< 2 Mbiri 36 >

1 Tsono anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namuyika kukhala mfumu mu Yerusalemu mʼmalo mwa abambo ake.
Og Folket i Landet tog Joakas, Josias's Søn, og de gjorde ham til Konge i hans Faders Sted, i Jerusalem.
2 Yowahazi anali wa zaka 23 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu.
Joakas var tre og tyve Aar gammel, der han blev Konge, og regerede tre Maaneder i Jerusalem;
3 Mfumu ya Igupto inamuchotsa pa udindo wa ufumu mu Yerusalemu ndipo inakhometsa msonkho dziko la Yuda wa makilogalamu 3,400 asiliva ndi agolide.
men Kongen af Ægypten afsatte ham i Jerusalem og straffede Landet paa hundrede Centner Sølv og et Centner Guld.
4 Mfumu ya Igupto inakhazika Eliyakimu, mʼbale wake wa Yehowahazi kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu ndipo anasintha dzina la Eliyakimu kukhala Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yowahazi mʼbale wake wa Eliyakimu ndi kupita naye ku Igupto.
Og Kongen af Ægypten gjorde Eliakim, hans Broder, til Konge over Juda og Jerusalem og omvendte hans Navn til Jojakim; men Neko tog hans Broder Joakas og førte ham til Ægypten.
5 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake.
Jojakim var fem og tyve Aar gammel, der han blev Konge, og regerede elleve Aar i Jerusalem; og han gjorde det, som var ondt for Herrens, hans Guds, Øjne.
6 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anachita naye nkhondo ndipo anamumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kumutenga kupita naye ku Babuloni.
Nebukadnezar, Kongen af Babel, drog op imod ham og bandt ham med to Kobberlænker for at føre ham til Babel.
7 Nebukadinezara anatenganso zipangizo za ku Nyumba ya Yehova kupita nazo ku Babuloni ndipo anaziyika mʼnyumba ya Mulungu wake kumeneko.
Og Nebukadnezar førte nogle af Herrens Hus's Kar til Babel og lagde dem i sit Tempel i Babel.
8 Zochitika zina za pa ulamuliro wa Yehoyakimu, zinthu zonyansa zimene anachita ndi zonse zinapezeka kuti zinali zomutsutsa zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Men det øvrige af Jojakims Handeler og hans Vederstyggeligheder, som han gjorde, og det, som fandtes hos ham, se, de Ting ere skrevne i Israels og Judas Kongers Bog; og Jojakin, hans Søn, blev Konge i hans Sted.
9 Yehoyakini anali ndi zaka 21 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu ndi masiku khumi. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Jojakin var otte Aar gammel, der han blev Konge, og regerede tre Maaneder og ti Dage i Jerusalem og gjorde det, som var ondt for Herrens Øjne.
10 Nthawi ya mphukira, mfumu Nebukadinezara inayitanitsa Yehoyakini ndipo inapita naye ku Babuloni, pamodzi ndi ziwiya zamtengowapatali za mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova, ndipo anayika Zedekiya malume wake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.
Men der Aaret var omme, sendte Kong Nebukadnezar hen og lod ham føre til Babel tillige med Herrens Hus's kostelige Kar og gjorde Zedekias, hans Broder, til Konge over Juda og Jerusalem.
11 Zedekiya anali ndi zaka 21 pamene ankakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11.
Zedekias var et og tyve Aar gammel, der han blev Konge, og regerede elleve Aar i Jerusalem.
12 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake ndipo sanadzichepetse yekha pamaso pa mneneri Yeremiya amene ankayankhula mawu a Yehova.
Og han gjorde det, som var ondt for Herren, hans Guds, Øjne; han ydmygede sig ikke for Profeten Jeremias, som talte af Herrens Mund.
13 Iye anawukiranso mfumu Nebukadinezara amene anamulumbiritsa mʼdzina la Mulungu. Iyeyo anali wosamva ndipo anawumitsa mtima wake. Sanatembenukire kwa Yehova Mulungu wa Israeli.
Tilmed faldt han og af fra Kong Nebukadnezar, som havde ladet ham sværge ved Gud; og han gjorde sin Nakke stiv og forhærdede sit Hjerte og vilde ikke omvende sig til Herren, Israels Gud.
14 Kuwonjezera apo, atsogoleri onse a ansembe ndi anthu ena anapitirapitira kukhala osakhulupirika, kutsatira machitidwe onse onyansa a mitundu ina ndi kudetsa Nyumba ya Yehova Mulungu wawo, imene anayipatula mu Yerusalemu.
