortira de tes flancs, bâtira lui-même la maison à mon nom.
10 “Yehova wasunga zimene analonjeza. Ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide, ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova Mulungu wa Israeli.
Le Seigneur accomplit donc sa parole qu’il avait dite: et moi, je me levai à la place de David, mon père; je me suis assis sur le trône d’Israël comme l’a dit le Seigneur, et j’ai bâti la maison au nom du Seigneur Dieu d’Israël.
11 Mʼmenemo ndayikamo Bokosi la Chipangano, mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi ana a Israeli.”
J’y ai mis l’arche, dans laquelle est l’alliance du Seigneur qu’il a faite avec les enfants d’Israël.
12 Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova patsogolo pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake.
Il se tint donc devant l’autel du Seigneur, en face de toute la multitude d’Israël, et il étendit ses mains;
13 Iyeyo anali atapanga nsanja yamkuwa, kutalika kwake kunali mamita awiri, mulifupi mwake munali mamita awiri, msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka ndipo nsanjayo anayimika pakati pa bwalo lakunja. Iye anayimirira pa nsanjapo nagwada pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba.
Car Salomon avait fait une estrade d’airain, et il l’avait placée au milieu de la basilique: elle avait cinq coudées de longueur, cinq coudées de largeur et trois coudées de hauteur; et il s’y tint debout; puis, les genoux fléchis en face de toute la multitude d’Israël, et les mains levées au ciel,
14 Iye anati, “Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pa dziko. Inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse.
Il dit: Seigneur Dieu d’Israël, il n’est pas un Dieu semblable à vous, dans le ciel et sur la terre; vous qui conservez l’alliance et la miséricorde à vos serviteurs qui marchent devant vous de tout leur cœur;
15 Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu monga mmene tikuonera lero lino.
Vous qui avez exécuté en faveur de votre serviteur David, mon père, toutes les paroles que vous lui aviez dites, et qui avez mis à effet ce que vous lui aviez promis de bouche, comme le présent temps le prouve.
16 “Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo ndi kusunga malamulo anga monga iwe wachitira.’
Maintenant donc, Seigneur Dieu d’Israël, accomplissez en faveur de votre serviteur, mon père David, tout ce que vous lui avez promis, disant: Il ne manquera pas devant moi d’homme, sorti de toi, qui soit assis sur le trône d’Israël, pourvu cependant que tes fils gardent leurs voies, et qu’ils marchent dans ma loi, comme toi-même tu as marché devant moi.
17 Ndipo tsopano Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide.
Et maintenant, Seigneur Dieu d’Israël, qu’elle soit confirmée, la parole que vous avez dite à votre serviteur David.
18 “Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi ndi munthu? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga!
Est-il donc croyable que Dieu habite avec les hommes sur la terre? Si le ciel et les cieux des cieux ne vous contiennent point, combien moins cette maison que j’ai bâtie!
19 Koma Inu Yehova, Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu.
Aussi a-t-elle été faite seulement pour que vous considériez, Seigneur mon Dieu, votre serviteur et ses supplications, et que vous écoutiez les prières que répand devant vous votre serviteur;
20 Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usana ndi usiku, malo ano amene Inu munati mudzayikamo Dzina lanu, imvani pemphero la mtumiki wanu limene akupemphera pa malo ano.
Pour que vous ouvriez les yeux sur cette maison pendant les jours et les nuits, sur ce lieu en lequel vous avez promis que votre nom serait invoqué,
21 Imvani mapembedzero a mtumiki wanu ndi a anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.
Et que vous exauceriez la demande que votre serviteur vous y adresse; et pour que vous exauciez les prières de votre serviteur et de votre peuple Israël. Quiconque priera en ce lieu, exaucez-le de votre demeure, c’est-à-dire des cieux, et soyez-lui propice.
22 “Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino,
Si quelqu’un pèche contre son prochain, et qu’il vienne prêt à jurer contre lui, et qu’il se lie par la malédiction devant l’autel dans cette maison,
23 imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.
Vous écouterez du ciel, et vous jugerez vos serviteurs, de telle sorte que vous rameniez la voie de l’homme inique sur sa propre tête, et que vous vengiez le juste, lui rendant selon sa justice.
24 “Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera pamaso panu mʼNyumba ino,
Si le peuple d’Israël est vaincu par ses ennemis (car ils pécheront contre vous), et que, convertis, ils fassent pénitence, invoquent votre nom, et prient en ce lieu,
25 pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa iwo ndi makolo awo.
Vous l’exaucerez du ciel; pardonnez le péché de votre peuple Israël, et ramenez-les dans la terre que vous leur avez donnée, à eux et à leurs pères.
26 “Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga,
Si, le ciel fermé, il ne tombe point de pluie à cause des péchés du peuple; s’ils prient en ce lieu et qu’ils rendent gloire à votre nom, et se convertissent de leurs péchés, lorsque vous les aurez affligés,
27 pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera, ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.
Exaucez-les du ciel, Seigneur, et pardonnez les péchés de vos serviteurs et de votre peuple Israël; enseignez-leur la bonne voie par laquelle ils doivent marcher, et donnez de la pluie à la terre que vous avez donnée à votre peuple pour la posséder.
