< 2 Mbiri 5 >

1 Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
Tous les travaux, entrepris par le roi Salomon pour la maison du Seigneur, étant terminés, Salomon réunit les legs pieux de David, son père, en argent, or, vases de toute sorte, et les déposa dans les trésors du temple de Dieu.
2 Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
Alors Salomon convoqua à Jérusalem les anciens d’Israël, tous les chefs de tribu et chefs de famille des enfants d’Israël, pour procéder au transfert de l’arche d’alliance de l’Eternel de la cité de David, qui est Sion.
3 Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Tous les citoyens d’Israël se réunirent auprès du roi Salomon, pendant la fête qui tombe dans le septième mois.
4 Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
Tous les anciens d’Israël étant arrivés, les Lévites se chargèrent de l’arche.
5 ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
On transporta l’arche, la Tente d’assignation et tous les objets sacrés qui s’y trouvaient prêtres et Lévites les transportèrent ensemble.
6 ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
Le roi Salomon et toute la communauté d’Israël rassemblée près de lui, se plaçant devant l’arche, firent des sacrifices de menu et de gros bétail, si nombreux qu’on n’aurait pu les compter.
7 Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
Alors les prêtres installèrent l’arche d’alliance de l’Eternel à la place qui lui était assignée, dans le debir du temple ou Saint des Saints, sous les ailes des chérubins.
8 Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
Les chérubins déployaient leurs ailes dans la direction de l’arche, de sorte qu’ils couvraient, en les dominant, l’arche et ses barres.
9 Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
On avait prolongé ces barres, de façon que leurs extrémités s’apercevaient de l’enceinte sacrée, à l’entrée du debir, mais n’étaient pas apparentes extérieurement; elles y sont restées jusqu’à ce jour.
10 Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
Il n’y avait dans l’arche que les deux tables de pierre que Moïse y déposa près de l’Horeb, alors que l’Eternel conclut un pacte avec les Israélites, après leur sortie d’Egypte.
11 Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
Or, lorsque les prêtres sortirent du lieu saint, car tous les prêtres présents s’étaient sanctifiés, l’ordre des classes ne pouvant être observé,
12 Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
de même les Lévites, et tous les chantres, Assaph, Hêmân, Yedouthoun, leurs fils et leurs frères, vêtus de byssus et munis de cymbales, de luths, et de harpes, étaient placés à l’est de l’autel; près d’eux des prêtres, au nombre de cent vingt, sonnaient de la trompette;
13 Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
lorsque donc sonneurs de trompettes et chanteurs entonnèrent à l’unisson les louanges et les actions de grâces à l’Eternel, lorsque les accents des trompettes, des cymbales, des autres instruments de musique accompagnèrent le chant: "Gloire au Seigneur; car il est bon, car sa grâce dure à jamais!", la maison, le temple du Seigneur fut rempli d’une nuée,
14 choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
et les prêtres ne purent, par suite, s’y tenir pour faire leur service, parce que la majesté divine remplissait la maison de Dieu.

< 2 Mbiri 5 >