< 2 Mbiri 35 >

1 Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
And Josiah kept, in Jerusalem, a passover unto Yahweh, —and they slaughtered the passover, on the fourteenth of the first month.
2 Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
And he set the priests over their charges, —and encouraged them unto the service of the house of Yahweh;
3 Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
and said to the Levites who gave instruction to all Israel as to the things which were hallowed unto Yahweh, Put the holy ark in the house which Solomon son of David king of Israel did build, it is not yours as a burden on the shoulder, —Now, serve ye Yahweh your God, and his people Israel;
4 Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
and prepare yourselves by your ancestral houses, according to your courses, —by the writing of David king of Israel, and by what hath been written by Solomon his son;
5 “Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
and stand ye in the holy place, by the divisions of the ancestral house, for your brethren, the sons of the people, and the partitioning of an ancestral house, for the Levites.
6 Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
So slaughter ye the passover, —and hallow yourselves, and prepare for your brethren, that they may do according to the word of Yahweh, by the hand of Moses.
7 Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
And Josiah presented to the sons of the people—of flocks, young sheep and the young of the goats, the whole for the passover offerings, for all present, to the number of thirty thousand, and, of bullocks, three thousand, —these, out of the substance of the king.
8 Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
And, his rulers, willingly, to the people and to the priests and to the Levites, presented, —Hilkiah and Zechariah and Jehiel, chief rulers of the house of God, unto the priests, did give, for passover offerings, two thousand and six hundred, and, of bullocks, three hundred;
9 Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
and, Conaniah, and Shemaiah and Nethanel his brethren, and Hashabiah and Jeiel and Jozabad, rulers of the Levites, presented to the Levites, for passover offerings, five thousand, and, of bullocks, five hundred.
10 Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
Thus was the service prepared, —and the priests stood in their place, and the Levites in their courses, according to the commandment of the king.
11 Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
So they slaughtered the passover, and the priests dashed [the blood received] at their hand, and the Levites were flaying [the offerings].
12 Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
Then they removed the ascending-sacrifice, that they might give them—by the divisions of each ancestral house—unto the sons of the people, to offer unto Yahweh, as it is written in the Book of Moses, —and, in like manner, with the bullocks.
13 Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
And they cooked the passover with fire, according to the regulation, —but, the hallowed things, cooked they in cauldrons and in pots and in bowls, and then took quickly, unto all the sons of the people.
14 Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
And, afterwards, prepared they for themselves and for the priests, because, the priests, the sons of Aaron, had been engaged in offering up the ascending-sacrifice and the fat pieces, until night, —the Levites, therefore prepared for themselves, and for the priests, the sons of Aaron.
15 Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
the singers also, the sons of Asaph, were in their place, according to the commandment of David, and Asaph, and Heman, and Jeduthun the seer of the king, and, the doorkeepers, were at the several doors, —there was no need for them to remove from their service, for, their brethren the Levites, prepared for them.
16 Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
Thus was all the service of Yahweh prepared on that day; to keep the passover, and to offer up the ascending-sacrifice, upon the altar of Yahweh, —according to the commandment of King Josiah.
17 Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
So the sons of Israel who were present kept the passover at that time, —and the festival of unleavened cakes, seven days.
18 Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
And there had not been kept, a passover like it, in Israel, since the days of Samuel the prophet, —yea, none of the kings of Israel, had kept such a passover as was kept by Josiah and the priests and the Levites and all Judah and Israel that were present, and the inhabitants of Jerusalem.
19 Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
In the eighteenth year of the reign of Josiah, was kept this passover.
20 Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
After all this—when Josiah had prepared the house, Neco king of Egypt came up, -to fight against Carchemish, by Euphrates, and Josiah went forth against him.
21 Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
But he sent unto him messengers, saying—What have I to do with thee, O king of Judah? not against thee, [have I come] this day, but against the house wherewith I have war, and, God, hath given word to speed me, —cease thou from [provoking] God who is with me, lest he destroy thee.
22 Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
Howbeit Josiah turned not his face from him, for, to fight against him, he had disguised himself, and he hearkened not unto the words of Neco, from the mouth of God, —so he came to fight in the valley of Megiddo.
23 Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
And the archers shot at King Josiah, —and the king said unto his servants, Take me away, for I am sore wounded.
24 Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
So his servants took him away out of the war-chariot, and conveyed him in a second chariot which he had, and carried him to Jerusalem, and he died, and was buried in the sepulchres of his fathers, —and, all Judah and Jerusalem, were mourning over Josiah.
25 Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
And Jeremiah chanted a dirge over Josiah, and all the singing men and singing women in their dirges have spoken concerning Josiah, until this day, and they appointed them by statute for Israel, —and, there they are, written among the dirges.
26 Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
But, the rest of the story of Josiah, and his lovingkindness, —according to that which is written in the law of Yahweh:
27 zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
even his story, first and last, there it is, written in the book of the Kings of Israel and Judah.

< 2 Mbiri 35 >