< 2 Mbiri 35 >
1 Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
A HANA no hoi o Iosia i ka ahaaina moliaola no Iehova ma Ierusalema; a pepehi lakou i ka mohai moliaola i ka la umikumamaha o ka malama mua.
2 Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
A hoonoho oia i na kahuna ma ka lakou oihana, a hooikaika ia lakou ma ka lawelawe ana no ka hale o Iehova.
3 Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
Olelo aku la ia i na Levi, ka poe i ao aku i ka Iseraela a pau, ka poe i hoolaaia no Iehova, E hoonoho oukou i ka pahu hoano iloko o ka hale a Solomona ke keiki a Davida ke alii o ka Iseraela i kukulu ai: aole ia e lilo i mea kaumaha maluna o ko oukou mau poohiwi; e hookauwa aku oukou na Iehova, ko oukou Akua, a me ka Iseraela kona poe kanaka;
4 Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
E hoomakaukau oukou ma ko na hale o ko oukou poe kupuna ma ko oukou mau papa, e like me ka mea a Davida ke alii o ka Iseraela i kakau ai, a e like me ka mea i kakauia e Solomona kana keiki.
5 “Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
A e ku ae oukou iluna ma kahi hoano e like me ka mahele ana o na ohana kupuna o ko oukou poe hoahanau o ka ahakanaka, a e like me ka mahele ana o na ohana Levi.
6 Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
A e pepehi oukou i ka mohai moliaola, a e huikala oukou ia oukou iho. a e hoomakaukau i ko oukou poe hoahanau o hana e like me ka olelo a Iehova ma o Mose la.
7 Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
A haawi o Iosia na na kanaka i na holoholona, i na hipa keiki, a me na kao keiki, i mau mohai moliaola, no na kanaka a pau i hiki mai, he kanakolu tausani ma ka helu ana, a me na bipi ekolu tausani; a o keia mau mea no ko ke alii waiwai no ia.
8 Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
Ua haawi oluolu na alii ona i ua poe kanaka la, a i ka poe kahuna, a i na Levi; o Hilikia, a me Zekaria, a me Iehiela, ka poe luna o ka hale o ko Akua, haawi lakou na ka poe kahuna no na mohai moliaola, elua tausani eono haneri holoholona liilii, a me na bipi ekolu haneri.
9 Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
O Konania hoi a me Semaia, a me Netaneela kona mau hoahanau, a me Hasabia a me Ieiela, a me Iozabada, ka poe koikoi o na Levi, haawi lakou i na Levi, no na mohai moliaola, i elima tausani hipa, a me na bipi elima haneri.
10 Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
Pela i hoomakaukauia'i ka lawelawe ana, a ku ae la na kahuna ma ko lakou wahi, a o na Levi ma ko lakou mau papa, e like me ke kauoha a ke alii.
11 Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
Pepehi lakou i ka mohaimoliaola, a kapipi na kahuna i ke koko i loaa, mai ko lakou lima mai, a lole na Levi i ka ili.
12 Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
A lawe aku la lakou i na mohaikuni, i haawi lakou e like me ka mahele ana o na ohana kupuna o na kanaka, e mohai ia Iehova, e like me ka mea i kakauia ma ka buke a Mose; a pela lakou i hana'i i na bipi.
13 Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
A pulehu lakou i ka mohai moliaola i ke ahi e like me ke kanawai; a hoolapalapa lakou i na mea i hoanoia ma na ipu hao, a ma na ipu nui, a ma na pa, a mahele koke ae la no na kanaka a pau.
14 Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
A mahope iho, hoomakaukau lakou no lakou iho, a no na kahuna; no ka mea, o na kahuna, na keiki a Aarona, ua lilo lakou i ka mohai ana i na mohaikuni, a me na mea momona, a po ka la; no ia mea, hoomakaukau na Levi no lakou iho, a no ka poe kahuna na keiki a Aarona.
15 Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
A ma ko lakou wahi, ka poe mele, na keiki a Asapa, o lakou e like me ke kauoha a Davida, a me Asapa, a me Hemana a me ledutuna, ke kaula a ke alii; a o na mea kiaipuka, ma kela puka keia puka lakou: aole o lakou kuleana e haalele ai i ka lakou lawelawe ana; no ka mea, ua hoomakaukau ko lakou poe hoahanau, o na Levi no lakou.
16 Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
Pela i hoomakaukauia'i ka oihana a pau a Iehova ia la hookahi, e hana i ka ahaaina moliaola, e mohai aku i na mohaikuni maluna o ke kuahn o Iehova, e like me ke kauoha a Iosia ke alii.
17 Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
A o na mamo a Iseraela malaila ia wa, hana lakou i ka ahaaina moliaola, a me ka ahaaina berena hu ole i na la ehiku.
18 Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
Aole pela i hanaia'i ka ahaaina moliaola ma Iseraela, mai ka wa mai ia Samuela ke kaula mai; aole i hana na'lii a pau o ka Iseraela i ka ahaaina moliaola e like me ka mea a Iosia i hana'i, a me na kahuna, a me na Levi, a me ka Iuda a pau a me ka Iseraela i hiki mai, a me ko Ierusalema.
19 Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
I ka makahiki umikumamawalu o ke aupuni o Iosia, ua hanaia keia ahaaina moliaola.
20 Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
A mahope o keia mau mea a pau, a Iosia i hooponopono ai ma ka luakini, pii mai la o Neko ke alii o Aigupita e kaua ia Karekemisa aia no ma Euperate; a hele ku e aku o Iosia ia ia.
21 Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
A hoouna mai kela i na elele io na la, i mai la, Heaha iho nei keia o kaua, e ke alii o ka Iuda? aole au i pii mai e ku e ia oe i keia la, aka, i ko ka hale a'u e kaua aku ai. Olelo mai la ke Akua ia'u e wikiwiki. E waiho aku oe i ke Akua, eia no ia me au, o pepehi auanei ia ia oe.
22 Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
Aole i haliu ae o Iosia mai ona aku la, aka, huna oia ia ia iho, a kaua aku ia ia; aole ia i hoolohe i na olelo a Neko mai ka waha o ke Akua mai, a hele ia e kaua ma ke awawa o Megido.
23 Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
A pana mai ka poe pana kakaka i ka alii ia Iosia: a olelo ke alii i kana poe kauwa, E lawe ia'u iwaho; no ka mea, ua eha loa au.
24 Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
A lawe aku kana poe kauwa ia ia mailoko mai o kona kaakaua, a hoee lakou ia ia i ka lua o kona kaa; a lawe aku lakou ia ia i Ierusalema, a make ia, a kanuia iho la ma na ilina o kona poe kupuna: a o ka Iuda a pau a me ko Ierusalema, kanikau lakou ia Iosia.
25 Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
A kanikau o Ieremia no Iosia; a o ka poe mele kanikau a pau, ka poe kane a me ka poe wahine, olelo lakou no Iosia i ko lakou kanikau ana a hiki i keia la, a hoolilo lakou ia mau mea la i mea mau iloko o ka Iseraela; aia hoi, ua kakauia iloko o na kanikau.
26 Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
A o ke koena o na mea a Iosia i hana'i, a me kona maikai, e like me ka mea i kakauia iloko o ke kanawai o Iehova,
27 zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
A o na mea ana i haua'i, o ka mua a me ka hope, aia hoi, ua kakauia iloko o ka buke no na'lii o Iseraela a me Iuda.