< 2 Mbiri 36 >
1 Tsono anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namuyika kukhala mfumu mu Yerusalemu mʼmalo mwa abambo ake.
Och folket i landena tog Joahas, Josia son, och gjorde honom till Konung i hans faders stad i Jerusalem.
2 Yowahazi anali wa zaka 23 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu.
Tre och tjugu åra gammal var Joahas, då han Konung vardt och regerade i tre månader i Jerusalem.
3 Mfumu ya Igupto inamuchotsa pa udindo wa ufumu mu Yerusalemu ndipo inakhometsa msonkho dziko la Yuda wa makilogalamu 3,400 asiliva ndi agolide.
Ty Konungen i Egypten satte honom af i Jerusalem, och beskattade landet till hundrade centener silfver, och en centener guld.
4 Mfumu ya Igupto inakhazika Eliyakimu, mʼbale wake wa Yehowahazi kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu ndipo anasintha dzina la Eliyakimu kukhala Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yowahazi mʼbale wake wa Eliyakimu ndi kupita naye ku Igupto.
Och Konungen i Egypten gjorde Eliakim, hans broder, till Konung öfver Juda och Jerusalem, och förvände hans namn Jojakim; men Necho tog hans broder Joahas, och förde honom uti Egypten.
5 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake.
Fem och tjugu åra gammal var Jojakim, då han Konung vardt; och regerade ellofva år i Jerusalem, och gjorde det ondt var för Herranom sinom Gud.
6 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anachita naye nkhondo ndipo anamumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kumutenga kupita naye ku Babuloni.
Och NebucadNezar, Konungen i Babel, drog upp emot honom, och band honom med kedjor, att han skulle föra honom till Babel.
7 Nebukadinezara anatenganso zipangizo za ku Nyumba ya Yehova kupita nazo ku Babuloni ndipo anaziyika mʼnyumba ya Mulungu wake kumeneko.
Och förde NebucadNezar någor Herrans hus kärile till Babel, och satte dem uti sitt tempel i Babel.
8 Zochitika zina za pa ulamuliro wa Yehoyakimu, zinthu zonyansa zimene anachita ndi zonse zinapezeka kuti zinali zomutsutsa zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Hvad nu mer af Jojakim sägande är, och hans styggelse, som han gjorde, och med honom funnen vordo, si, de äro skrifne uti Israels och Juda Konungars bok: och hans son Jojachin vardt Konung i hans stad.
9 Yehoyakini anali ndi zaka 21 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu ndi masiku khumi. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Åtta åra gammal var Jojachin, då han Konung vardt, och regerade i tre månader och tio dagar i Jerusalem, och gjorde det Herranom illa behagade.
10 Nthawi ya mphukira, mfumu Nebukadinezara inayitanitsa Yehoyakini ndipo inapita naye ku Babuloni, pamodzi ndi ziwiya zamtengowapatali za mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova, ndipo anayika Zedekiya malume wake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.
Då nu året omgick, sände NebucadNezar, och lät hemta honom till Babel, med de kosteliga tygen i Herrans hus; och man gjorde Zedekia hans broder till Konung öfver Juda och Jerusalem.
11 Zedekiya anali ndi zaka 21 pamene ankakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11.
Ett och tjugu åra gammal var Zedekia, då han Konung vardt; och regerade ellofva år i Jerusalem;
12 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake ndipo sanadzichepetse yekha pamaso pa mneneri Yeremiya amene ankayankhula mawu a Yehova.
Och gjorde det ondt var för Herranom sinom Gud, och ödmjukade sig intet för den Propheten Jeremia, som talade utaf Herrans mun.
13 Iye anawukiranso mfumu Nebukadinezara amene anamulumbiritsa mʼdzina la Mulungu. Iyeyo anali wosamva ndipo anawumitsa mtima wake. Sanatembenukire kwa Yehova Mulungu wa Israeli.
Dertill vardt han affällig ifrå NebucadNezar, Konungenom i Babel, hvilken af honom en ed vid Gud tagit hade; och vardt halsstyf, och förstockade sitt hjerta, så att han intet omvände sig till Herran Israels Gud.
14 Kuwonjezera apo, atsogoleri onse a ansembe ndi anthu ena anapitirapitira kukhala osakhulupirika, kutsatira machitidwe onse onyansa a mitundu ina ndi kudetsa Nyumba ya Yehova Mulungu wawo, imene anayipatula mu Yerusalemu.