Og alle de øverste iblandt Præsterne og Folket forsyndede sig saare meget, idet de efterlignede alle Hedningernes Vederstyggeligheder og besmittede Herrens Hus, som han havde helliget i Jerusalem.
15 Yehova, Mulungu wa makolo awo, ankatumiza mawu kwa iwo kudzera kwa amithenga ake kawirikawiri, chifukwa ankawamvera chisoni anthu ake ndi malo ake okhalapo.
Og Herren, deres Fædres Gud, sendte til dem ved sine Sendebud tidligt og ideligt; thi han vilde skaane sit Folk og sin Bolig.
16 Koma iwo ananyoza amithenga a Mulungu, anapeputsa mawu awo ndipo ankaseka aneneri ake mpaka anawutsa mkwiyo wa Yehova pa anthu ake ndipo panalibenso mankhwala owachiritsa.
Men de bespottede Guds Sendebud og foragtede hans Ord og forhaanede hans Profeter, indtil Herrens Vrede tog til over hans Folk, indtil der var ingen Lægedom mere.
17 Yehova anabweretsa mfumu ya anthu a ku Babuloni, imene inapha anyamata awo ndi lupanga ku malo opatulika, ndipo sanasiye kaya mnyamata kapena mtsikana, wamkulu kapena wokalamba. Mulungu anapereka onsewo kwa Nebukadinezara.
Og han førte Kaldæernes Konge op imod dem, og denne ihjelslog deres unge Karle med Sværd udi deres Helligdoms Hus og sparede hverken unge Karle eller Jomfruer, gamle eller udlevede; han gav dem alle i hans Haand.
18 Iye ananyamula kupita nazo ku Babuloni zipangizo zonse za mʼNyumba ya Yehova Mulungu wawo, zazikulu ndi zazingʼono zomwe, ndi chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso chuma cha mfumu ndi akuluakulu ake.
Og alle Kar fra Guds Hus, store og smaa, og Herrens Hus's Skatte og Kongens og hans Fyrsters Skatte førte han alt sammen til Babel.
19 Iwo anayatsa moto Nyumba ya Mulungu, ndipo anagwetsa makoma a Yerusalemu. Anatentha moto nyumba zonse zaufumu ndipo anawononga chilichonse chimene chinali chofunika.
Og de opbrændte Guds Hus og nedbrøde Jerusalems Mure, og de opbrændte alle dens Paladser med Ild, og alle dens kostelige Kar bleve ødelagte.
20 Iye anagwira ukapolo anthu otsala amene anapulumuka ku lupanga ndi kupita nawo ku Babuloni, ndipo anakhala antchito ake ndi ana ake mpaka pamene ufumu wa Peresiya unakhazikitsidwa.
Og han bortførte til Babel dem, som vare overblevne fra Sværdet, og de bleve hans og hans Sønners Tjenere, indtil Persiens Rige fik Magten;
21 Dziko linakondwera ndi masabata ake. Pa nthawi yonse ya chipasuko chake nthaka inapuma, mpaka zaka 70 zinakwana pokwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya.
at Herrens Ord skulde opfyldes, som var talt ved Jeremias's Mund, indtil Landet havde faaet nok af sine Sabbater; det hvilede den ganske Tid, som Ødelæggelsen varede, indtil halvfjerdsindstyve Aar bleve fyldte.
22 Mʼchaka choyamba cha Koresi mfumu ya Peresiya, pofuna kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anakhudza mtima wa mfumu ya Peresiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse ndipo anazilemba:
Men i Kyrus's, Kongen af Persiens, første Aar, da Herrens Ord, som var talt ved Jeremias's Mund, var fuldkommet, opvakte Herren Kyrus's, Kongen af Persiens, Aand, at han lod udraabe over sit ganske Rige, ja kundgøre ved Skrift, og sige:
23 Chimene mfumu Koresi ya Peresiya ikunena ndi ichi: “Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa ine mafumu onse a dziko lapansi ndipo wandisankha kuti ndimumangire Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ku Yuda. Aliyense wa anthu ake pakati panu, Yehova Mulungu wake akhale naye, ndipo apite.”
Saa siger Kyrus, Kongen i Persien: Herren, Himmelens Gud, har givet mig alle Riger paa Jorden, og han har befalet mig at bygge sig et Hus i Jerusalem, som er i Juda. Hvo der maatte være iblandt eder af alle hans Folk, med ham være Herren hans Gud, og han drage op!

< 2 Mbiri 36 >