< 2 Mbiri 6 >

1 Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda;
Then said Solomon, “The Lord said that he would dwell in the thick darkness.
2 ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”
And I have indeed built a dwelling-house for thee, and have settled a place for thy abode for ever.”
3 Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa.
And the king turned his face, and blessed the whole congregation of Israel, and all the congregation of Israel was standing.
4 Ndipo inati, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati,
And he said, Blessed be the Lord, the God of Israel, who spoke with his mouth unto David my father, and hath with his hands fulfilled it, when he said,
5 ‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba kuti ndizikhalamo kapena munthu wina aliyense kuti akhale mtsogoleri wa Aisraeli anthu anga.
Since the day that I brought forth my people out of the land of Egypt, I did not make choice of any city out of all the tribes of Israel to build a house, that my name might be therein; nor did I make choice of any man to be a ruler over my people of Israel;
6 Koma tsopano ndasankha Yerusalemu kuti Dzina langa likhale kumeneko ndiponso ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’
But I have made choice of Jerusalem, that my name might be there; and I have made choice of David to be over my people Israel,
7 “Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire Nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
And it was in the heart of David my father to build a house for the name of the Lord the God of Israel.
8 Koma Yehova ananena kwa abambo anga Davide kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira Nyumba dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo.
But the Lord said unto David my father, Whereas it was in thy heart to build a house unto my name, thou didst well in that it was in thy heart:
9 Komatu si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye amene adzandimangire Nyumba.’
Nevertheless thou shalt not thyself build the house; but thy son that shall come forth out of thy loins, he shall build the house unto my name.
10 “Yehova wasunga zimene analonjeza. Ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide, ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova Mulungu wa Israeli.
And the Lord hath fulfilled his word that he hath spoken; and I am risen up in the stead of David my father, and I sit on the throne of Israel, as the Lord hath spoken, and I have built the house unto the name of the Lord the God of Israel.
11 Mʼmenemo ndayikamo Bokosi la Chipangano, mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi ana a Israeli.”
And I have placed there the ark, wherein is the covenant of the Lord which he hath made with the children of Israel.
12 Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova patsogolo pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake.
And he now placed himself before the altar of the Lord in the presence of all the congregation of Israel, and spread forth his hands;
13 Iyeyo anali atapanga nsanja yamkuwa, kutalika kwake kunali mamita awiri, mulifupi mwake munali mamita awiri, msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka ndipo nsanjayo anayimika pakati pa bwalo lakunja. Iye anayimirira pa nsanjapo nagwada pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba.
For Solomon had made a laver of copper, and had placed it in the midst of the out-court, five cubits being its length, five cubits its breadth, and three cubits its height; and he placed himself upon it, and kneeled down upon his knees in the presence of all the congregation of Israel, and spread forth his hands toward heaven;
14 Iye anati, “Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pa dziko. Inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse.
And he said, O Lord God of Israel, there is no god like thee in the heavens, or on the earth, thou who keepest the covenant, and the kindness for thy servants that walk before thee with all their heart;
15 Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu monga mmene tikuonera lero lino.
Who has kept for thy servant David my father that which thou hadst promised him; and thou spokest with thy mouth, and hast fulfilled it with thy hand, as it is this day.
16 “Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo ndi kusunga malamulo anga monga iwe wachitira.’
And now, O Lord, God of Israel, keep for thy servant David my father that which thou hast spoken concerning him, saying, There shall never fail thee a man in my sight who sitteth on the throne of Israel, if thy children but take heed to their way to walk in my law, as thou hast walked before me.
17 Ndipo tsopano Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide.
And now, O Lord, the God of Israel, let thy word be verified, which thou hast spoken unto thy servant, unto David.
18 “Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi ndi munthu? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga!
For, in truth, will God then dwell with men on the earth? behold, the heavens and the heavens of heavens cannot contain thee: how much less then this house that I have built!
19 Koma Inu Yehova, Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu.
Yet wilt thou turn thy regard unto the prayer of thy servant, and to his supplication, O Lord my God, to listen unto the entreaty and the prayer which thy servant prayeth before thee:
20 Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usana ndi usiku, malo ano amene Inu munati mudzayikamo Dzina lanu, imvani pemphero la mtumiki wanu limene akupemphera pa malo ano.
That thy eyes may be open toward this house day and night, toward the place of which thou hast said that thou wouldst put thy name there; that thou mayest listen unto the prayer which thy servant will pray at this place.
21 Imvani mapembedzero a mtumiki wanu ndi a anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.
And listen thou to the supplications of thy servant, and of thy people Israel, which they will pray at this place: and oh, do thou hear from thy dwelling-place, from heaven; and hear, and forgive.
22 “Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino,
If any man trespass against his neighbor, and an oath be laid upon him to cause him to swear, and the oath come before thy altar in this house:
23 imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.
Then do thou hear from heaven, and act, and judge thy servants, by requiting the wicked, to bring his way upon his own head; and by justifying the righteous, to give him according to his righteousness.
