< 2 Mbiri 36 >
1 Tsono anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namuyika kukhala mfumu mu Yerusalemu mʼmalo mwa abambo ake.
And they took [the] people of the land Jehoahaz [the] son of Josiah and they made king him in place of father his in Jerusalem.
2 Yowahazi anali wa zaka 23 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu.
[was] a son of Three and twenty year[s] Jehoahaz when became king he and three months he reigned in Jerusalem.
3 Mfumu ya Igupto inamuchotsa pa udindo wa ufumu mu Yerusalemu ndipo inakhometsa msonkho dziko la Yuda wa makilogalamu 3,400 asiliva ndi agolide.
And he removed him [the] king of Egypt in Jerusalem and he imposed a fine on the land one hundred talent[s] of silver and a talent of gold.
4 Mfumu ya Igupto inakhazika Eliyakimu, mʼbale wake wa Yehowahazi kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu ndipo anasintha dzina la Eliyakimu kukhala Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yowahazi mʼbale wake wa Eliyakimu ndi kupita naye ku Igupto.
And he made king [the] king of Egypt Eliakim brother his over Judah and Jerusalem and he changed name his Jehoiakim and Jehoahaz brother his he took Necho and he brought him Egypt towards.
5 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake.
[was] a son of Twenty and five year[s] Jehoiakim when became king he and one [plus] ten year[s] he reigned in Jerusalem and he did the evil in [the] eyes of Yahweh God his.
6 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anachita naye nkhondo ndipo anamumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kumutenga kupita naye ku Babuloni.
On him he came up Nebuchadnezzar [the] king of Babylon and he bound him with bronze fetters to take him Babylon towards.
7 Nebukadinezara anatenganso zipangizo za ku Nyumba ya Yehova kupita nazo ku Babuloni ndipo anaziyika mʼnyumba ya Mulungu wake kumeneko.
And some of [the] articles of [the] house of Yahweh he brought Nebuchadnezzar to Babylon and he put them in palace his in Babylon.
8 Zochitika zina za pa ulamuliro wa Yehoyakimu, zinthu zonyansa zimene anachita ndi zonse zinapezeka kuti zinali zomutsutsa zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And [the] rest of [the] matters of Jehoiakim and abominations his which he did and [what] was found on him there they [are] written on [the] scroll of [the] kings of Israel and Judah and he became king Jehoiachin son his in place of him.
9 Yehoyakini anali ndi zaka 21 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu ndi masiku khumi. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
[was] a son of Eight years Jehoiachin when became king he and three months and ten days he reigned in Jerusalem and he did the evil in [the] eyes of Yahweh.
10 Nthawi ya mphukira, mfumu Nebukadinezara inayitanitsa Yehoyakini ndipo inapita naye ku Babuloni, pamodzi ndi ziwiya zamtengowapatali za mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova, ndipo anayika Zedekiya malume wake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.
And to [the] return of the year he sent the king Nebuchadnezzar and he brought him Babylon towards with [the] articles of preciousness of [the] house of Yahweh and he made king Zedekiah relative his over Judah and Jerusalem.
11 Zedekiya anali ndi zaka 21 pamene ankakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11.
[was] a son of Twenty and one year[s] Zedekiah when became king he and one [plus] ten year[s] he reigned in Jerusalem.
12 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake ndipo sanadzichepetse yekha pamaso pa mneneri Yeremiya amene ankayankhula mawu a Yehova.
And he did the evil in [the] eyes of Yahweh God his not he humbled himself from to before Jeremiah the prophet from [the] mouth of Yahweh.
13 Iye anawukiranso mfumu Nebukadinezara amene anamulumbiritsa mʼdzina la Mulungu. Iyeyo anali wosamva ndipo anawumitsa mtima wake. Sanatembenukire kwa Yehova Mulungu wa Israeli.
And also against the king Nebuchadnezzar he rebelled who he had made swear an oath him by God and he made stiff neck his and he made hard heart his from turning back to Yahweh [the] God of Israel.
14 Kuwonjezera apo, atsogoleri onse a ansembe ndi anthu ena anapitirapitira kukhala osakhulupirika, kutsatira machitidwe onse onyansa a mitundu ina ndi kudetsa Nyumba ya Yehova Mulungu wawo, imene anayipatula mu Yerusalemu.
