< 2 Mbiri 5 >

1 Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
Then Solomon brought in all the things that David his father had vowed, the silver, and the gold, and all the vessels he put among the treasures of the house of God.
2 Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
And after this he gathered together the ancients of Israel, and all the princes of the tribes, and the heads of the families, of the children of Israel to Jerusalem, to bring the ark of the covenant of the Lord out of the city of David, which is Sion.
3 Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
And all the men of Israel came to the king in the solemn day of the seventh month.
4 Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
And when all the ancients of Israel were come, the Levites took up the ark,
5 ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
And brought it in, together with all the furniture of the tabernacle. And the priests with the Levites carried the vessels of the sanctuary, which were in the tabernacle.
6 ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
And king Solomon and all the assembly of Israel, and all that were gathered together before the ark, sacrificed rams, and oxen without number: so great was the multitude of the victims.
7 Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
And the priests brought in the ark of the covenant of the Lord into its place, that is, to the oracle of the temple, into the holy of holies under the wings of the cherubims:
8 Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
So that the cherubims spread their wings over the place, in which the ark was set, and covered the ark itself and its staves.
9 Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
Now the ends of the staves wherewith the ark was carried, because they were some thing longer, were seen before the oracle: but if a man were a little outward, he could not see them. So the ark has been there unto this day.
10 Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
And there was nothing else in the ark but the two tables which Moses put there at Horeb when the Lord gave the law to the children of Israel, at their coming out of Egypt.
11 Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
Now when the priests were come out of the sanctuary, (for all the priests that could be found there, mere sanctified: and as yet at that time the courses and orders of the ministries were not divided among them, )
12 Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
Both the Levites and the singing men, that is, both they that were under Asaph, and they that were under Heman, and they that were under Idithun, with their sons, and their brethren, clothed with fine linen, sounded with cymbals, and psalteries, and harps, standing on the east side of the altar, and with them a hundred and twenty priests, sounding with trumpets.
13 Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
So when they all sounded together, both with trumpets, and voice, and cymbals, and organs, and with divers kind of musical instruments, and lifted up their voice on high: the sound was heard afar off, so that when they began to praise the Lord, and to say: Give glory to the Lord for he is good, for his mercy endureth for ever: the house of God was filled with a cloud.
14 choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
Nor could the priests stand and minister by reason of the cloud. For the glory of the Lord had filled the house of God.

< 2 Mbiri 5 >