24 “Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera pamaso panu mʼNyumba ino,
And if thy people Israel be struck down before the enemy, because they have sinned against thee, and they return and confess thy name, and pray, and make supplication before thee in this house:
25 pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa iwo ndi makolo awo.
Then do thou hear from heaven, and forgive the sin of thy people Israel, and cause them to return unto the land which thou hast given to them and to their fathers.
26 “Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga,
When the heavens be shut up, and there he no rain, because they have sinned against thee, and they pray toward this place, and confess thy name, and turn from their sin, because thou hast afflicted them:
27 pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera, ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.
Then do thou hear in heaven, and forgive the sin of thy servants, and of thy people Israel; for thou wilt direct them unto the good way, wherein they should walk; and give then rain upon thy land, which thou hast given unto thy people for an inheritance.
28 “Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene adani azungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera,
If there be famine in the land, if there be pestilence, blasting, or mildew, if there be locusts, or caterpillars; if their enemies besiege them in their land, in their gates at whatsoever plague, and at whatsoever sickness;
29 ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso ake ndi ululu wake, ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino,
What prayer and what supplication soever be made by any man, or by all thy people Israel, when they shall be conscious every man of his plague and his pain, and he then spread forth his hands toward this house:
30 pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita popeza Inu mumadziwa mtima wake, (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu),
Then do thou hear from heaven the place of thy dwelling, and forgive, and give to every man in accordance with all his ways, as thou mayest know his heart; for thou, thyself alone, knowest the heart of the children of men;
31 motero iwo adzakuopani ndipo adzayenda mʼnjira zanu masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.
In order that they may fear thee, to walk in thy ways, all the days that they live on the face of the land which thou hast given unto our fathers.
32 “Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu lotchukali, ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino,
But also to the stranger, who is not of thy people Israel, but cometh out of a far-off country for the sake of thy great name, and of thy mighty hand, and of thy outstretched arm, — if they come and pray in this house, —
33 pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi dzina lanu.
Mayest thou likewise listen from heaven, from the place of thy dwelling, and do according to all that the stranger will call on thee for: in order that all people of the earth may know thy name, both to fear thee, as do thy people Israel, and to understand that this house, which I have built, is called by thy name.
34 “Anthu akapita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo akapemphera moyangʼana mzinda uno umene mwausankha ndi Nyumba yanu imene ndakumangirani,
If thy people go out to battle against their enemies on the way on which thou mayest send them, and they do pray unto thee in the direction of this city which thou hast chosen, and of the house that I have built unto thy name:
35 pamenepo imvani kumwamba pemphero lawo ndi kupempha kwawo ndipo muwapulumutse.
Then hear thou from heaven their prayer and their supplication, and procure them justice.
36 “Pamene achimwira inu, pakuti palibe amene sachimwa, ndipo inu mwawakwiyira ndi kuwapereka kwa adani awo, amene awatenga ukapolo ku dziko lawo lakutali kapena pafupi.
If they sin against thee—for there is no man that may not sin, —and thou be angry with them, and give them up before the enemy, so that their captors carry them away captive unto a land far off or near;
37 Ngati asintha mitima yawo ku dziko limene ali akapolo ndi kulapa ndi kukudandaulirani inu mʼdziko la ukapolo wawo ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa ndipo tachita moyipa kwambiri.’
And if they then take it to their heart in the land whither they have been carried captive, and repent and make supplication unto thee in the land of their captivity, saying, We have sinned, we have committed iniquity, and have acted wickedly;
38 Ndipo ngati atembenukira kwa inu ndi mtima ndi moyo wawo wonse mʼdziko lawo la ukapolo kumene anatengedwako ndi kupemphera moyangʼana dziko limene inu munalipereka kwa makolo awo, moyangʼana Nyumba yanu imene ndakumangirani;
And they return unto thee with all their heart and with all their soul in the land of their captivity, whither they have been carried captive, and they pray in the direction of their land, which thou hast given unto their fathers, and of the city which thou hast chosen, and toward the house which I have built unto thy name:
39 pamenepo imvani kumwamba, malo anu okhala, pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwapulumutse. Ndipo mukhululukire anthu anu, amene akuchimwirani.
Then hear thou from heaven, from the place of thy dwelling, their prayer and their supplications, and procure them justice, and forgive thy people for what they have sinned against thee.
40 “Tsono Inu Mulungu wanga, tsekulani maso anu ndi makutu anu kuti mumve mapemphero ochitikira pa malo ano.
Now, my God, let I beseech thee, thy eyes be open, and thy ears be attentive unto the prayer on this place.
41 “Tsopano dzukani Inu Yehova Mulungu, ndipo bwerani ku malo anu ampumulo,
And now arise, O Lord God, unto thy resting-place, thou, and the ark of thy strength: let thy priests, O Lord God, clothe themselves with salvation, and let thy pious servants rejoice in happiness.
42 Inu Yehova Mulungu musamukane wodzozedwa wanu.
O Lord God, turn not away the face of thy anointed: remember the pious deeds of David thy servant.

< 2 Mbiri 6 >