< 2 Mbiri 5 >

1 Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
And so was ended all the work which Solomon made for the house of the Lord; and Solomon brought in the things sanctified by David his father; and the silver, and the gold, and all the vessels he placed in the treasuries of the house of God.
2 Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
Then did Solomon assemble the elders of Israel, and all the heads of the tribes, the princes of the divisions of the children of Israel, unto Jerusalem, to bring up the ark of the covenant of the Lord out of the city of David, which is Zion.
3 Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
And all the men of Israel assembled themselves unto the king at the feast which is [in] the seventh month.
4 Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
All the elders of Israel came, and the Levites took up the ark.
5 ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
And they brought up the ark, and the tabernacle of the congregation, and all the holy vessels that were in the tabernacle: these did the priests and the Levites bring up.
6 ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
And king Solomon, and all the congregation of Israel that were assembled unto him were before the ark, sacrificing sheep and oxen, which could not be numbered nor told for multitude.
7 Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
And the priests brought in the ark of the covenant of the Lord unto its place, into the debir of the house, into the most holy place, under the wings of the cherubim.
8 Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
And the cherubim spread forth their wings over the place of the ark, and the cherubim covered the ark and its staves from above.
9 Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
And they had made the staves so long that the ends of the staves were seen [standing out] from the ark in the front of the debir; but they were not seen without; and they have remained there until this day.
10 Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
There was nothing in the ark save the two tables which Moses had placed [therein] at Horeb, where the Lord made a covenant with the children of Israel, when they came out of Egypt.
11 Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
And it came to pass, when the priests were come out of the holy place; for all the priests that were present had sanctified themselves, the divisions not having been observed; —
12 Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
And the Levites the singers, all together, of Assaph, of Heman, of Jeduthun, with their sons and their brethren, arrayed in white linen, having cymbals and psalteries and harps, stood at the east side of the altar, and with them were one hundred and twenty priests blowing on trumpets; —
13 Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
And it came thus to pass, as the trumpeters and singers were as one, to make one sound to be heard in praising and thanking the Lord; and when they lifted up their voice [accompanied] with trumpets and cymbals and instruments of music, and in praising the Lord, For he is good; because unto everlasting endureth his kindness: that the house, even the house of the Lord, was filled with a cloud;
14 choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
And the priests were not able to stand to minister because of the cloud; for the glory of the Lord had filled the house of God.

< 2 Mbiri 5 >