< 2 Mbiri 35 >

1 Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
و یوشیا عید فصحی در اورشلیم برای خداوند نگاه داشت، و فصح را درچهاردهم ماه اول در اورشلیم ذبح نمودند.۱
2 Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
وکاهنان را بر وظایف ایشان قرار داده، ایشان رابرای خدمت خانه خداوند قوی‌دل ساخت.۲
3 Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
وبه لاویانی که تمامی اسرائیل را تعلیم می‌دادند وبرای خداوند تقدیس شده بودند، گفت: «تابوت مقدس را در خانه‌ای که سلیمان بن داود، پادشاه اسرائیل بنا کرده است بگذارید. و دیگر بر دوش شما بار نباشد. الان به خدمت یهوه خدای خود وبه قوم او اسرائیل بپردازید.۳
4 Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
و خویشتن رابرحسب خاندانهای آبای خود و فرقه های خویش بر وفق نوشته داود، پادشاه اسرائیل ونوشته پسرش سلیمان مستعد سازید.۴
5 “Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
وبرحسب فرقه های خاندانهای آبای برادران خویش یعنی بنی قوم و موافق فرقه های خاندانهای آبای لاویان در قدس بایستید.۵
6 Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
وفصح را ذبح نمایید و خویشتن را تقدیس نموده، برای برادران خود تدارک بینید تا برحسب کلامی که خداوند به واسطه موسی گفته است عمل نمایند.»۶
7 Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
پس یوشیا به بنی قوم یعنی به همه آنانی که حاضر بودند، از گله بره‌ها و بزغاله‌ها به قدر سی هزار راس، همه آنها را به جهت قربانی های فصح داد و از گاوان سه هزار راس که همه اینها از اموال خاص پادشاه بود.۷
8 Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
و سروران او به قوم و به کاهنان و به لاویان هدایای تبرعی دادند. و حلقیاو زکریا و یحیئیل که روسای خانه خدا بودند، دوهزار و ششصد بره و سیصد گاو به جهت قربانی های فصح دادند.۸
9 Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
و کوننیا و شمعیا ونتنیئیل برادرانش و حشبا و یعیئیل و یوزاباد که روسای لاویان بودند، پنج هزار بره و پانصد گاو به لاویان به جهت قربانی های فصح دادند.۹
10 Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
پس آن خدمت مهیا شد و کاهنان درجایهای خود و لاویان در فرقه های خویش، برحسب فرمان پادشاه ایستادند.۱۰
11 Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
و فصح را ذبح کردند و کاهنان خون را از دست ایشان (گرفته )پاشیدند و لاویان پوست آنها را کندند.۱۱
12 Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
و قربانی های سوختنی را برداشتند تا آنها رابرحسب فرقه های خاندانهای آبا به پسران قوم بدهند تا ایشان آنها را برحسب آنچه در کتاب موسی نوشته بود، برای خداوند بگذرانند و باگاوان نیز چنین عمل نمودند.۱۲
13 Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
و فصح را موافق رسم به آتش پختند و هدایای مقدس را در دیگهاو پاتیلها و تابه‌ها پخته، آنها را به تمامی پسران قوم به زودی دادند.۱۳
14 Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
و بعد از آن برای خودشان و برای کاهنان مهیا ساختند زیرا که پسران هارون کهنه در گذرانیدن قربانی های سوختنی و پیه تاشام مشغول بودند. لهذا لاویان برای خودشان وبرای پسران هارون کهنه مهیا ساختند.۱۴
15 Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
ومغنیان از بنی آساف برحسب فرمان داود و آساف و هیمان و یدوتون که رایی پادشاه بود، به‌جای خود ایستادند و دربانان نزد هر دروازه و برای ایشان لازم نبود که از خدمت خود دور شوند زیراکه برادران ایشان لاویان به جهت ایشان مهیاساختند.۱۵
16 Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
پس تمامی خدمت خداوند در همان روز آماده شد تا فصح را نگاه دارند و قربانی های سوختنی را بر مذبح خداوند برحسب فرمان یوشیا پادشاه بگذرانند.۱۶
17 Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
پس بنی‌اسرائیل که حاضر بودند، در همان وقت، فصح و عید فطیر راهفت روز نگاه داشتند.۱۷
18 Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
و هیچ عید فصح مثل این از ایام سموئیل نبی در اسرائیل نگاه داشته نشده بود، و هیچ کدام از پادشاهان اسرائیل مثل این عید فصحی که یوشیا و کاهنان و لاویان وتمامی حاضران یهودا و اسرائیل و سکنه اورشلیم نگاه داشتند، نگاه نداشته بود.۱۸
19 Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
واین فصح در سال هجدهم سلطنت یوشیا واقع شد.۱۹
20 Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
بعد از همه این امور چون یوشیا هیکل راآماده کرده بود، نکو پادشاه مصر برآمد تا باکرکمیش نزد نهر فرات جنگ کند. و یوشیا به مقابله او بیرون رفت.۲۰
21 Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
و (نکو) قاصدان نزد اوفرستاده، گفت: «ای پادشاه یهودا مرا با تو چه‌کار است؟ من امروز به ضد تو نیامده‌ام بلکه به ضد خاندانی که با آن محاربه می‌نمایم. و خدامرا امر فرموده است که بشتابم. پس از آن خدایی که با من است، دست بردار مبادا تو را هلاک سازد.»۲۱
22 Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
لیکن یوشیا روی خود را از او برنگردانیدبلکه خویشتن را متنکر ساخت تا با وی جنگ کندو به کلام نکو که از جانب خدا بود گوش نگرفته، به قصد مقاتله به میدان مجدو درآمد.۲۲
23 Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
وتیراندازان بر یوشیا پادشاه تیر انداختند و پادشاه به خادمان خود گفت: «مرا بیرون برید زیرا که سخت مجروح شده‌ام.»۲۳
24 Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
پس خادمانش او را ازارابه‌اش گرفتند و بر ارابه دومین که داشت سوارکرده، به اورشلیم آوردند. پس وفات یافته، درمقبره پدران خود دفن شد، و تمامی یهودا واورشلیم برای یوشیا ماتم گرفتند.۲۴
25 Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
و ارمیا به جهت یوشیا مرثیه خواند و تمامی مغنیان ومغنیات یوشیا را در مراثی خویش تا امروز ذکرمی کنند و آن را فریضه‌ای در اسرائیل قرار دادند، چنانکه در سفر مراثی مکتوب است.۲۵
26 Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
و بقیه وقایع یوشیا و اعمال حسنه‌ای که مطابق نوشته تورات خداوند به عمل آورد،۲۶
27 zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
و امور اول وآخر او اینک در تواریخ پادشاهان اسرائیل ویهودا مکتوب است.۲۷

< 2 Mbiri 35 >