Sammalunda alle öfverstarna ibland Presterna, samt med folket, syndade svårliga, och förtogo sig med allahanda Hedningastyggelse, och orenade Herrans hus, det han helgat hade i Jerusalem.
15 Yehova, Mulungu wa makolo awo, ankatumiza mawu kwa iwo kudzera kwa amithenga ake kawirikawiri, chifukwa ankawamvera chisoni anthu ake ndi malo ake okhalapo.
Och Herren deras fäders Gud sände till dem med sin bådskap bittida; ty han skonade sitt folk och sina boning.
16 Koma iwo ananyoza amithenga a Mulungu, anapeputsa mawu awo ndipo ankaseka aneneri ake mpaka anawutsa mkwiyo wa Yehova pa anthu ake ndipo panalibenso mankhwala owachiritsa.
Men de begabbade Guds bådskap, och föraktade hans ord, och bespottade hans Propheter, intilldess Herrans grymhet växte öfver hans folk, att dem nu intet mer stod till botande.
17 Yehova anabweretsa mfumu ya anthu a ku Babuloni, imene inapha anyamata awo ndi lupanga ku malo opatulika, ndipo sanasiye kaya mnyamata kapena mtsikana, wamkulu kapena wokalamba. Mulungu anapereka onsewo kwa Nebukadinezara.
Ty han förde öfver dem de Chaldeers Konung, och lät dräpa deras unga män med svärd, uti deras helgedoms huse, och skonade hvarken piltar eller pigor, hvarken åldrigom eller utgamlom; alla gaf han dem i hans hand.
18 Iye ananyamula kupita nazo ku Babuloni zipangizo zonse za mʼNyumba ya Yehova Mulungu wawo, zazikulu ndi zazingʼono zomwe, ndi chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso chuma cha mfumu ndi akuluakulu ake.
Och all tyg i Guds hus, stor och små, håfvorna i Herrans hus, och Konungens och hans Förstars håfvor; allt lät han föra till Babel.
19 Iwo anayatsa moto Nyumba ya Mulungu, ndipo anagwetsa makoma a Yerusalemu. Anatentha moto nyumba zonse zaufumu ndipo anawononga chilichonse chimene chinali chofunika.
Och de brände upp Guds hus, och bröto ned murarna i Jerusalem; och all deras palats brände de upp med eld, så att all deras kosteliga ting blefvo förfaren.
20 Iye anagwira ukapolo anthu otsala amene anapulumuka ku lupanga ndi kupita nawo ku Babuloni, ndipo anakhala antchito ake ndi ana ake mpaka pamene ufumu wa Peresiya unakhazikitsidwa.
Och de som för svärdet undsluppo, fördes till Babel, och vordo hans och hans söners trälar, tilldess riket kom till de Perser;
21 Dziko linakondwera ndi masabata ake. Pa nthawi yonse ya chipasuko chake nthaka inapuma, mpaka zaka 70 zinakwana pokwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya.
På det att fullkomnas skulle Herrans ord genom Jeremia mun, tilldess att landet hade fyllest i sina Sabbather; förty hele tiden af förderfvelsen var Sabbath, intilldess sjutio år fullkomnade vordo.
22 Mʼchaka choyamba cha Koresi mfumu ya Peresiya, pofuna kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anakhudza mtima wa mfumu ya Peresiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse ndipo anazilemba:
Men i första årena Cores, Konungens i Persien, på det fullkomnadt skulle varda Herrans ord, taladt genom Jeremia mun, uppväckte Herren Cores anda, Konungens i Persien, att han lät utropa öfver allt sitt rike, ja ock med bref, och säga:
23 Chimene mfumu Koresi ya Peresiya ikunena ndi ichi: “Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa ine mafumu onse a dziko lapansi ndipo wandisankha kuti ndimumangire Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ku Yuda. Aliyense wa anthu ake pakati panu, Yehova Mulungu wake akhale naye, ndipo apite.”
Detta säger Cores, Konungen i Persien: Herren Gud af himmelen hafver gifvit mig all rike i landen, och hafver befallt mig bygga sig ett hus i Jerusalem i Juda; hvilken som nu ibland eder är af hans folk, med honom vare Herren hans Gud, och drage ditupp.