< 2 Mbiri 35 >
1 Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
Le nambena’ Iosià e Ierosalaime ao ty fihelañ’ ambone am’ Iehovà; vaho linenta amy faha-folo-efats’ ambi’ i volam-baloha’eiy i fihelañ’ amboney.
2 Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
Le nalaha’e am-pirimboñañe o mpisoroñeo, le nosihe’e amy fitoroñañe i anjomba’ Iehovàiy.
3 Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
Le hoe re amo nte-Levy mpañoke Israele iabio, o navaheñe amy Iehovào: Apoho amy anjomba’ rinanji’ i Selomò ana’ i Davidey i vata masiñey, fa tsy ho kilankañe an-tsoro’ areo eo ka, vaho toroño t’Iehovà Andrianañahare’ areo naho ondati’e Israeleo henane zao;
4 Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
le mihentseña sambe anjomban-droae, songa firimboñañe, ty amy sinoki’ i Davide mpanjaka’ Israeley naho i sinoki’ i Selomò ana’ey;
5 “Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
le mijohaña an-toe-miavake ao, songa firimboñan’ anjomban-droaen-drolongo, naho ami’ty fizarañe o anjomban-droaen-te-Levio.
6 Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
Le lentao i fihelañ’ amboney naho miavaha, le ampihentseño o longo’ areoo, hañorike i tsara’ Iehovà ampità’ i Mosèy.
7 Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
Le nitolora’ Iosià vik’ añondry naho vik’ ose amo ana’ondatio, ze teo iaby, songa hengaeñe amy fihelañ’ amboney, le telo’ ale ty hamaro’e naho añombe telo’ arivo, boak’ am-panaña’ i mpanjakay.
8 Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
Nañomey an-tsatrin’ arofo amo mpisoroñeo naho amo nte-Levio ka o roandriañeo. Le natolo’ i Kilkià naho i Zekarià vaho Iekiele, mpiaolo amy anjomban’ Añaharey amo mpisoroñeo ty ro’arivo-tsi-enenjato hisoroñañe amy fihelañ’ amboney naho añombe telon-jato.
9 Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
Nanolotse amo nte-Levio ka t’i Konanià naho i Semaia naho i Netanele, rahalahi’e naho i Kasabià naho Ieiele vaho Iozabade, mpiaolo’ o nte-Levio, ty lime-arivo hisoroñañe amy fihelañ’ amboney naho ty añombe liman-jato.
10 Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
Aa le nihalankañeñe i fitoloñañey, songa nijohañe an-toe’e eo o mpisoroñeo naho o nte-Levio, sindre firimboñañe, ty amy lili’ i mpanjakay.
11 Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
Le linenta’ iareo i vik’ añondrim-pihelañ’ amboney, le nafetsa’ o mpisoroñeo boak’ ampità’ iareo ty lio’e vaho nolire’ o nte-Levio.
12 Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
Navi’ iareo o hisoroñañeo, hanolora’ iareo amo fizaran’ anjomban-droae’ o ana’ ondatio, hañenga’ iareo am’ Iehovà ty amy misokitse am-boke’ i Mosèy. Manahake izay o añombeo.
13 Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
Natono’ iareo añ’ afo i fihelañ’ amboney ty amy fañèy fe natokoñe ambalàñe naho an-tsajoa ao vaho an-tsiliàñe o soroñe miavakeo vaho nasese’ iareo masìka amo ana’ ondatio.
14 Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
Ie nañeneke izay le nañajary ho am-bata’e naho amo mpisoroñeo; amy te nañenga o soroñeo naho i saboray pak’ amy haleñey o mpisoroñe ana’ i Aharoneo; aa le nifañalankañe ho am-bata’e naho ho amo mpisoroñe ana’ i Aharoneo o nte-Levio.
15 Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
An-toe’e eo ka o mpisabo ana’ i Asafeo, ty amy lili’ i Davide naho i Asafe naho Iedotone, mpioni’ i mpanjakay; le tsy niavota’ o mpañambeñeo ty fitoroña’ iareo amo lalambey iabio, amy te nañalankañe ho a iareo o nte-Levy longo’ iareoo.
16 Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
Aa le nihenek’ amy àndroy ty fitoroñañe am’ Iehovà, ty fañambenañe i fihelañ’ amboney naho ty fisoroñañe o engan-koroañe an-kitreli’ Iehovào, ty amy nafe’ Ioase mpanjakay.
17 Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
Le nambena’ o ana’ Israele niatreke eo tañ’andro zaio fito andro i fihelañ’ amboney naho i sabadidake mofo-po-dalivaiy.
18 Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
Le tsy teo ty fihelañ’ ambone nihajarieñe hambañ’ama’e e Israele ao boak’ añ’ andro’ i Samoele mpitoky; vaho tsy tamo mpanjaka’ Israeleo ty nahaambeñe fihelañ’ ambone manahake ty nanoe’ Ioase rekets’ o mpisoroñe naho nte-Levio naho Iehodà naho Israele iaby niatrekeo, mitraok’ amo mpimone’ Ierosalaimeo.
19 Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
Amy taom-paha-folo-valo-ambim-pifehea’ Ioasey ty nañambenañe i fihelañ’ amboney.
20 Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
Ie añe, naho fa nihajarie’ Iosia i anjombay, te nimb’eo t’i Nekò, mpanjaka’ i Mitsraime hialy e Karkemise e Peratey añe, le niavotse mb’eo t’Iosia hiatreatre.
21 Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
Fe nampihitrifa’e ìrake, nanao ty hoe: Manao inoñ’ ama’o iraho ry mpanjaka’ Iehodà? Tsy ihe ty atretrèko androany, fa i anjomba anañako aliy; vaho nandily ahy hihitrihitry mb’eo t’i Andrianañahare; aa le mifoneña tsy hitsoborea’o i Andrianañahare mpañolotse ahikoy, tsy mone harotsa’e.
22 Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
Fe tsy nimete nitolike tsy ho ama’e t’Iosia fa nañonohono vatañe hialia’e, le tsy hinao’e i saontsi’ i Nekò boak’ am-palien’ Añaharey vaho nimb’ am-bavatane’ i Megidò re hialy.
23 Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
Aa le tinifi’ o mpitàm-paleo t’Iosia mpanjaka; le hoe i mpanjakay amo mpitoro’eo; Asitaho iraho, fa vata’e fere.
24 Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
Aa le nakare’ o mpitoro’eo amy saretey vaho najo’ iareo amy sarete faharoe nindese’ey naho nasese’ iareo mb’e Ierosalaime mb’eo naho nihomake vaho nalentek’ an-kiborin-droae’e ao. Le fonga nandala aze t’Iehoda naho Ierosalaime.
25 Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
Nibeko fandalañe am’ Iosia t’Ieremià naho hene takasie’ o sakeran-dahilahio naho bekoe’ o sairy ampelao t’Iosia pak’ androany; vaho nanoa’ iareo fañè e Israele ao; oniño t’ie misokitse amo Firovetañeo.
26 Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
Aa naho o fitoloña’ Iosià ila’eo naho o fatariha’e ty amo pinatetse amy Hà’ Iehovàio
27 zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
le o tolon-draha’eo, ty valoha’e pak’ am-para’e; ingo fonga sinokitse amy bokem-panjakà’ Israele naho Iehoday.