28 “Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene adani azungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera,
S’il se lève sur la terre une famine, une peste, la rouille, l’aridité, la sauterelle et la chenille, et que les ennemis, après avoir ravagé les contrées, assiègent les portes de la ville, et que toute sorte de plaies et d’infirmités nous accable;
29 ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso ake ndi ululu wake, ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino,
Si quelqu’un de votre peuple Israël prie, reconnaissant sa plaie et son infirmité, et qu’il étende ses mains en cette maison,
30 pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita popeza Inu mumadziwa mtima wake, (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu),
Vous l’exaucerez du ciel, c’est-à-dire de votre demeure élevée; soyez propice, et rendez à chacun selon ses voies, que vous savez qu’il a en son cœur (car vous seul vous connaissez les cœurs des enfants des hommes);
31 motero iwo adzakuopani ndipo adzayenda mʼnjira zanu masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.
Afin qu’ils vous craignent et qu’ils marchent dans vos voies, pendant tous les jours qu’ils vivent sur la face de la terre que vous avez donnée à nos pères.
32 “Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu lotchukali, ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino,
Même l’étranger qui n’est point de votre peuple Israël, s’il vient d’une terre lointaine à cause de votre grand nom, et à cause de votre main puissante, de votre bras étendu, et qu’il vous adore en ce lieu,
33 pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi dzina lanu.
Vous l’exaucerez du ciel, votre demeure inébranlable, et vous ferez toutes les choses pour lesquelles cet étranger vous invoquera, afin que tous les peuples de la terre sachent votre nom, et qu’ils vous craignent comme le fait votre peuple Israël, et qu’ils reconnaissent que votre nom a été invoqué sur cette maison que j’ai bâtie.
34 “Anthu akapita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo akapemphera moyangʼana mzinda uno umene mwausankha ndi Nyumba yanu imene ndakumangirani,
Si votre peuple sort pour la guerre contre ses ennemis, et que dans la voie dans laquelle vous les aurez envoyés, ils vous adorent, tournés vers la voie dans laquelle est cette ville que vous avez choisie, et la maison que j’ai bâtie à votre nom,
35 pamenepo imvani kumwamba pemphero lawo ndi kupempha kwawo ndipo muwapulumutse.
Vous exaucerez du ciel leurs prières et leurs supplications, et veuillez les venger.
36 “Pamene achimwira inu, pakuti palibe amene sachimwa, ndipo inu mwawakwiyira ndi kuwapereka kwa adani awo, amene awatenga ukapolo ku dziko lawo lakutali kapena pafupi.
Que s’ils pèchent contre vous (car il n’y a point d’homme qui ne pèche), que si vous êtes irrité contre eux, et que vous les livriez à leurs ennemis, et que ceux-ci les emmènent captifs dans une terre lointaine, ou bien qui est proche,
37 Ngati asintha mitima yawo ku dziko limene ali akapolo ndi kulapa ndi kukudandaulirani inu mʼdziko la ukapolo wawo ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa ndipo tachita moyipa kwambiri.’
Et que, convertis en leur cœur, dans la terre dans laquelle ils auront été emmenés captifs, ils fassent pénitence, et vous prient dans la terre de leur captivité, disant: Nous avons péché, nous avons fait l’iniquité, et nous avons agi injustement,
38 Ndipo ngati atembenukira kwa inu ndi mtima ndi moyo wawo wonse mʼdziko lawo la ukapolo kumene anatengedwako ndi kupemphera moyangʼana dziko limene inu munalipereka kwa makolo awo, moyangʼana Nyumba yanu imene ndakumangirani;
Et qu’ils reviennent à vous en tout leur cœur et en toute leur âme dans la terre de leur captivité, dans laquelle ils ont été emmenés, et qu’ils vous adorent, tournés du côté de la terre que vous avez donnée à leurs pères, de la ville que vous avez choisie, et de la maison que j’ai bâtie à votre nom,
39 pamenepo imvani kumwamba, malo anu okhala, pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwapulumutse. Ndipo mukhululukire anthu anu, amene akuchimwirani.
Vous exaucerez du ciel, c’est-à-dire de votre demeure stable, leurs prières; veuillez faire justice, et pardonner votre peuple, quoique pécheur:
40 “Tsono Inu Mulungu wanga, tsekulani maso anu ndi makutu anu kuti mumve mapemphero ochitikira pa malo ano.
Car vous êtes mon Dieu. Que vos yeux soient ouverts, je vous en conjure, et que vos oreilles soient attentives à la prière qui se fait en ce lieu.
41 “Tsopano dzukani Inu Yehova Mulungu, ndipo bwerani ku malo anu ampumulo,
Maintenant donc, levez-vous, Seigneur Dieu, pour établir ici votre repos, vous et l’arche de votre puissance; que vos prêtres, Seigneur Dieu, soient revêtus de salut, et que vos saints se réjouissent en vos biens.
42 Inu Yehova Mulungu musamukane wodzozedwa wanu.
Seigneur mon Dieu, ne détournez pas la face de votre christ: souvenez-vous des miséricordes de David, votre serviteur.