Also all [the] leaders of the priests and the people they increased (to act unfaithfully *Q(K)*) unfaithfulness according to all [the] abominations of the nations and they made unclean [the] house of Yahweh which he had consecrated in Jerusalem.
15 Yehova, Mulungu wa makolo awo, ankatumiza mawu kwa iwo kudzera kwa amithenga ake kawirikawiri, chifukwa ankawamvera chisoni anthu ake ndi malo ake okhalapo.
And he sent Yahweh [the] God of ancestors their to them by [the] hand of messengers his rising early and sending for he had compassion on people his and on dwelling place his.
16 Koma iwo ananyoza amithenga a Mulungu, anapeputsa mawu awo ndipo ankaseka aneneri ake mpaka anawutsa mkwiyo wa Yehova pa anthu ake ndipo panalibenso mankhwala owachiritsa.
And they were deriding [the] messengers of God and despising words his and mocking at prophets his until came up [the] anger of Yahweh on people his until there not [was] healing.
17 Yehova anabweretsa mfumu ya anthu a ku Babuloni, imene inapha anyamata awo ndi lupanga ku malo opatulika, ndipo sanasiye kaya mnyamata kapena mtsikana, wamkulu kapena wokalamba. Mulungu anapereka onsewo kwa Nebukadinezara.
And he brought up on them [the] king of ([the] Chaldeans *Q(k)*) and he killed young men their with the sword in [the] house of sanctuary their and not he had compassion on young man and young woman [the] old and [the] decrepit everyone he gave in hand his.
18 Iye ananyamula kupita nazo ku Babuloni zipangizo zonse za mʼNyumba ya Yehova Mulungu wawo, zazikulu ndi zazingʼono zomwe, ndi chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso chuma cha mfumu ndi akuluakulu ake.
And all [the] articles of [the] house of God great and small and [the] treasures of [the] house of Yahweh and [the] treasures of the king and officials his everything he brought Babylon.
19 Iwo anayatsa moto Nyumba ya Mulungu, ndipo anagwetsa makoma a Yerusalemu. Anatentha moto nyumba zonse zaufumu ndipo anawononga chilichonse chimene chinali chofunika.
And they burned [the] house of God and they pulled down [the] wall of Jerusalem and all palaces its they burned with fire and all [the] articles of preciousness its to destroy.
20 Iye anagwira ukapolo anthu otsala amene anapulumuka ku lupanga ndi kupita nawo ku Babuloni, ndipo anakhala antchito ake ndi ana ake mpaka pamene ufumu wa Peresiya unakhazikitsidwa.
And he took into exile the remainder from the sword to Babylon and they became for him and for sons his slaves until reigned [the] kingdom of Persia.
21 Dziko linakondwera ndi masabata ake. Pa nthawi yonse ya chipasuko chake nthaka inapuma, mpaka zaka 70 zinakwana pokwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya.
To fulfill [the] word of Yahweh by [the] mouth of Jeremiah until it has accepted the land sabbaths its all [the] days of the desolation of it it rested to complete seventy year[s].
22 Mʼchaka choyamba cha Koresi mfumu ya Peresiya, pofuna kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anakhudza mtima wa mfumu ya Peresiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse ndipo anazilemba:
And in year one of Cyrus [the] king of Persia to fulfill [the] word of Yahweh by [the] mouth of Jeremiah he stirred up Yahweh [the] spirit of Cyrus [the] king of Persia and he caused to pass a proclamation in all kingdom his and also in writing saying.
23 Chimene mfumu Koresi ya Peresiya ikunena ndi ichi: “Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa ine mafumu onse a dziko lapansi ndipo wandisankha kuti ndimumangire Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ku Yuda. Aliyense wa anthu ake pakati panu, Yehova Mulungu wake akhale naye, ndipo apite.”
Thus he says Cyrus - [the] king of Persia all [the] kingdoms of the earth he has given to me Yahweh [the] God of the heavens and he he has appointed me to build for him a house in Jerusalem which [is] in Judah who? [is] among you from all people his Yahweh God his [be] with him and let him go up.